< 2 Mafumu 5 >

1 Tsono Naamani anali mtsogoleri wa gulu lankhondo a mfumu ya ku Aramu. Iye anali munthu wodalirika pamaso pa mbuye wake ndipo anali wokondedwa kwambiri, chifukwa kudzera mwa iye Yehova anapambanitsa Aaramu. Anali msilikali wolimba mtima, koma anali ndi khate.
Náman hejtman vojska krále Syrského, jsa muž veliký u pána svého, a osoba vzácná, skrze něho zajisté dal Hospodin vysvobození zemi Syrské, ten, pravím, muž tak udatný byl malomocný.
2 Tsono magulu a Aaramu anapita ku nkhondo ndipo anakagwira ukapolo mtsikana wamngʼono wa ku Israeli, ndipo ankatumikira mkazi wa Naamani.
Byli pak vyšli z země Syrské lotříkové, kteříž zajali z země Izraelské děvečku malou, a ta sloužila manželce Námanově.
3 Mtsikanayo anawuza mkazi wa Naamani kuti, “Mbuye wanga akanapita kukaonana ndi mneneri amene amakhala ku Samariya, akanachiritsidwa khate lawo.”
Kteráž řekla paní své: Ó by pán můj dostal se k proroku, kterýž jest v Samaří, tedy on by ho uzdravil od malomocenství jeho.
4 Naamani anapita kwa mbuye wake kukamuwuza zomwe mtsikana wochokera ku Israeli ananena.
A on všed, oznámil pánu svému, řka: Takto a takto pravila děvečka, kteráž jest z země Izraelské.
5 Mfumu ya ku Aramu inayankha kuti, “Iwe uyenera kupita. Ine ndilembera kalata mfumu ya ku Israeli.” Choncho Naamani ananyamuka kupita ku Samariya, atatenga ndalama za siliva 30,000, ndalama zagolide 6,000 ndiponso zovala khumi za pa chikondwerero.
Tedy řekl král Syrský: Jdi, vyprav se, a já pošli list králi Izraelskému. A odcházeje, vzal s sebou deset centnéřů stříbra a šest tisíců zlatých, nad to desatero roucho proměnné.
6 Kalata imene anapita nayo kwa mfumu ya ku Israeli inali ndi mawu awa: “Taonani, ndikutumiza Naamani mtumiki wanga pamodzi ndi kalatayi kwa inu kuti mumuchiritse khate lake.”
I přinesl list králi Izraelskému v tato slova: Hned, jakž tě dojde list tento, aj, poslal jsem k tobě Námana služebníka svého, abys ho uzdravil od malomocenství jeho.
7 Mfumu ya ku Israeli itangowerenga kalatayo, inangʼamba mkanjo wake ndipo inati, “Kodi ine ndine Mulungu? Kodi ndingathe kupha kapena kupereka moyo? Chifukwa chiyani munthu ameneyu wanditumizira munthu woti ndimuchiritse khate lake? Taonani, iyeyu akungofuna kuti apeze chifukwa choyambanirana nane!”
I stalo se, že když přečetl král Izraelský ten list, roztrhl roucho své a řekl: Zdali jsem já Bohem, abych mohl umrtviti a obživiti, že tento poslal ke mně, abych uzdravil muže od malomocenství jeho? Nýbrž posuďte, prosím, a pohleďte, že příčiny hledá proti mně.
8 Elisa munthu wa Mulungu atamva kuti mfumu ya ku Israeli yangʼamba mkanjo wake, anatumiza uthenga uwu: “Chifukwa chiyani mwangʼamba mkanjo wanu? Mutumizeni munthuyo kwa ine ndipo iyeyo adzadziwa kuti muli mneneri mu Israeli.”
A když uslyšel Elizeus muž Boží, že roztrhl král Izraelský roucho své, poslal k králi, řka: Proč jsi roztrhl roucho své? Nechť nyní přijde ke mně a zvíť, že jest prorok v Izraeli.
9 Choncho Naamani anapita pamodzi ndi akavalo ake ndi magaleta nakayima pa khomo la nyumba ya Elisa.
A tak přibral se Náman s jízdou svou a s vozy svými, a stál u dveří domu Elizeova.
10 Elisa anatumiza uthenga kwa iye woti, “Pita, kasambe kasanu ndi kawiri mu mtsinje wa Yorodani, thupi lako lidzachira ndi kukhalanso monga kale ndipo udzayeretsedwa.”
