< 2 Mafumu 6 >
1 Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri.
and to say son: child [the] prophet to(wards) Elisha behold please [the] place which we to dwell there to/for face your narrow from us
2 Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.” Ndipo Elisa anati, “Pitani.”
to go: went please till [the] Jordan and to take: take from there man: anyone beam one and to make to/for us there place to/for to dwell there and to say to go: went
3 Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.” Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.”
and to say [the] one be willing please and to go: went with servant/slave your and to say I to go: went
4 Ndipo anapita nawo. Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo.
and to go: went with them and to come (in): come [the] Jordan [to] and to cut [the] tree
5 Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!”
and to be [the] one to fall: fell(trees) [the] beam and [obj] [the] iron to fall: fell(trees) to(wards) [the] water and to cry and to say alas! lord my and he/she/it to ask
6 Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama.
and to say man [the] God where? to fall: fall and to see: see him [obj] [the] place and to shear tree: stick and to throw there [to] and to flow [the] iron
7 Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga.
and to say to exalt to/for you and to send: reach hand his and to take: take him
8 Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.”
and king Syria to be to fight in/on/with Israel and to advise to(wards) servant/slave his to/for to say to(wards) place someone someone encampment my
9 Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.”
and to send: depart man [the] God to(wards) king Israel to/for to say to keep: careful from to pass [the] place [the] this for there Syria descended
10 Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo.
and to send: depart king Israel to(wards) [the] place which to say to/for him man [the] God (and to warn him *Q(K)*) and to keep: guard there not one and not two
11 Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?”
and to rage heart king Syria upon [the] word: because [the] this and to call: call to to(wards) servant/slave his and to say to(wards) them not to tell to/for me who? from which/that to/for us to(wards) king Israel
12 Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.”
and to say one from servant/slave his not lord my [the] king for Elisha [the] prophet which in/on/with Israel to tell to/for king Israel [obj] [the] word which to speak: speak in/on/with chamber bed your
13 Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.”
and to say to go: went and to see: see where? he/she/it and to send: depart and to take: take him and to tell to/for him to/for to say behold in/on/with Dothan
14 Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo.
and to send: depart there [to] horse and chariot and strength: soldiers heavy and to come (in): come night and to surround upon [the] city
15 Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?”
and to rise to minister man [the] God to/for to arise: rise and to come out: come and behold strength: soldiers to turn: surround [obj] [the] city and horse and chariot and to say youth his to(wards) him alas! lord my how? to make: do
16 Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.”
and to say not to fear for many which with us from whence with them
17 Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa.
and to pray Elisha and to say LORD to open please [obj] eye his and to see: see and to open LORD [obj] eye [the] youth and to see: see and behold [the] mountain: mount to fill horse and chariot fire around Elisha
18 Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa.
and to go down to(wards) him and to pray Elisha to(wards) LORD and to say to smite please [obj] [the] nation [the] this in/on/with blindness and to smite them in/on/with blindness like/as word Elisha
19 Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya.
and to say to(wards) them Elisha not this [the] way: road and not this [the] city to go: follow after me and to go: take [obj] you to(wards) [the] man which to seek [emph?] and to go: take [obj] them Samaria [to]
20 Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya.
and to be like/as to come (in): come they Samaria and to say Elisha LORD to open [obj] eye these and to see: see and to open LORD [obj] eye their and to see: see and behold in/on/with midst Samaria
21 Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?”
and to say king Israel to(wards) Elisha like/as to see: see he [obj] them to smite to smite father my
22 Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.”
and to say not to smite which to take captive in/on/with sword your and in/on/with bow your you(m. s.) to smite to set: make food: bread and water to/for face: before their and to eat and to drink and to go: went to(wards) lord their
23 Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli.
and to feed to/for them feast great: large and to eat and to drink and to send: depart them and to go: went to(wards) lord their and not to add: again still band Syria to/for to come (in): come in/on/with land: country/planet Israel
24 Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya.
and to be after so and to gather Ben-hadad Ben-hadad king Syria [obj] all camp his and to ascend: rise and to confine upon Samaria
25 Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu.
and to be famine great: large in/on/with Samaria and behold to confine upon her till to be head donkey in/on/with eighty silver: money and fourth [the] kab (quano *Q(K)*) in/on/with five silver: money
26 Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!”
and to be king Israel to pass upon [the] wall and woman to cry to(wards) him to/for to say to save [emph?] lord my [the] king
27 Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?”
and to say not to save you LORD from where? to save you from [the] threshing floor or from [the] wine
28 Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’
and to say to/for her [the] king what? to/for you and to say [the] woman [the] this to say to(wards) me to give: give [obj] son: child your and to eat him [the] day and [obj] son: child my to eat tomorrow
29 Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.”
and to boil [obj] son: child my and to eat him and to say to(wards) her in/on/with day [the] another to give: give [obj] son: child your and to eat him and to hide [obj] son: child her
30 Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli.
and to be like/as to hear: hear [the] king [obj] word [the] woman and to tear [obj] garment his and he/she/it to pass upon [the] wall and to see: see [the] people and behold [the] sackcloth upon flesh his from house: inside
31 Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!”
and to say thus to make: do to/for me God and thus to add if to stand: stand head Elisha son: child Shaphat upon him [the] day: today
32 Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?”
and Elisha to dwell in/on/with house: home his and [the] old: elder to dwell with him and to send: depart man from to/for face: before his in/on/with before to come (in): come [the] messenger to(wards) him and he/she/it to say to(wards) [the] old: elder to see: behold! for to send: depart son: warrior [the] to murder [the] this to/for to turn aside: remove [obj] head my to see: behold! like/as to come (in): come [the] messenger to shut [the] door and to oppress [obj] him in/on/with door not voice: sound foot lord his after him
33 Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”
still he to speak: speak with them and behold [the] messenger to go down to(wards) him and to say behold this [the] distress: harm from with LORD what? to wait: wait to/for LORD still