< 2 Mafumu 7 >

1 Ndipo Elisa anati, “Mverani mawu a Yehova. Yehova akuti, ‘Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.’”
and to say Elisha to hear: hear word LORD thus to say LORD like/as time tomorrow seah fine flour in/on/with shekel and seah barley in/on/with shekel in/on/with gate Samaria
2 Mtsogoleri amene mfumu inkamudalira anati kwa munthu wa Mulungu, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Elisa anamuyankha kuti, “Taona, iweyo udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
and to answer [the] officer which to/for king to lean upon hand his [obj] man [the] God and to say behold LORD to make window in/on/with heaven to be [the] word: thing [the] this and to say look! you to see: see in/on/with eye your and from there not to eat
3 Tsono pa chipata cholowera mu mzinda wa Samariya pankakhala anthu anayi akhate. Iwo anayankhulana kuti, “Chifukwa chiyani tikungokhala pano kudikira kufa?
and four human to be be leprous entrance [the] gate and to say man: anyone to(wards) neighbor his what? we to dwell here till to die
4 Ngati tinganene kuti, ‘Tidzalowa mu mzinda,’ njala ili mu mzindamo ndipo tidzafa. Ndipo ngati tikhalebe pano, tidzafa ndithu. Choncho tiyeni tipite ku msasa wa Aaramu ndi kukadzipereka. Ngati sakatipha, tidzakhala ndi moyo, ngati akatipha, basi tikafa.”
if to say to come (in): come [the] city and [the] famine in/on/with city and to die there and if to dwell here and to die and now to go: come! and to fall: fall to(wards) camp Syria if to live us to live and if to die us and to die
5 Iwo ananyamuka ndi kachisisira kupita ku msasa wa Aaramu. Atafika mʼmalire a msasa, taonani, sanapeze munthu ndi mmodzi yemwe,
and to arise: rise in/on/with twilight to/for to come (in): come to(wards) camp Syria and to come (in): come till end camp Syria and behold nothing there man: anyone
6 pakuti Ambuye anali atamveketsa phokoso la magaleta ndi akavalo ndiponso mdidi wa gulu lalikulu la ankhondo, kotero anayamba kuwuzana kuti, “Taonani, mfumu ya ku Israeli yalemba ganyu mafumu a Ahiti ndi a Aigupto kuti adzatithire nkhondo!”
and Lord to hear: hear [obj] camp Syria voice: sound chariot voice: sound horse voice: sound strength: soldiers great: large and to say man: anyone to(wards) brother: compatriot his behold to hire upon us king Israel [obj] king [the] Hittite and [obj] king Egypt to/for to come (in): come upon us
7 Choncho ananyamuka nathawa ndi kachisisira ndipo anasiya matenti, akavalo ndi abulu awo. Iwo anasiya msasa wawo momwe unalili nathawa kupulumutsa miyoyo yawo.
and to arise: rise and to flee in/on/with twilight and to leave: forsake [obj] tent their and [obj] horse their and [obj] donkey their [the] camp like/as as which he/she/it and to flee to(wards) soul: life their
8 Anthu akhate aja atafika mʼmalire mwa msasa analowa mʼtenti imodzi. Anadya ndi kumwa, natenga siliva, golide ndi zovala ndipo anachoka kupita kukazibisa. Atabwerera anakalowa mʼtenti ina ndipo anatenga zinthu mʼmenemo nakazibisanso.
and to come (in): come [the] be leprous [the] these till end [the] camp and to come (in): come to(wards) tent one and to eat and to drink and to lift: bear from there silver: money and gold and garment and to go: went and to hide and to return: return and to come (in): come to(wards) tent another and to lift: bear from there and to go: went and to hide
9 Kenaka akhate aja anawuzana kuti, “Ife sitikuchita bwino. Lero ndi tsiku la uthenga wabwino ndipo tikungokhala chete. Tikadikira mpaka kucha, tidzalangidwa. Tiyeni msanga tikafotokoze zimenezi ku nyumba yaufumu.”
and to say man: anyone to(wards) neighbor his not right we to make: do [the] day: today [the] this day: today good news he/she/it and we be silent and to wait till light [the] morning and to find us iniquity: punishment and now to go: come! and to come (in): come and to tell house: household [the] king
10 Choncho anapita nakayitana alonda a pa chipata cha mzinda ndi kufotokoza kuti, “Ife tinapita ku msasa wa Aaramu ndipo sitinapezeko munthu, kapena phokoso la wina aliyense koma tinangopeza akavalo okha pamodzi ndi abulu ali chimangire.”
and to come (in): come and to call: call to to(wards) gatekeeper [the] city and to tell to/for them to/for to say to come (in): come to(wards) camp Syria and behold nothing there man: anyone and voice: listen man that if: except if: except [the] horse to bind and [the] donkey to bind and tent like/as as which they(masc.)