Poslal pak k němu Elizeus posla, řka: Jdi a umej se sedmkrát v Jordáně, a uzdraveno bude tělo tvé, a čist budeš.
11 Koma Naamani anachoka mokwiya ndipo anati, “Ine ndimaganiza kuti munthuyu atuluka ndipo ayimirira nayitana dzina la Yehova Mulungu wake, nayendetsa dzanja lake pamwamba pa nthendayi ndi kundichiritsa khate langa.
Tedy rozhněvav se Náman, bral se odtud a mluvil: Hle, řekl jsem u sebe, že jistotně vyjde, a stoje, vzývati bude jméno Hospodina Boha svého, a vznášeje ruku svou nad místem neduživým, tak uzdraví malomocenství mé.
12 Kodi Abana ndi Faripara, mitsinje ya ku Damasiko, siyoposa mitsinje ina yonse ya ku Israeli? Kodi sindikanasamba mʼmitsinje imeneyo ndi kuyeretsedwa?” Kotero anatembenuka nachoka ali wokwiya kwambiri.
Zdali nejsou lepší Abana a Farfar, řeky Damašské, nad všecky vody Izraelské? Zdaliž bych se nemohl v nich zmýti, abych čist byl? A obrátiv se, jel s hněvem.
13 Antchito ake anamuyandikira namufunsa kuti, “Abambo anga, mneneri akanakulamulani chinthu chachikulu, kodi inu simukanachita? Nanga nʼzovuta motani zomwe mneneri wanena kuti ‘Kasambeni ndipo mudzayeretsedwa!’”
Ale přistoupivše služebníci jeho, mluvili k němu a řekli: Otče můj, jakkoli velikou věc prorok ten rozkázal by tobě, což bys neměl učiniti toho? Èím tedy více, kdyžť řekl: Umej se, a budeš čist.
14 Choncho Naamani anapita ku Yorodani nakadzimiza mʼmadzimo kasanu nʼkawiri, monga momwe munthu wa Mulungu anamuwuzira. Thupi lake linakhalanso monga kale ndipo linakhala losalala ngati la kamnyamata.
A protož sstoupiv, pohřížil se v Jordáně sedmkrát vedlé řeči muže Božího. I učiněno jest tělo jeho jako tělo dítěte malého, a očištěn jest.
15 Pamenepo Naamani ndi atumiki ake onse anabwerera kwa munthu wa Mulungu uja. Naamani anayima pamaso pa Elisa ndipo anati, “Tsopano ndikudziwa kuti kulibe Mulungu wina pa dziko lonse lapansi koma mu Israeli mokha. Chonde, tsopano landirani mphatso ya mtumiki wanu.”
A hned navrátil se k muži Božímu se vším komonstvem svým, a přišed, stál před ním a řekl: Aj, již jsem poznal, žeť není Boha na vší zemi, jediné v Izraeli. Protož nyní vezmi, prosím, dary tyto od služebníka svého.
16 Mneneri anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene ine ndimamutumikira, sindidzalandira zimenezi.” Ndipo ngakhale Naamani anamukakamiza, iye anakanabe.
On pak řekl: Živť jest Hospodin, před jehož oblíčejem stojím, žeť nic nevezmu. A ač ho nutil, aby vzal, však nikoli nechtěl.
17 Naamani anati, “Ngati inu simulandira, chonde lolani mtumiki wanu kuti atengeko dothi lokwanira kunyamula abulu awiri, popeza mtumiki wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa mulungu wina koma Yehova.
I řekl Náman: Tedy nic? Ale nechť jest dáno, prosím, mně služebníku tvému břímě země na dva mezky; neboť nebude více obětovati služebník tvůj zápalů aneb obětí bohům cizím, ale Hospodinu.
18 Koma Yehova andikhululukire ine pa chinthu ichi: Pamene mbuye wanga alowa mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni ine ndimapita naye ndipo ndimakagwada naye limodzi. Pamene ndikugwada mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni, Yehova azikhululukira mtumiki wanu pa chinthu chimenechi.”
V této však věci odpusť Hospodin služebníku tvému: Když vchází pán můj do chrámu Remmon, aby se tam modlil, a on podpírá se na mou ruku, že i já skláním se v chrámě Remmon. Toho sklánění mého v chrámě Remmon nechť neváží, prosím, Hospodin služebníku tvému při té věci.
