< 2 Mafumu 5 >

1 Tsono Naamani anali mtsogoleri wa gulu lankhondo a mfumu ya ku Aramu. Iye anali munthu wodalirika pamaso pa mbuye wake ndipo anali wokondedwa kwambiri, chifukwa kudzera mwa iye Yehova anapambanitsa Aaramu. Anali msilikali wolimba mtima, koma anali ndi khate.
Naaman, Konungens härhöfvitsman af Syrien, var en härlig man för sin herra, och mycket aktad; förty genom honom hade Herren gifvit salighet i Syrien; och han var en mägtig man, dock spitelsk.
2 Tsono magulu a Aaramu anapita ku nkhondo ndipo anakagwira ukapolo mtsikana wamngʼono wa ku Israeli, ndipo ankatumikira mkazi wa Naamani.
Och krigsmännerna i Syrien voro utfallne, och hade bortfört en liten pigo utur Israels land; och hon var i tjenst när Naamans hustru.
3 Mtsikanayo anawuza mkazi wa Naamani kuti, “Mbuye wanga akanapita kukaonana ndi mneneri amene amakhala ku Samariya, akanachiritsidwa khate lawo.”
Hon sade till sina fru: Ack! att min herre vore när den Propheten i Samarien, den skulle väl göra honom fri ifrå hans spitelsko.
4 Naamani anapita kwa mbuye wake kukamuwuza zomwe mtsikana wochokera ku Israeli ananena.
Då gick hon in till sin herra, och gaf honom det tillkänna, och sade: Så och så hafver den pigan af Israels land sagt.
5 Mfumu ya ku Aramu inayankha kuti, “Iwe uyenera kupita. Ine ndilembera kalata mfumu ya ku Israeli.” Choncho Naamani ananyamuka kupita ku Samariya, atatenga ndalama za siliva 30,000, ndalama zagolide 6,000 ndiponso zovala khumi za pa chikondwerero.
Konungen i Syrien sade: Så far dit, och jag vill skrifva Israels Konung ett bref till. Och han drog dit, och tog med sig tio centener silfver, och sextusend gylden, och tio högtidskläder;
6 Kalata imene anapita nayo kwa mfumu ya ku Israeli inali ndi mawu awa: “Taonani, ndikutumiza Naamani mtumiki wanga pamodzi ndi kalatayi kwa inu kuti mumuchiritse khate lake.”
Och förde brefvet till Israels Konung, och det lydde alltså: När detta bref kommer till dig, si, så vet att jag hafver sändt min tjenare Naaman till dig, att du gör honom fri ifrån hans spitelsko.
7 Mfumu ya ku Israeli itangowerenga kalatayo, inangʼamba mkanjo wake ndipo inati, “Kodi ine ndine Mulungu? Kodi ndingathe kupha kapena kupereka moyo? Chifukwa chiyani munthu ameneyu wanditumizira munthu woti ndimuchiritse khate lake? Taonani, iyeyu akungofuna kuti apeze chifukwa choyambanirana nane!”
När Israels Konung las brefvet, ref han sin kläder sönder, och sade: Är jag då Gud, att jag skulle kunna döda och lif gifva, efter han sänder till mig, att jag skall göra den mannen fri ifrå hans spitelsko? Märker och ser, huru han söker tillfälle emot mig.
8 Elisa munthu wa Mulungu atamva kuti mfumu ya ku Israeli yangʼamba mkanjo wake, anatumiza uthenga uwu: “Chifukwa chiyani mwangʼamba mkanjo wanu? Mutumizeni munthuyo kwa ine ndipo iyeyo adzadziwa kuti muli mneneri mu Israeli.”
Då Elisa den Guds mannen det hörde, att Israels Konung hade rifvit sin kläder sönder, sände han till honom, och lät säga honom: Hvi hafver du rifvit din kläder? Låt honom komma till mig, att han må förnimma att en Prophet är i Israel.
9 Choncho Naamani anapita pamodzi ndi akavalo ake ndi magaleta nakayima pa khomo la nyumba ya Elisa.
Alltså kom Naaman med hästar och vagnar, och höll för Elisa husdörr.
