< 2 Mafumu 25 >
1 Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
And it was in [the] year ninth of reigning his in the month tenth on the ten of the month he came Nebuchadnezzar [the] king of Babylon he and all army his on Jerusalem and he encamped on it and they built on it a siege-wall all around.
2 Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
And it came the city in state of siege until one [plus] ten year of the king Zedekiah.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
(In the month fourth *X*) on [day] nine of the month and it was severe the famine in the city and not it belonged food to [the] people of the land.
4 Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
And it was broken into the city and all [the] men of war - this night [the] way of [the] gate - between the two walls which [was] at [the] garden of the king and [the] Chaldeans [were] on the city all around and he went [the] direction of the Arabah.
5 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
And they pursued [the] army of [the] Chaldeans after the king and they overtook him in [the] plains of Jericho and all army his they were scattered from with him.
6 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
And they seized the king and they brought up him to [the] king of Babylon Riblah towards and they spoke with him judgment.
7 Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
And [the] sons of Zedekiah they slaughtered to eyes his and [the] eyes of Zedekiah he made blind and he bound him with bronze fetters and he brought him Babylon.
8 Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
And in the month fifth on [day] seven of the month it [was] year nine-teen year of the king Nebuchadnezzar [the] king of Babylon he came Nebuzaradan [the] chief of [the] bodyguards [the] servant of [the] king of Babylon Jerusalem.
9 Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
And he burned [the] house of Yahweh and [the] house of the king and all [the] houses of Jerusalem and every house of a great [person] he burned with fire.
10 Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
And [the] walls of Jerusalem all around they broke down all [the] army of [the] Chaldeans who [was the] chief of [the] bodyguards.
11 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
And [the] rest of the people which remained in the city and those [who] fell who they fell on the king of Babylon and [the] rest of the multitude he took into exile Nebuzaradan [the] chief of [the] bodyguards.
12 Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
And some of [the] poor people of the land he left behind [the] chief of [the] bodyguards to vinedressers and to ploughmen.
13 Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
And [the] pillars of bronze which [were] [the] house of Yahweh and the stands and [the] sea of bronze which [was] in [the] house of Yahweh they broke [the] Chaldeans and they carried bronze their Babylon towards.
14 Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
And the pots and the shovels and the snuffers and the pans and all [the] articles of bronze which people served with them they took.
15 Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
And the fire-pans and the bowls which [were] gold gold and which [were] silver silver he took [the] chief of [the] bodyguards.
16 Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
The pillars - two the sea one and the stands which he had made Solomon for [the] house of Yahweh not it belonged weight to [the] bronze of all the articles these.
17 Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
[was] eight-Teen cubit[s] [the] height of - the pillar one and a capital [was] on it - bronze and [the] height of the capital [was] three (cubits *Q(K)*) and a network and pomegranates [were] on the capital all around everything [was] bronze and like these [things] [belonged] to the pillar second with the network.
18 Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
And he took [the] chief of [the] bodyguards Seraiah [the] priest of the head and Zephaniah a priest second and [the] three [the] keepers of the threshold.
19 Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
And from the city he took a court-official one who he [was] overseer - over [the] men of war and five men from [those who] saw [the] face of the king who they were found in the city and the scribe [the] commander of the army who mustered [the] people of the land and sixty man from [the] people of the land who were found in the city.
20 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
And he took them Nebuzaradan [the] chief of [the] bodyguards and he brought them to [the] king of Babylon Riblah towards.
21 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
And he struck down them [the] king of Babylon and he put to death them at Riblah in [the] land of Hamath and it went into exile Judah from on land its.
22 Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
And the people who remained in [the] land of Judah whom he left behind Nebuchadnezzar [the] king of Babylon and he appointed over them Gedaliah [the] son of Ahikam [the] son of Shaphan.
23 Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
And they heard all [the] commanders of the armies they and the men that he had appointed [the] king of Babylon Gedaliah and they came to Gedaliah Mizpah and Ishmael [the] son of Nethaniah and Johanan [the] son of Kareah and Seraiah [the] son of Tanhumeth the Netophathite and Jaazaniah [the] son of the Maacathite they and men their.
24 Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
And he swore an oath to them Gedaliah and to men their and he said to them may not you be afraid from [the] servants of the Chaldeans dwell in the land and serve [the] king of Babylon so it may go well for you.
25 Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
And it was - in the month seventh he came Ishmael [the] son of Nethaniah [the] son of Elishama one of [the] offspring of royalty and ten men with him and they struck down Gedaliah and he died and the Jews and the Chaldeans who they were with him at Mizpah.
26 Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
And they arose all the people from [the] small and unto [the] great and [the] commanders of the armies and they went Egypt for they were afraid of [the] Chaldeans.
27 Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
And it was in thirty and seven year of [the] exile of Jehoiachin [the] king of Judah in two [plus] ten month on [day] twenty and seven of the month he lifted up Evil-Merodach [the] king of Babylon in [the] year became king he [the] head of Jehoiachin [the] king of Judah from [the] house of imprisonment.
28 Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
And he spoke with him good and he set throne his above [the] throne of the kings who [were] with him in Babylon.
29 Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
And he changed [the] clothes of imprisonment his and he ate bread continually before him all [the] days of life his.
30 Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.
And allowance his an allowance of continuity it was given to him from with the king [the] matter of a day in day its all [the] days of life his.