< 2 Mafumu 3 >
1 Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
Joram, Ahabs son, blev konung över Israel i Samaria i Josafats, Juda konungs, adertonde regeringsår, och han regerade i tolv år.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
Han gjorde vad ont var i HERRENS ögon; dock icke såsom hans fader och moder, ty han skaffade bort den Baalsstod som hans fader hade låtit göra.
3 Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
Dock höll han fast vid de Jerobeams, Nebats sons, synder genom vilka denne hade kommit Israel att synda; från dessa avstod han icke.
4 Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
Mesa, konungen i Moab, som ägde mycken boskap, hade i skatt till konungen i Israel erlagt hundra tusen lamm och ull av hundra tusen vädurar.
5 Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
Men när Ahab var död, avföll konungen i Moab från konungen i Israel.
6 Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
Då drog konung Joram ut från Samaria och mönstrade hela Israel.
7 Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
Därefter sände han åstad bud till Josafat, konungen i Juda, och lät säga honom: "Konungen i Moab har avfallit från mig. Vill du draga med mig för att strida mot Moab?" Han svarade: "Ja, jag vill draga ditupp -- jag såsom du, mitt folk såsom ditt folk, mina hästar såsom dina hästar!"
8 Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
Och han frågade: "Vilken väg skola vi draga ditupp?" Han svarade "Vägen genom Edoms öken."
9 Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
Så drogo då konungen i Israel konungen i Juda och konungen i Edom åstad; men när de hade färdats sju dagsresor, fanns intet vatten för hären och för djuren som de hade med sig.
10 Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
Då sade Israels konung: "Ack att HERREN skulle kalla tillhopa dessa tre konungar för att giva dem i Moabs hand!"
11 Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
Men Josafat sade: "Finnes här ingen HERRENS profet, så att vi kunna fråga HERREN genom honom?" Då svarade en av Israels konungs tjänare och sade: "Elisa, Safats son, finnes här, han som plägade gjuta vatten på Elias händer."
12 Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
Josafat sade: "Hos honom är HERRENS ord." Israels konung och Josafat och Edoms konung gingo då ned till honom.
13 Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
Men Elisa sade till Israels konung: "Vad har du med mig att göra? Gå du till din faders profeter och till din moders profeter." Israels konung svarade honom: "Bort det, att HERREN skulle hava kallat tillhopa dessa tre konungar för att giva dem i Moabs hand!"
14 Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
Då sade Elisa: "Så sant HERREN Sebaot lever, han vilkens tjänare jag är: om jag icke hade undseende för Josafat, Juda konung, så skulle jag icke akta på dig eller se till dig.
15 Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
Men hämten nu hit åt mig en harpospelare." Så ofta harpospelaren spelade, kom nämligen HERRENS hand över honom.
16 ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
Och han sade: "Så säger HERREN: Gräven i denna dal grop vid grop.
17 Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
Ty så säger HERREN: I skolen icke märka någon vind, ej heller se något regn, men likväl skall denna dal bliva full med vatten, så att både I själva skolen hava att dricka och eder boskap och edra övriga djur.
18 Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
Dock anser HERREN icke ens detta vara nog, utan han vill ock giva Moab i eder hand.
19 Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
Och I skolen intaga alla befästa städer och alla andra ansenliga städer, I skolen fälla alla nyttiga träd och kasta igen alla vattenkällor, och alla bördiga åkerstycken skolen I fördärva med stenar."
20 Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
Och se, om morgonen, vid den tid då spisoffret frambäres, strömmade vatten till från Edomssidan, så att landet fylldes med vatten.
21 Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
Moabiterna hade nu allasammans hört att konungarna hade dragit upp för att strida mot dem, och alla de som voro vid vapenför ålder eller därutöver blevo uppbådade och stodo nu vid gränsen.
22 Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
Men bittida om morgonen, när solen gick upp och lyste på vattnet, sågo moabiterna vattnet framför sig rött såsom blod.
23 Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
Då sade de: "Det är blod! Konungarna hava helt visst råkat i strid och därvid dräpt varandra. Nu till plundring, Moab!"
24 Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
Men när de kommo till Israels läger, bröto israeliterna fram och slogo moabiterna, så att de flydde för dem. Och de drogo in i landet och slogo ytterligare moabiterna.
25 Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
Och städerna förstörde de, och på alla bördiga åkerstycken kastade de var och en sin sten, till dess de hade överhöljt dem, och alla vattenkällor täppte de till, och alla nyttiga träd fällde de, så att de till slut lämnade kvar allenast stenarna av Kir-Hareset. Men när slungkastarna omringade staden och besköto den
26 Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
och Moabs konung såg att han icke kunde hålla stånd i striden, tog han med sig sju hundra svärdbeväpnade män för att slå sig igenom till Edoms konung; men de kunde det icke.
27 Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.
Då tog han sin förstfödde son, den som skulle bliva konung efter honom, och offrade denne på muren till ett brännoffer. Då drabbades Israel av svår hemsökelse, så att de måste bryta upp och lämna honom i fred och vända tillbaka till sitt land igen.