19 Elisa anati, “Pita mu mtendere.” Choncho anachoka nayenda pangʼono.
I řekl jemu: Jdi v pokoji. A když odjel od něho nedaleko,
20 Koma Gehazi, mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu, anaganiza mu mtima mwake kuti, “Taonani, mbuye wanga wamulekerera Naamani Mwaramuyu, posalandira zomwe anabweretsa. Pali Yehova wamoyo, ine ndimuthamangira ndipo ndikatengako zinthu kwa iye.”
V tom řekl Gézi služebník Elizea muže Božího: Hle, nedopustil pán můj Námanovi Syrskému tomuto, aby dáti měl z ruky své to, což přivezl. Živť jest Hospodin, žeť poběhnu za ním, a vezmu něco od něho.
21 Choncho Gehazi anamuthamangira Naamani uja. Naamani ataona Gehazi akumuthamangira, anatsika mʼgaleta lake ndi kukakumana naye. Iye anafunsa Gehazi kuti, “Kodi nʼkwabwino?”
Protož běžel Gézi za Námanem. A vida Náman běžícího za sebou, rychle skočil s vozu vstříc jemu a řekl: Dobře-li se děje?
22 Gehazi anayankha kuti, “Inde nʼkwabwino. Mbuye wanga wandituma kuti ndidzakuwuzeni kuti, ‘Anyamata awiri mwa ana a aneneri angondipeza kumene kuchokera ku dziko la mapiri la Efereimu. Chonde apatseniko ndalama za siliva 3,000 ndi zovala ziwiri za pa phwando.’”
A on odpověděl: Dobře. Pán můj poslal mne, aťbych řekl: Aj, teď nyní přišli ke mně dva mládenci s hory Efraim z synů prorockých; dej jim medle centnéř stříbra a dvoje roucho proměnné.
23 Naamani anati, “Kuli bwino utenge ndalama zasiliva 6,000.” Iye anakakamiza Gehazi kuti alandire, ndipo kenaka anamanga matumba awiri a ndalama zasiliva pamodzi ndi zovala zinayi za pa mphwando. Naamani anazipereka kwa antchito ake awiri ndipo anazinyamula nayenda patsogolo pa Gehazi.
I řekl Náman: Raději vezmi dva centnéře. I přinutil ho. A svázav dva centnéře stříbra do dvou pytlů, a dvoje roucho proměnné, vložil to na dva pacholky své, kteříž nesli před ním.
24 Gehazi atafika ku phiri, anawalanda antchito aja zinthu zija nazibisa mʼnyumbamo. Iye anawawuza anthu aja kuti abwerere ndipo anapita.
A když přišel na vrch, vzal to z rukou jejich, a složil v jednom domě, propustiv muže ty, kteřížto odešli.
25 Kenaka analowa mʼnyumbamo nakayima pamaso pa mbuye wake Elisa. Elisa anafunsa kuti, “Kodi Gehazi unali kuti?” Iye anayankha kuti, “Mtumiki wanu sanapite kwina kulikonse.”
Sám pak všed, stál před pánem svým. I řekl mu Elizeus: Odkudžto, Gézi? Odpověděl: Nechodil služebník tvůj nikam.
26 Koma Elisa anati kwa Gehazi, “Kodi mzimu wanga sunali nawe pamene munthu uja anatsika mʼgaleta lake ndi kukumana nawe? Kodi ino ndi nthawi yolandira ndalama, kapena kulandira zovala, mitengo ya olivi, minda ya mpesa, nkhosa, ngʼombe kapena antchito aamuna kapena antchito aakazi?
Kterýž řekl jemu: Zdaliž srdce mé nebylo při tom, když obrátil se muž s vozu svého vstříc tobě? Zdaliž čas byl bráti stříbro aneb roucho, aneb olivoví a vinice, aneb stáda a voly, neb služebníky aneb děvky?
27 Khate la Naamani lidzakumatirira iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.” Ndipo Gehazi anachoka pamaso pa Elisa ali ndi khate lotuwa ngati phulusa.
Protož malomocenství Námanovo přichytí se tebe i semene tvého na věky. I vyšel od tváři jeho malomocný jako sníh.

< 2 Mafumu 5 >