10 Elisa anatumiza uthenga kwa iye woti, “Pita, kasambe kasanu ndi kawiri mu mtsinje wa Yorodani, thupi lako lidzachira ndi kukhalanso monga kale ndipo udzayeretsedwa.”
Då sände Elisa ett båd till honom, och lät säga honom: Gack bort, och två dig sju resor i Jordan; och ditt kött skall komma sig till igen, och varda rent.
11 Koma Naamani anachoka mokwiya ndipo anati, “Ine ndimaganiza kuti munthuyu atuluka ndipo ayimirira nayitana dzina la Yehova Mulungu wake, nayendetsa dzanja lake pamwamba pa nthendayi ndi kundichiritsa khate langa.
Då vardt Naaman vred, och drog sina färde, och sade: Jag mente han skulle komma hitut till mig, och gå fram, och åkalla Herrans sins Guds Namn, och med sine hand taga på rummet, och så bota spitelskona.
12 Kodi Abana ndi Faripara, mitsinje ya ku Damasiko, siyoposa mitsinje ina yonse ya ku Israeli? Kodi sindikanasamba mʼmitsinje imeneyo ndi kuyeretsedwa?” Kotero anatembenuka nachoka ali wokwiya kwambiri.
Äro icke Abana och Pharphars vatten i Damascon bättre än all vatten i Israel, att jag må två mig deruti, och varda ren? Och vände sig, och for sin väg med vrede.
13 Antchito ake anamuyandikira namufunsa kuti, “Abambo anga, mneneri akanakulamulani chinthu chachikulu, kodi inu simukanachita? Nanga nʼzovuta motani zomwe mneneri wanena kuti ‘Kasambeni ndipo mudzayeretsedwa!’”
Då gingo hans tjenare till honom, och talade till honom, och sade: Min fader, om Propheten hade sagt dig något dråpeligit före, skulle du icke hafva gjort det? Huru mycket mer, medan han säger till dig: Två dig, så varder du ren?
14 Choncho Naamani anapita ku Yorodani nakadzimiza mʼmadzimo kasanu nʼkawiri, monga momwe munthu wa Mulungu anamuwuzira. Thupi lake linakhalanso monga kale ndipo linakhala losalala ngati la kamnyamata.
Då steg han af, och doppade sig i Jordan sju resor, såsom Guds mannen sagt hade; och hans kött kom till sig igen, såsom en ung drängs kött, och vardt ren.
15 Pamenepo Naamani ndi atumiki ake onse anabwerera kwa munthu wa Mulungu uja. Naamani anayima pamaso pa Elisa ndipo anati, “Tsopano ndikudziwa kuti kulibe Mulungu wina pa dziko lonse lapansi koma mu Israeli mokha. Chonde, tsopano landirani mphatso ya mtumiki wanu.”
Och han vände om igen till Guds mannen, med all sin skara. Och då han kom in, gick han fram för honom, och sade: Si, jag vet, att ingen Gud är i all land, utan i Israel; så tag nu välsignelse af dinom tjenare.
16 Mneneri anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene ine ndimamutumikira, sindidzalandira zimenezi.” Ndipo ngakhale Naamani anamukakamiza, iye anakanabe.
Men han sade: Så sant som Herren lefver, för hvilkom jag står, jag tager det icke. Och han nödgade honom, att han skulle tågat; men han ville icke.
17 Naamani anati, “Ngati inu simulandira, chonde lolani mtumiki wanu kuti atengeko dothi lokwanira kunyamula abulu awiri, popeza mtumiki wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa mulungu wina koma Yehova.
Då sade Naaman: Må då icke dinom tjenare varda gifvet en börda af denna jordene, så mycket som två mular orka bära? ty din tjenare vill icke mer androm gudom offra, och bränneoffer göra, utan Herranom;
18 Koma Yehova andikhululukire ine pa chinthu ichi: Pamene mbuye wanga alowa mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni ine ndimapita naye ndipo ndimakagwada naye limodzi. Pamene ndikugwada mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni, Yehova azikhululukira mtumiki wanu pa chinthu chimenechi.”
Att Herren ville derutinnan vara dinom tjenare nådelig, när jag tillbeder i Rimmons hus, när min herre går uti Rimmons hus till att tillbedja der, och han stödjer sig vid mina hand.
