< 2 Mafumu 3 >

1 Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
And Jehoram son of Ahab has reigned over Israel, in Samaria, in the eighteenth year of Jehoshaphat king of Judah, and he reigns twelve years,
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
and does evil in the eyes of YHWH, only not like his father, and like his mother, and he turns aside the standing-pillar of Ba‘al that his father made;
3 Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
surely he has cleaved to the sins of Jeroboam son of Nebat that he caused Israel to sin; he has not turned aside from it.
4 Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
And Mesha king of Moab was a sheep-master, and he rendered to the king of Israel one hundred thousand lambs and one hundred thousand rams, [with] wool,
5 Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
and it comes to pass at the death of Ahab, that the king of Moab transgresses against the king of Israel.
6 Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
And King Jehoram goes out from Samaria in that day, and inspects all Israel,
7 Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
and goes and sends to Jehoshaphat king of Judah, saying, “The king of Moab has transgressed against me; do you go with me to Moab for battle?” And he says, “I go up, as I, so you; as my people, so your people; as my horses, so your horses.”
8 Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
And he says, “Where [is] this—the way we go up?” And he says, “The way of the wilderness of Edom.”
9 Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
And the king of Israel goes, and the king of Judah, and the king of Edom, and they turn around the way seven days, and there has been no water for the camp, and for the livestock that [are] at their feet,
10 Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
and the king of Israel says, “Aah! For YHWH has called for these three kings to give them into the hand of Moab.”
11 Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
And Jehoshaphat says, “Is there not a prophet of YHWH here, and we seek YHWH by him?” And one of the servants of the king of Israel answers and says, “Here [is] Elisha son of Shaphat, who poured water on the hands of Elijah.”
12 Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
And Jehoshaphat says, “The word of YHWH is with him”; and the king of Israel goes down to him, and Jehoshaphat, and the king of Edom.
13 Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
And Elisha says to the king of Israel, “And what do I [have to do] with you? Go to the prophets of your father, and to the prophets of your mother”; and the king of Israel says to him, “No, for YHWH has called for these three kings to give them into the hand of Moab.”
14 Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
And Elisha says, “YHWH of Hosts lives, before whom I have stood; for unless I am lifting up the face of Jehoshaphat king of Judah, I do not look to you, nor see you;
15 Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
and now, bring a musician to me”; and it has been, at the playing of the musician, that the hand of YHWH is on him,
16 ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
and he says, “Thus said YHWH: Make this valley ditches—ditches;
17 Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
for thus said YHWH: You do not see wind, nor do you see rain, and that valley is full of water, and you have drunk—you, and your livestock, and your beasts.
18 Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
And this has been light in the eyes of YHWH, and he has given Moab into your hand,
19 Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
and you have struck every fortified city, and every choice city, and you cause every good tree to fall, and you stop all fountains of waters, and you mar every good portion with stones.”
20 Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
And it comes to pass in the morning, at the ascending of the [morning] present, that behold, waters are coming in from the way of Edom, and the land is filled with the waters,
21 Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
and all of Moab has heard that the kings have come up to fight against them, and they are called together, from everyone girding on a girdle and upward, and they stand by the border.
22 Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
And they rise early in the morning, and the sun has shone on the waters, and the Moabites see, from opposite [them], [that] the waters [are] red as blood,
23 Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
and say, “This [is] blood; the kings have been surely destroyed, and they each strike his neighbor; and now for spoil, Moab!”
24 Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
And they come to the camp of Israel, and Israel rises, and strikes the Moabites, and they flee from their face; and they enter into Moab, so as to strike Moab,
25 Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
and they break down the cities, and they each cast his stone [on] every good portion, and have filled it, and they stop every fountain of water, and they cause every good tree to fall—until one had left its stones in Kir-Haraseth, and the slingers go around and strike it.
26 Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
And the king of Moab sees that the battle has been too strong for him, and he takes with him seven hundred men drawing sword, to cleave through to the king of Edom, and they have not been able,
27 Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.
and he takes his son, the firstborn who reigns in his stead, and causes him to ascend [as] a burnt-offering on the wall, and there is great wrath against Israel, and they journey from off him, and return to the land.

< 2 Mafumu 3 >