< 2 Mafumu 25 >
1 Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
Og det skete i hans Regerings niende Aar, i den tiende Maaned, paa den tiende Dag i Maaneden, da kom Nebukadnezar, Kongen af Babel, han og hele hans Hær, imod Jerusalem og lejrede sig imod den, og de byggede et Bolværk imod den trindt omkring.
2 Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
Saa blev Staden belejret indtil Kong Zedekias's ellevte Aar.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
Paa den niende Dag i Maaneden, da fik Hungeren Overhaand i Staden, og der var ikke Brød for Folket i Landet.
4 Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
Og man brød ind i Staden, og alle Krigsmænd flyede om Natten ad Vejen gennem Porten imellem de to Mure, hvilken gaar til Kongens Have; og Kaldæerne laa trindt omkring Staden, og Kongen drog hen ad Vejen til den slette Mark.
5 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
Men Kaldæernes Hær forfulgte Kongen, og de naaede ham paa den slette Mark ved Jeriko, og hele hans Hær blev adspredt fra ham.
6 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
Og de grebe Kongen og førte ham op til Kongen af Babel, til Ribla, og holdt Ret over ham.
7 Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Og de nedhuggede Zedekias's Sønner for hans Øjne, og man blindede Zedekias's Øjne, og de bandt ham med to Kobberlænker og førte ham til Babel.
8 Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
Og i den femte Maaned paa den syvende Dag i Maaneden (det Aar var Kong Nebukadnezars, Babels Konges, nittende Aar) kom Nebusar-Adan, Øversten for Livvagten, Kongen af Babels Tjener, til Jerusalem.
9 Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
Og han opbrændte Herrens Hus og Kongens Hus; og alle Husene i Jerusalem, ja alle store Huse opbrændte han med Ild.
10 Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
Og hele Kaldæernes Hær, som var med den øverste for Livvagten, nedbrød Jerusalems Mur trindt omkring.
11 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Men det øvrige Folk, de overblevne i Staden og de frafaldne, som vare gaaede over til Kongen af Babel, og den øvrige Hob førte Nebusar-Adan, Øversten for Livvagten, bort.
12 Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
Og Øversten for Livvagten lod nogle af de ringeste i Landet blive tilbage til Vingaardsmænd og til Agermænd.
13 Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
Og Kobberstøtterne, som vare i Herrens Hus, og Stolene og Kobberhavet, som var i Herrens Hus, sønderbrøde Kaldæerne, og de førte Kobberet af dem til Babel.
14 Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
Og Gryderne og Skufferne og Knivene og Røgelseskaalerne og alle Kobberkarrene, som brugtes til Tjenesten, toge de bort.
15 Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
Og Ildkarrene og Skaalerne, hvad som var helt Guld, og som var helt Sølv, tog den øverste for Livvagten.
16 Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
De to Støtter og det ene Hav og de Stole, som Salomo havde gjort til Herrens Hus: — Der var ikke Vægt paa Kobberet af alle disse Ting.
17 Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
Højden af den ene Støtte var atten Alen, og Kronen derpaa var af Kobber, og Kronens Højde var tre Alen; og Nettet og Granatæblerne trindt omkring paa Kronen var alt sammen af Kobber, og paa samme Maade var den anden Støtte med Nettet.
18 Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
Og Øversten for Livvagten tog Ypperstepræsten Seraja og Zefania, Præsten af anden Rang, og tre, som toge Vare paa Dørtærskelen;
19 Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
og af Staden tog han een Hofbetjent, som var Befalingsmand over Krigsmændene, og fem Mænd af dem, som saa Kongens Ansigt og som fandtes i Staden, og Skriveren, som var hos Stridshøvedsmanden, og som udskrev Folket i Landet, og tresindstyve Mænd af Folket i Landet, som fandtes i Staden.
20 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
Og Nebusar-Adan, den øverste for Livvagten, tog dem og førte dem til Kongen af Babel, til Ribla.
21 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
Og Kongen af Babel slog dem ihjel og dræbte dem i Ribla, i Hamaths Land; saa blev Juda bortført fra sit Land.
22 Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
Men over Folket, som blev tilbage i Judas Land, som Nebukadnezar, Kongen af Babel, lod blive tilbage, over dem satte han Gedalia, en Søn af Ahikam, Safans Søn.
23 Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
Der alle Stridshøvedsmændene, de og deres Mænd, hørte, at Kongen af Babel havde sat Gedalia over dem, da kom de til Gedalia til Mizpa, baade Ismael, Nethanias Søn, og Johanan, Kareaks Søn, og Seraja, Netofatiten Thanhumeths Søn, og Maakatiten Jaasanias Søn, de og deres Mænd.
24 Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
Og Gedalia tilsvor dem og deres Mænd og sagde til dem: Frygter ikke for Kaldæernes Tjenere; bliver i Landet og tjener Kongen af Babel, saa skal det gaa eder vel.
25 Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
Men det skete i den syvende Maaned, at Ismael, en Søn af Nethania, Elisamas Søn, af kongelig Sæd, kom og ti Mænd med ham, og de sloge Gedalia, saa at han døde tillige med Jøderne og Kaldæerne, som vare hos ham i Mizpa.
26 Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
Da gjorde alt Folket sig rede, baade smaa og store, tillige med Hærenes Øverster og drog til Ægypten; thi de frygtede for Kaldæerne.
27 Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
Og det skete i det syv og tredivte Aar, efter at Jojakin, Kongen af Juda, var bortført, i den tolvte Maaned, paa den syv og tyvende Dag i Maaneden, da opløftede Evilmerodak, Kongen af Babel, i det Aar han blev Konge, Jojakins, Judas Konges Hoved fra Fængselets Hus.
28 Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
Og han talede gode Ord med ham, og han satte hans Stol over de Kongers Stole, som vare hos ham i Babel.
29 Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
Og han omskiftede sine Fængselsklæder, og han aad stedse Brød for hans Ansigt i alle sine Livsdage.
30 Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.
Og angaaende hans Underholdning, da gaves ham stadig Underholdning af Kongen, hver Dag hvad han behøvede for den Dag, alle hans Livsdage.