< 2 Mafumu 3 >

1 Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
Or la dix-huitième année de Josaphat Roi de Juda, Joram fils d'Achab avait commencé à régner sur Israël en Samarie, et il régna douze ans.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
Et fit ce qui déplaît à l'Eternel, non pas toutefois comme [avaient fait] son père et sa mère, car il ôta la statue de Bahal que son père avait faite.
3 Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
Mais il adhéra aux péchés de Jéroboam fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël, [et] ne se détourna point d'aucun d'eux.
4 Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
Or Mésah, Roi de Moab, se mêlait de bétail, et payait au Roi d'Israël cent mille agneaux, et cent mille moutons [portant] laine.
5 Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
Mais aussitôt qu'Achab fut mort, il arriva que le Roi de Moab se rebella contre le Roi d'Israël.
6 Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
C'est pourquoi le Roi Joram sortit ce jour-là de Samarie, et dénombra tout Israël.
7 Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
Puis il alla, et envoya vers Josaphat Roi de Juda, pour lui dire: Le Roi de Moab s'est rebellé contre moi, ne viendras-tu pas avec moi à la guerre contre Moab? et il répondit: J'y monterai; fais ton compte de moi comme de toi, de mon peuple comme de ton peuple, et de mes chevaux comme de tes chevaux.
8 Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
Ensuite il dit: Par quel chemin monterons-nous? Et il répondit: Par le chemin du désert d'Edom.
9 Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
Ainsi le Roi d'Israël, et le Roi de Juda, et le Roi d'Edom partirent, et tournoyèrent par le chemin durant sept jours, jusqu'à ce qu'ils n'eurent plus d'eau pour le camp, ni pour les bêtes qu'ils menaient.
10 Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
Et le Roi d'Israël dit: Ha! Ha! certainement l'Eternel a appelé ces trois Rois pour les livrer entre les mains de Moab.
11 Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
Et Josaphat dit: N'y a-t-il point ici quelque Prophète de l'Eternel, afin que par son moyen nous consultions l'Eternel? Et un des serviteurs du Roi d'Israël répondit, et dit: Il y a ici Elisée fils de Saphat, qui versait de l'eau sur les mains d'Elie.
12 Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
Alors Josaphat dit: La parole de l'Eternel est avec lui; et le Roi d'Israël, et Josaphat, et le Roi d'Edom descendirent vers lui.
13 Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
Mais Elisée dit au Roi d'Israël: Qu'y a-t-il entre moi et toi? va-t'en vers les prophètes de ton père, et vers les prophètes de ta mère. Et le Roi d'Israël lui répondit: Non; car l'Eternel a appelé ces trois Rois pour les livrer entre les mains de Moab.
14 Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
Et Elisée dit: L'Eternel des armées, devant lequel je me tiens, est vivant, que si je n'avais de la considération pour Josaphat le Roi de Juda, je n'aurais aucun égard pour toi, et ne t'aurais même pas vu.
15 Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
Mais maintenant amenez-moi un joueur d'instruments. Et comme le joueur jouait des instruments, la main de l'Eternel fut sur Elisée;
16 ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
Et il dit: Ainsi a dit l'Eternel: Qu'on coupe par des fossés toute cette vallée.
17 Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
Car ainsi a dit l'Eternel: Vous ne verrez ni vent, ni pluie, et néanmoins cette vallée sera remplie d'eaux, et vous boirez, vous et vos bêtes.
18 Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
Encore cela est peu de chose pour l'Eternel; car il livrera Moab entre vos mains;
19 Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
Et vous détruirez toutes les villes fortes, et toutes les villes principales, et vous abattrez tous les bons arbres, et vous boucherez toutes les fontaines d'eaux, et vous gâterez avec des pierres tous les meilleurs champs.
20 Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
Il arriva donc au matin, environ l'heure qu'on offre l'oblation, qu'on vit venir des eaux du chemin d'Edom, en sorte que ce lieu-là fut rempli d'eaux.
21 Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
Or tous les Moabites ayant appris que ces Rois-là étaient montés pour leur faire la guerre, s'étaient assemblés à cri public, depuis tous ceux qui étaient en âge de porter les armes, et au-dessus, et ils se tinrent sur la frontière.
22 Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
Et le lendemain ils se levèrent de bon matin, et comme le soleil fut levé sur les eaux, les Moabites virent vis-à-vis d'eux les eaux rouges comme du sang.
23 Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
Et ils dirent: C'est du sang; certainement ces Rois-là se sont entre-tués, et chacun a frappé son compagnon; maintenant donc, Moabites, au butin.
24 Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
Ainsi ils vinrent au camp d'Israël, et les Israëlites se levèrent, et frappèrent les Moabites, lesquels s'enfuirent devant eux; puis ils entrèrent au pays, et frappèrent Moab.
25 Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
Ils détruisirent les villes; et chacun jetait des pierres dans les meilleurs champs, de sorte qu'ils les en remplirent; ils bouchèrent toutes les fontaines d'eaux, et abattirent tous les bons arbres, jusqu'à ne laisser que les pierres à Kir-haréseth, laquelle les tireurs de fronde environnèrent, et battirent.
26 Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
Et le Roi de Moab voyant qu'il n'était pas le plus fort, prit avec lui sept cents hommes dégainant l'épée, pour enfoncer jusqu'au Roi d'Edom; mais ils ne purent.
27 Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.
Alors il prit son fils premier-né, qui devait régner en sa place, et l'offrit en holocauste sur la muraille, et il y eut une grande indignation en Israël; ainsi ils se retirèrent de lui, et s'en retournèrent en leur pays.

< 2 Mafumu 3 >