< 2 Mafumu 3 >

1 Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
Forsothe Joram, sone of Achab, regnede on Israel, in Samarie, in the eiytenthe yeer of Josephat, kyng of Juda. And he regnede twelue yeer,
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
and he dide yuel bifor the Lord, but not as his fader and modir;
3 Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
for he took awei the ymagis of Baal, whiche his fadir hadde maad, netheles in the synnes of Jeroboam, sone of Nabath, that made Israel to do synne, `he cleuyde, and yede not awei fro tho.
4 Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
Forsothe Mesa, kyng of Moab, nurschide many beestis, and paiede to the kyng of Israel an hundrid thousynde of lambren, and an hundrid thousynde of wetheris, with her fleesis.
5 Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
And whanne Achab was deed, he brak the boond of pees, which he hadde with the kyng of Israel.
6 Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
Therfor kyng Joram yede out of Samarie in that dai, and noumbride al Israel.
7 Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
And he sente to Josephat, kyng of Juda, and seide, The kyng of Moab yede awei fro me; come thou with me ayens him to batel. Which Josephat answeride, Y schal stie; he that is myn, is thin; my puple is thi puple; and myn horsis ben thin horsis.
8 Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
And he seide, Bi what weie schulen we stie? And he answeride, Bi the deseert of Ydumee.
9 Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
Therfor the kyng of Israel, and the kyng of Juda, and the kyng of Edom, yeden forth, and cumpassiden bi the weie of seuene daies; and `watir was not to the oost, and to the beestis, that sueden hem.
10 Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
And the kyng of Israel seide, Alas! alas! alas! the Lord hath gaderide vs thre kyngis to bitake vs in the hond of Moab.
11 Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
And Josephat seide, Whether ony prophete of the Lord is here, that we biseche the Lord bi hym? And oon of the seruauntis of the kyng of Israel answeride, Elisee, the sone of Saphat, is here, that schedde watir on the hondis of Elie.
12 Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
And Josephat seide, Is the word of the Lord at hym? Whiche seiden, `It is. And the kyng of Israel, and Josephat, kyng of Juda, and the kyng of Edom, yeden doun to hym.
13 Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
Forsothe Elise seide to the kyng of Israel, What is to me and to thee? Go thou to the prophetis of thi fadir and of thi modir. And the kyng of Israel seide to hym, Whi hath the Lord gaderid these thre kyngis, to bitake hem into the hondis of Moab?
14 Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
And Elisee seide to hym, The Lord of oostis lyueth, in whos siyt Y stonde, if Y were not aschamed of the cheer of Josephat, king of Juda, treuli Y hadde not perseyued, nethir Y hadde biholde thee.
15 Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
Now forsothe brynge ye to me a sautrere. And whanne the sautrere song, the hond of the Lord was maad on hym, and he seide, The Lord seith these thingis,
16 ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
Make ye the wombe, ether depthe, of this stronde dichis and dichis.
17 Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
For the Lord seith these thingis, Ye schulen not se wynd, nethir reyn, and this depthe schal be fillid with watris, and ye schulen drynke, and youre meynees, and youre beestis.
18 Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
And this is litil in the siyt of the Lord. Ferthermore also he schal bitake Moab in to youre hondis;
19 Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
and ye schulen smyte ech strengthid citee, and ech chosun citee, and ye schulen kitte doun ech tre berynge fruyt, and ye schulen stoppe alle the wellis of watris, and ye schulen hile with stonys ech noble feeld.
20 Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
Therfor it was doon eerli, whanne sacrifice is wont to be offrid, and, lo! watris camen bi the weie of Edom, and the lond was fillid with watris.
21 Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
Sotheli alle men of Moab herden, that kyngis hadden stied to fiyte ayens hem; `and men of Moab clepiden togidere alle men, that weren gird with girdil aboue, and thei stoden in the termes.
22 Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
And men of Moab risiden ful eerli, and whanne the sunne was risun thanne euen ayens the watris, thei sien the watris reed as blood euene ayens.
23 Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
And thei seiden, It is the blood of swerd, `that is, sched out bi swerd; kyngis fouyten ayens hem silf, and thei ben slayn togider; now go thou, Moab, to the prey.
24 Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
And thei yeden in to the castels of Israel; forsothe Israel roos, and smoot Moab, and thei fledden bifor men of Israel. Therfor thei that hadden ouercome, camen, and smytiden Moab, and destrieden cytees;
25 Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
and alle men sendynge stoonys filliden ech beste feeld, and stoppiden alle the wellis of watris, and kittiden doun alle trees berynge fruyt, so that oneli `wallis maad of erthe weren left; and the citee was cumpassid of men settinge engynes, and was smytun bi greet part.
26 Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
And whanne the kyng of Moab hadde seyn this, that is, that the enemyes hadden the maistrie, he took with hym seuene hundrid men drawynge swerdis, that thei shulden breke in to the kyng of Edom; and thei myyten not.
27 Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.
And he took his firste gendrid sone, that schulde regne for hym, and offride brent sacrifice on the wal; and greet indignacioun was maad in Israel; and anoon thei yeden awei fro hym, and turneden ayen in to her lond.

< 2 Mafumu 3 >