< 2 Mafumu 7 >

1 Ndipo Elisa anati, “Mverani mawu a Yehova. Yehova akuti, ‘Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.’”
Da sagde Elisa: Hører Herrens Ord! saa sagde Herren: I Morgen ved denne Tid skal en Maade Mel koste en Sekel, og to Maader Byg en Sekel i Samarias Port.
2 Mtsogoleri amene mfumu inkamudalira anati kwa munthu wa Mulungu, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Elisa anamuyankha kuti, “Taona, iweyo udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
Men Høvedsmanden, til hvis Haand Kongen hældede sig, svarede den Guds Mand og sagde: Se, om Herren gjorde Vinduer paa Himmelen, mon dette Ord kunde ske? og han sagde: Se, du skal se det med dine Øjne, men ikke æde deraf.
3 Tsono pa chipata cholowera mu mzinda wa Samariya pankakhala anthu anayi akhate. Iwo anayankhulana kuti, “Chifukwa chiyani tikungokhala pano kudikira kufa?
Men der var fire spedalske Mænd, ved Indgangen til Porten, og de sagde den ene til den anden: Hvorfor blive vi her, indtil vi dø?
4 Ngati tinganene kuti, ‘Tidzalowa mu mzinda,’ njala ili mu mzindamo ndipo tidzafa. Ndipo ngati tikhalebe pano, tidzafa ndithu. Choncho tiyeni tipite ku msasa wa Aaramu ndi kukadzipereka. Ngati sakatipha, tidzakhala ndi moyo, ngati akatipha, basi tikafa.”
Om vi sige: Vi ville gaa ind i Staden, saa er der Hunger i Staden, og vi dø der, og om vi blive her, da maa vi og dø; saa kommer nu og lader os gaa over til Syrernes Lejr, lade de os leve, saa leve vi, og dræbe de os, saa dø vi.
5 Iwo ananyamuka ndi kachisisira kupita ku msasa wa Aaramu. Atafika mʼmalire a msasa, taonani, sanapeze munthu ndi mmodzi yemwe,
Og de gjorde sig rede i Tusmørket at komme til Syrernes Lejr; der de kom til det yderste af Syrernes Lejr, se, da var der ikke en Mand.
6 pakuti Ambuye anali atamveketsa phokoso la magaleta ndi akavalo ndiponso mdidi wa gulu lalikulu la ankhondo, kotero anayamba kuwuzana kuti, “Taonani, mfumu ya ku Israeli yalemba ganyu mafumu a Ahiti ndi a Aigupto kuti adzatithire nkhondo!”
Thi Herren havde ladet Syrernes Lejr høre en Lyd af Vogne og en Lyd af Heste, ja, en Lyd af en stor Hær, og de sagde, den ene til den anden: Se, Israels Konge har lejet imod os Hethiternes Konger og Ægypternes Konger til at komme over os.
7 Choncho ananyamuka nathawa ndi kachisisira ndipo anasiya matenti, akavalo ndi abulu awo. Iwo anasiya msasa wawo momwe unalili nathawa kupulumutsa miyoyo yawo.
Derfor gjorde de sig rede og flyede i Tusmørket og forlode deres Telte og deres Heste og deres Asener og Lejren, som den stod, og flyede for at redde deres Liv.
8 Anthu akhate aja atafika mʼmalire mwa msasa analowa mʼtenti imodzi. Anadya ndi kumwa, natenga siliva, golide ndi zovala ndipo anachoka kupita kukazibisa. Atabwerera anakalowa mʼtenti ina ndipo anatenga zinthu mʼmenemo nakazibisanso.
Der disse spedalske kom til det yderste af Lejren, da kom de til et Telt og aade og drak og toge derfra Sølv og Guld og Klæder og gik bort og skjulte det, og de vendte tilbage og kom til et andet Telt og toge ogsaa noget derfra og gik bort og skjulte det.
9 Kenaka akhate aja anawuzana kuti, “Ife sitikuchita bwino. Lero ndi tsiku la uthenga wabwino ndipo tikungokhala chete. Tikadikira mpaka kucha, tidzalangidwa. Tiyeni msanga tikafotokoze zimenezi ku nyumba yaufumu.”
Da sagde de, den ene til den anden: Vi gøre ikke ret, denne Dag er et godt Budskabs Dag, og skulde vi tie? dersom vi bie, indtil det bliver lys Morgen, da rammer vor Misgerning os; velan da, lader os gaa og give det til Kende for Kongens Hus!
10 Choncho anapita nakayitana alonda a pa chipata cha mzinda ndi kufotokoza kuti, “Ife tinapita ku msasa wa Aaramu ndipo sitinapezeko munthu, kapena phokoso la wina aliyense koma tinangopeza akavalo okha pamodzi ndi abulu ali chimangire.”
