< 2 Mafumu 25 >

1 Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
Devete godine njegova kraljevanja, desetoga dana desetoga mjeseca, krenu sam babilonski kralj Nabukodonozor sa svom svojom vojskom na Jeruzalem. Utabori se pred gradom i opasa ga opkopom.
2 Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
Grad osta opkoljen do jedanaeste godine Sidkijina kraljevanja.
3 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
Devetoga dana četvrtoga mjeseca, kad je u gradu zavladala takva glad da priprosti puk nije imao ni kruha,
4 Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
neprijatelj provali u grad. Tada kralj i svi ratnici pobjegoše noću kroz vrata između dva zida nad Kraljevim vrtom - Kaldejci bijahu opkolili grad - i krenuše putem prema Arabi.
5 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
Kaldejske čete nagnuše u potjeru za kraljem i sustigoše ga na Jerihonskim poljanama, a sva se njegova vojska razbježala.
6 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
Kaldejci uhvatiše kralja i odvedoše ga u Riblu pred kralja babilonskog, koji mu izreče presudu.
7 Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
Sidkijine sinove pokla pred njegovim očima, Sidkiji iskopa oči, okova ga verigama i odvede u Babilon.
8 Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
Sedmoga dana petoga mjeseca - devetnaeste godine kraljevanja Nabukodonozora, kralja babilonskog - uđe u Jeruzalem Nebuzaradan, zapovjednik kraljeve tjelesne straže i časnik babilonskog kralja.
9 Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
On zapali Dom Jahvin, kraljevski dvor i sve kuće u Jeruzalemu.
10 Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
Kaldejske čete, pod zapovjednikom kraljevske tjelesne straže, razoriše zidine koje su okruživale Jeruzalem.
11 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Nebuzaradan, zapovjednik kraljeve tjelesne straže, odvede u sužanjstvo ostatak naroda koji bijaše ostao u gradu, a tako i prebjege babilonskom kralju i ostalu svjetinu.
12 Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
Neke od malih ljudi ostavi zapovjednik u zemlji kao vinogradare i ratare.
13 Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
Kaldejci razbiše tučane stupove u Domu Jahvinu, podnožja i mjedeno more koji su bili u Domu Jahvinu i tuč odniješe u Babilon.
14 Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
Uzeše i lonce, lopate, noževe, posudice i uopće sav tučani pribor koji se upotrebljavao za bogoslužja.
15 Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
Zapovjednik uze i kadionice i škropionice, uopće sve što bijaše od zlata i srebra,
16 Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
dva stupa, jedno more i podnožja, što je Salomon dao izraditi za Dom Jahvin. Nije moguće procijeniti koliko je tuča bilo u svim tim predmetima.
17 Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
Prvi stup bijaše visok osamnaest lakata, imao je glavicu od tuča, visoku pet lakata; obvijaše je oplet i mogranji, sve od tuča. Takav je bio i drugi stup.
18 Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
Zapovjednik straže odveo je svećeničkog poglavara Seraju, drugog svećenika, Sefaniju, i tri čuvara praga.
19 Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
Iz grada je odveo jednog dvoranina, vojničkog zapovjednika, pet ljudi iz kraljeve pratnje koji se zatekoše u gradu, pisara zapovjednika vojske koji je novačio puk i šezdeset pučana koji se također zatekoše u gradu.
20 Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
Zapovjednik kraljevske tjelesne straže Nebuzaradan odvede ih pred kralja babilonskoga u Riblu.
21 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
I kralj babilonski zapovjedi da ih pogube u Ribli, u zemlji hamatskoj. Tako su judejski narod odveli s njegove rodne grude.
22 Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
Narodu što je ostao u zemlji judejskoj i što ga je ostavio babilonski kralj Nabukodonozor - postavio je ovaj za upravitelja Gedaliju, sina Ahikamova, unuka Šafanova.
23 Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
Svi vojni zapovjednici i njihovi ljudi saznaše da je babilonski kralj postavio zemlji za namjesnika Gedaliju i dođoše pred njega u Mispu: Netanijin sin Jišmael; Kareahov sin Johanan; sin Tanhumeta iz Netofe, Seraja; Maakatijev sin Jaazanija - oni i svi njihovi ljudi.
24 Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
Gedalija se zakle njima i njihovim ljudima i reče: “Ne bojte se služiti Kaldejcima; ostanite u zemlji, budite podložni babilonskom kralju i bit će vam dobro.”
25 Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
Ali sedmoga mjeseca Jišmael, sin Netanijin, unuk Elišamin, koji bijaše kraljevskog roda, i još deset ljudi s njim ubiše Gedaliju te on umrije kao i svi Judejci i Kaldejci koji bijahu s njim u Mispi.
26 Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
Tada sav narod, od maloga do velikog, i svi zapovjednici četa ustadoše i odoše u Egipat jer se bojahu Kaldejaca.
27 Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
Trideset i sedme godine otkako je zasužnjen judejski kralj Jojakin, dvadeset i sedmog dana dvanaestoga mjeseca, babilonski kralj Evil Merodak u prvoj godini svoje vladavine pomilova judejskog kralja Jojakina i pusti ga iz tamnice.
28 Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
Ljubezno je s njime razgovarao i stolicu mu postavio više nego ostalim kraljevima koji bijahu s njim u Babilonu.
29 Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
Jojakin je odložio svoje tamničke haljine i jeo s kraljem za istim stolom svega svoga vijeka.
30 Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.
Do kraja njegova života babilonski mu je kralj trajno, iz dana u dan, davao uzdržavanje.

< 2 Mafumu 25 >