< 2 Mafumu 4 >
1 Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”
А одна з жінок пророчих синів кли́кала до Єлисей, говорячи: „Помер раб твій, мій чоловік! А ти знаєш, що раб твій боявся Господа. А позича́льник прийшов ось, щоб забрати собі двоє дітей моїх за рабів“.
2 Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?” Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”
І сказав до неї Єлисей: „Що́ я зроблю тобі? Розкажи мені, що́ є в тебе в домі“. А та відказала: „Нічого нема в домі твоєї невільниці, — є тільки горня́ оливи“.
3 Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa.
А він сказав: „Іди, позич собі настороні́ по́суд від усіх сусі́док твоїх, по́суд порожній. Не бери мало!
4 Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”
І вві́йдеш, і замкне́ш двері за собою та за синами своїми, і поналива́єш у всі ті посу́дини, а повні повідставля́й“.
5 Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta.
І пішла вона від нього, і замкну́ла двері за собою та за синами своїми. Вони подава́ли їй по́суд, а вона налива́ла.
6 Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.” Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.
І сталося, коли понапо́внювано по́суд, то сказала вона до сина свого: „Подай мені ще по́суду!“А він відказав їй: „Нема вже по́суду“. І спини́лася олива.
7 Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”
І вона прийшла, і доне́сла Божому чоловікові. І він сказав: „Іди, продай ту оливу, та й заплати своєму позича́льникові. А ти та сини́ твої будете жити на позоста́ле“.
8 Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya.
І сталося певного дня, і прийшов Єлисе́й до Шуна́му, а там була багата жінка, — і вона сильно просила його до себе поїсти хліба. І бувало, скільки разів прихо́див він, захо́див туди їсти хліб.
9 Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu.
І сказала вона до чоловіка свого: „Ось я познала, що Божий чоловік, який за́вжди прихо́дить до нас, він святий.
10 Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”
Зробім же малу муровану го́рницю, і поставимо йому там ліжко, і стола, і стільця́, і свічника́. І коли він прихо́дитиме до нас, то захо́дитиме туди“.
11 Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo.
Одно́го ра́зу прийшов він туди, і зайшов до горниці та й ліг там.
12 Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa.
І сказав він до свого слуги Ґехазі: „Поклич оцю шунамі́тянку!“І той покли́кав її, і вона стала перед ним.
13 Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’” Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”
І сказав він до нього: „Скажи їй: Ось ти старанно піклува́лася про всі наші потреби. Що́ зробити тобі за це! Чи є що, щоб сказати про тебе цареві або начальникові війська?“А вона відказала: „ Ні, — я сиджу́ серед народу свого!“
14 Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?” Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”
І сказав він: „Що́ ж зробити їй?“А Ґехазі відказав: „Та вона не має сина, а чоловік її стари́й“.
15 Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo.
А він сказав: „Поклич її“. І він покликав її, і вона стала при вході.
16 Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.” Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”
І він сказав: „На цей озна́чений час, коли саме цей час ве́рнеться, ти обійма́тимеш сина!“А вона відказала: „Ні, пане, чоловіче Божий, не говори неправди своїй невільниці!“
17 Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.
Та зачала́ та жінка, і породи́ла сина на той озна́чений час, того саме ча́су, про який говорив до неї Єлисей.
18 Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu.
І росло те дитя. А одно́го ра́зу вийшло воно до свого́ ба́тька до женці́в.
19 Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!” Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.”
І сказало воно до свого батька: „Голова моя, голова моя!“А той сказав слузі: „Занеси́ його до його матері!“
20 Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira.
І той поніс його, і приніс його до його матері. І сиділо воно на її колінах аж до полу́дня, та й померло...
21 Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.
І ввійшла вона, і поклала його на ліжко Божого чоловіка, і замкну́ла за ним двері та й вийшла.
22 Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”
І покликала вона свого чоловіка та й сказала: „Пришли мені одно́го із слуг та одну з ослиць, і я поїду до Божого чоловіка й вернуся“.
23 Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
А він сказав: „Чому ти їдеш до нього? Сьогодні не новомісяччя й не субота“. А вона відказала: „Добре!“
24 Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.”