Og der de kom, raabte de til Stadens Portvagt, og de gave den det til Kende og sagde: Vi kom til Syrernes Lejr, og se, der var ikke en Mand eller et Menneskes Røst, men Heste bundne og Asener bundne og Teltene, saaledes som de vare.
11 Alonda a pa chipata aja analengeza uthengawu kwa okhala mʼnyumba yaufumu.
Da raabte Portvagten og forkyndte det inde i Kongens Hus!
12 Mfumu inadzuka usiku ndipo inawuza atsogoleri ake a ankhondo kuti, “Ndikukuwuzani zimene Aaramu atichitira ife. Akudziwa kuti tikufa ndi njala; kotero achoka mu msasa wawo kukabisala kuthengo ndi kuti, ‘Iwowa atuluka ndithu, ndipo ife tidzawagwira amoyo ndi kulowa mu mzindamo.’”
Og Kongen stod op om Natten og sagde til sine Tjenere: Jeg vil kundgøre eder, hvad Syrerne have gjort imod os: De vide, at vi lide Hunger, derfor ere de udgangne af Lejren for at skjule sig paa Marken, sigende: Naar de gaa ud af Staden, da ville vi gribe dem levende og komme ind i Staden.
13 Mmodzi mwa atsogoleri ake ankhondo anayankha kuti, “Chonde uzani anthu ena atenge akavalo asanu amene atsala mu mzinda muno. Taonani, zomwe zingawachitikire zidzakhala zofanana ndi zomwe zingachitikire ena onse amene atsala. Inde iwo adzangokhala ngati Aisraeli ena onse amene awonongeka kale. Choncho tiyeni tiwatume akafufuze zomwe zachitika.”
Da svarede en af hans Tjenere og sagde: Lad dem dog tage fem af Hestene, som ere tilovers, som ere overblevne herinde; se, de ere som al Israels Hob, som ere overblevne herinde, se, de ere som al Israels Hob, der er omkommen; og lader os dog sende hen og se til!
14 Choncho anasankha magaleta awiri pamodzi ndi akavalo ake, ndipo mfumu inawatuma kuti alondole gulu lankhondo la Aaramu. Mfumuyo inalamula oyendetsa akavalowo kuti, “Pitani kaoneni.”
Da toge de to Vogne med Heste, og Kongen sendte dem efter Syrernes Hær og sagde: Drager hen og ser til!
15 Anthuwa anawalondola mpaka ku Yorodani, ndipo taonani, mʼnjira monse munali zovala zokhazokha ndi zinthu zimene Aaramu ankazitaya pamene ankathawa mofulumira. Ndipo amithengawo anabwerera ndi kudzafotokozera mfumu.
Og der de droge efter dem indtil Jordanen, se, da laa hele Vejen fuld af Klæder og Tøj, som Syrerne havde kastet fra sig, der de hastede af Sted; og Budene kom igen og gave Kongen det til Kende.
16 Tsono anthu a mu Samariya anatuluka nakafunkha ku msasa wa Aaramu. Kotero kuti makilogalamu atatu a ufa ankawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele ankawagulitsanso pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, monga momwe ananenera Yehova.
Saa gik Folket ud og plyndrede Syrernes Lejr; og en Maade Mel kostede en Sekel og to Maader Byg en Sekel, efter Herrens Ord.
17 Tsono mfumu inayika mtsogoleri amene ankamudalira uja kuti akhale woyangʼanira pa chipata ndipo anthu anamupondaponda ku chipata kuja, ndipo anafa, monga momwe Elisa munthu wa Mulungu ananenera mfumu itapita ku nyumba yake.
Men Kongen beskikkede den Høvedsmand, hvis Haand han hældede sig til, til at være ved Porten, og Folket traadte ham ned i Porten, saa at han døde, ligesom den Guds Mand havde talt, som havde talt det, der Kongen kom ned til ham.
18 Zinachitika molingana ndi zomwe ananena munthu wa Mulungu zija kuti “Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.”
Thi det skete, som den Guds Mand havde talt til Kongen og sagt: I Morgen paa denne Tid skulle to Maader Byg koste en Sekel og en Maade Mel en Sekel i Samarias Port.
19 Mtsogoleriyu ananena kwa munthu wa Mulungu kuti, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Munthu wa Mulungu anamuyankha kuti, “Iwe udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
Og Høvedsmanden havde svaret den Guds Mand og sagt: Ja se, om Herren gjorde Vinduer paa Himmelen, mon det kunde ske efter dette Ord? og han havde sagt: Se, du skal se det med dine Øjne og ikke æde deraf.
20 Ndipo izi ndi zomwe zinamuchitikiradi mtsogoleriyu, pakuti anthu anamupondaponda pa chipata ndipo anafa.
Og det gik ham saaledes; thi Folket traadte ham ned i Porten, saa at han døde.

< 2 Mafumu 7 >