19 Elisa anati, “Pita mu mtendere.” Choncho anachoka nayenda pangʼono.
Han sade till honom: Far i frid. Och han for ifrå honom ett litet stycke vägs på markene.
20 Koma Gehazi, mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu, anaganiza mu mtima mwake kuti, “Taonani, mbuye wanga wamulekerera Naamani Mwaramuyu, posalandira zomwe anabweretsa. Pali Yehova wamoyo, ine ndimuthamangira ndipo ndikatengako zinthu kwa iye.”
Då tänkte Gehasi, Gudsmannens Elisa tjenare: Si, min herre hafver spart denna Syren Naaman, så att han intet hafver tagit af honom, det han hit hade; så sant som Herren lefver, jag vill löpa efter honom, och taga något af honom.
21 Choncho Gehazi anamuthamangira Naamani uja. Naamani ataona Gehazi akumuthamangira, anatsika mʼgaleta lake ndi kukakumana naye. Iye anafunsa Gehazi kuti, “Kodi nʼkwabwino?”
Alltså jagade Gehasi efter Naaman; och då Naaman såg, att han lopp efter honom, steg han af vagnen emot honom, och sade: Går det väl till?
22 Gehazi anayankha kuti, “Inde nʼkwabwino. Mbuye wanga wandituma kuti ndidzakuwuzeni kuti, ‘Anyamata awiri mwa ana a aneneri angondipeza kumene kuchokera ku dziko la mapiri la Efereimu. Chonde apatseniko ndalama za siliva 3,000 ndi zovala ziwiri za pa phwando.’”
Han sade: Ja; men min herre hafver sändt mig, och låter dig säga: Si, nu på stundene äro till mig komne ifrå Ephraims berg två unga män utaf de Propheters söner. Gif dem en centener silfver, och tu högtidskläder.
23 Naamani anati, “Kuli bwino utenge ndalama zasiliva 6,000.” Iye anakakamiza Gehazi kuti alandire, ndipo kenaka anamanga matumba awiri a ndalama zasiliva pamodzi ndi zovala zinayi za pa mphwando. Naamani anazipereka kwa antchito ake awiri ndipo anazinyamula nayenda patsogolo pa Gehazi.
Naaman sade: Gerna; tag två centener. Och han nödgade honom, och band två centener silfver i två säcker, och tu högtidskläder, och fick det två sina tjenare; och de båro det med honom.
24 Gehazi atafika ku phiri, anawalanda antchito aja zinthu zija nazibisa mʼnyumbamo. Iye anawawuza anthu aja kuti abwerere ndipo anapita.
Och då han kom till mörkt rum, tog han det utaf deras händer, och lade det öfver en sido i huset, och lät männerna gå; och de gingo bort.
25 Kenaka analowa mʼnyumbamo nakayima pamaso pa mbuye wake Elisa. Elisa anafunsa kuti, “Kodi Gehazi unali kuti?” Iye anayankha kuti, “Mtumiki wanu sanapite kwina kulikonse.”
Då gick han fram för sin herra. Och Elisa sade till honom: Hvadan kommer du, Gehasi? Han sade: Din tjenare hafver hvarken hit eller dit gångit.
26 Koma Elisa anati kwa Gehazi, “Kodi mzimu wanga sunali nawe pamene munthu uja anatsika mʼgaleta lake ndi kukumana nawe? Kodi ino ndi nthawi yolandira ndalama, kapena kulandira zovala, mitengo ya olivi, minda ya mpesa, nkhosa, ngʼombe kapena antchito aamuna kapena antchito aakazi?
Han sade till honom: Månde icke mitt hjerta vandra med dig, då mannen vände om igen ifrå sin vagn emot dig? Nu, du hafver tagit silfver och kläder, oljogårdar, vingårdar, får, oxar, tjenare och tjenarinnor.
27 Khate la Naamani lidzakumatirira iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.” Ndipo Gehazi anachoka pamaso pa Elisa ali ndi khate lotuwa ngati phulusa.
Men Naamans spitelska skall låda vid dig, och dina säd, till evig tid. Så gick han ut ifrå honom spitelsker såsom en snö.

< 2 Mafumu 5 >