11 Alonda a pa chipata aja analengeza uthengawu kwa okhala mʼnyumba yaufumu.
and to call: call to [the] gatekeeper and to tell house: household [the] king within
12 Mfumu inadzuka usiku ndipo inawuza atsogoleri ake a ankhondo kuti, “Ndikukuwuzani zimene Aaramu atichitira ife. Akudziwa kuti tikufa ndi njala; kotero achoka mu msasa wawo kukabisala kuthengo ndi kuti, ‘Iwowa atuluka ndithu, ndipo ife tidzawagwira amoyo ndi kulowa mu mzindamo.’”
and to arise: rise [the] king night and to say to(wards) servant/slave his to tell please to/for you [obj] which to make: do to/for us Syria to know for hungry we and to come out: come from [the] camp to/for to hide (in/on/with land: country *Q(K)*) to/for to say for to come out: come from [the] city and to capture them alive and to(wards) [the] city to come (in): come
13 Mmodzi mwa atsogoleri ake ankhondo anayankha kuti, “Chonde uzani anthu ena atenge akavalo asanu amene atsala mu mzinda muno. Taonani, zomwe zingawachitikire zidzakhala zofanana ndi zomwe zingachitikire ena onse amene atsala. Inde iwo adzangokhala ngati Aisraeli ena onse amene awonongeka kale. Choncho tiyeni tiwatume akafufuze zomwe zachitika.”
and to answer one from servant/slave his and to say and to take: take please five from [the] horse [the] to remain which to remain in/on/with her behold they like/as all (crowd *Q(K)*) Israel which to remain in/on/with her look! they like/as all crowd Israel which to finish and to send: depart and to see: see
14 Choncho anasankha magaleta awiri pamodzi ndi akavalo ake, ndipo mfumu inawatuma kuti alondole gulu lankhondo la Aaramu. Mfumuyo inalamula oyendetsa akavalowo kuti, “Pitani kaoneni.”
and to take: take two chariot horse and to send: depart [the] king after camp Syria to/for to say to go: went and to see: see
15 Anthuwa anawalondola mpaka ku Yorodani, ndipo taonani, mʼnjira monse munali zovala zokhazokha ndi zinthu zimene Aaramu ankazitaya pamene ankathawa mofulumira. Ndipo amithengawo anabwerera ndi kudzafotokozera mfumu.
and to go: follow after them till [the] Jordan and behold all [the] way: road full garment and article/utensil which to throw Syria (in/on/with to hurry they *Q(K)*) and to return: return [the] messenger and to tell to/for king
16 Tsono anthu a mu Samariya anatuluka nakafunkha ku msasa wa Aaramu. Kotero kuti makilogalamu atatu a ufa ankawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele ankawagulitsanso pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, monga momwe ananenera Yehova.
and to come out: come [the] people and to plunder [obj] camp Syria and to be seah fine flour in/on/with shekel and seah barley in/on/with shekel like/as word LORD
17 Tsono mfumu inayika mtsogoleri amene ankamudalira uja kuti akhale woyangʼanira pa chipata ndipo anthu anamupondaponda ku chipata kuja, ndipo anafa, monga momwe Elisa munthu wa Mulungu ananenera mfumu itapita ku nyumba yake.
and [the] king to reckon: overseer [obj] [the] officer which to lean upon hand: power his upon [the] gate and to trample him [the] people in/on/with gate and to die like/as as which to speak: speak man [the] God which to speak: speak in/on/with to go down [the] king to(wards) him
18 Zinachitika molingana ndi zomwe ananena munthu wa Mulungu zija kuti “Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.”
and to be like/as to speak: speak man [the] God to(wards) [the] king to/for to say seah barley in/on/with shekel and seah fine flour in/on/with shekel to be like/as time tomorrow in/on/with gate Samaria
19 Mtsogoleriyu ananena kwa munthu wa Mulungu kuti, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Munthu wa Mulungu anamuyankha kuti, “Iwe udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
and to answer [the] officer [obj] man [the] God and to say and behold LORD to make window in/on/with heaven to be like/as Chronicles [the] this and to say look! you to see: see in/on/with eye your and from there not to eat
20 Ndipo izi ndi zomwe zinamuchitikiradi mtsogoleriyu, pakuti anthu anamupondaponda pa chipata ndipo anafa.
and to be to/for him so and to trample [obj] him [the] people in/on/with gate and to die

< 2 Mafumu 7 >