І осідла́ла вона ослицю, і сказала до свого слуги: „Поганяй та йди. Не затримуй мені в їзді, аж поки не скажу́ тобі“.
25 Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli. Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo!
І поїхала вона, і приїхала до Божого чоловіка, до гори Карме́л. І сталося, як Божий чоловік побачив її зда́лека, то сказав до слуги свого Ґехазі: „Ось та шунамі́тянка!
26 Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
Побіжи ж назу́стріч їй та й скажи їй: Чи все гара́зд тобі, чи гаразд чоловікові твоєму, чи гаразд дитині?“А та відказала: „Усе гаразді“
27 Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”
І прийшла вона до Божого чоловіка на го́ру, і сильно схопи́ла за но́ги його. А Ґехазі підійшов, щоб відіпхну́ти її, та Божий чоловік сказав: „Позостав її, бо затурбо́вана душа її, а Господь затаїв це передо мною й не сказав мені“.
28 Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”
А вона сказала: „Чи я жадала сина від пана? Чи я не говорила: Не впрова́джуй мене в обма́ну?“
29 Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”
І він сказав до Ґехазі: „Опережи сте́гна свої, і візьми мою па́лицю в руку свою та й іди. Коли спітка́єш кого, не повітаєш його, а коли хто повітає тебе, не відповіси́ йому. І покладеш мою палицю на хло́пцеве обличчя“.
30 Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.
А мати того хлопця сказала: „ Як живий Господь і жива душа твоя, — я не полишу́ тебе!“І він устав і пішов за нею.
31 Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”
А Ґехазі пішов перед ними, і поклав ту палицю на хлопцеве обличчя, та не було ані голосу, ані чуття. І вернувся він навпроти нього, і доніс йому, говорячи: „Не збуди́вся той хлопець!“
32 Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake.
І ввійшов Єлисей у дім, аж ось той хлопець лежить мертвий на ліжку його!
33 Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova.
І ввійшов він, і замкнув двері за ними обома́, та й молився до Господа.
34 Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda.
І ввійшов він, і ліг на того хло́пця, і поклав уста свої на уста його, а очі свої на очі його, і долоні свої на долоні його. І схилився над ним, і стало тепле тіло тієї дитини!...
35 Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.
І він зно́ву ходив по дому раз сюди́, а раз туди́. І ввійшов він, і знову схилився над ним, — і чхнув той хлопець аж до семи раз. І розплю́щив той хлопець очі свої.
36 Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.”
І покликав він Ґехазі та й сказав: „Поклич ту шунамі́тянку!“І той покликав її. І прийшла вона до нього, і він сказав: „Забери свого сина!“
37 Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.
І ввійшла вона, і впала до його ніг, і вклони́лася до землі. І взяла́ вона сина свого та й вийшла...
38 Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”
І вернувся Єлисей до Ґілґалу. А в Краю́ був голод, і пророчі сини сиділи перед ним. І сказав він до свого хлопця: „Пристав великого горшка́, і звари їжу для пророчих синів“.
39 Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa.
І вийшов один на поле, щоб назбирати ярини́, і знайшов там витку́ рослину, і назбирав із неї повну свою одежу диких огіркі́в. І він прийшов, і накриши́в до горшка́ ї́жі, бо вони не знали того́.
40 Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.
І поналива́ли вони лю́дям їжі. І сталося, як вони їли ту їжу, то закричали й сказали: „Смерть у горшку, чоловіче Божий!“І не могли вони їсти...
41 Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.
А він сказав: „Дайте муки́!“І він всипав її до горшка і сказав: „Наливай наро́дові, і нехай їдять!“І вже не було́ нічого злого в горшку́.
42 Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”
І прийшов один чоловік із Баал-Шалішу, і приніс Божому чоловікові хліб первопло́ду, — двадцять ячмінних хлібці́в та зе́рна в колоска́х у своїй торбі. І сказав Єлисе́й: „Дай наро́дові, і нехай вони їдять!“
43 Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?” Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’”
А слуга його сказав: „Що оце покладу я перед сотнею чоловіка?“Та він відказав: „Дай наро́дові, і нехай їдять, бо так сказав Господь: їжте й позоставте!“
44 Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.
І він поклав перед ними, і вони їли й позоставили, за словом Господнім.