< 2 Mafumu 24 >

1 Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
Dans les jours de Joakim, Nabuchodonosor, roi de Babylone, monta contre Juda, et Joakim lui fut assujetti durant trois ans; et ensuite il se révolta contre lui.
2 Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
Et le Seigneur envoya les voleurs des Chaldéens, les voleurs de Syrie, les voleurs de Moab et les voleurs des enfants d’Ammon, et il les envoya contre Juda pour l’exterminer, selon la parole que le Seigneur avait dite par ses serviteurs, les prophètes.
3 Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
Or ceci arriva par la parole du Seigneur contre Juda, pour l’ôter de devant lui, à cause de tous les péchés que Manassé fit,
4 kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
Et à cause du sang de l’innocent qu’il versa; car il remplit Jérusalem de sang innocent. C’est pour ce motif que le Seigneur ne voulut point se rendre propice.
5 Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Mais le reste des actions de Joakim, et tout ce qu’il a fait, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois de Juda? Et Joakim dormit avec ses pères;
6 Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Joachin, son fils, régna en sa place.
7 Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
Et le roi d’Egypte ne recommença plus à sortir de son pays; car le roi de Babylone avait emporté, depuis le torrent d’Egypte jusqu’au fleuve d’Euphrate, tout ce qui était au roi d’Egypte.
8 Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
Joachin avait dix-huit ans lorsqu’il commença à régner, et il régna trois mois à Jérusalem: le nom de sa mère était Nohesta, fille d’Elnathan de Jérusalem.
9 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
Et il fit le mal devant le Seigneur, selon tout ce qu’avait fait son père.
10 Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
En ce temps-là les serviteurs de Nabuchodonosor, roi de Babylone, montèrent à Jérusalem, et la ville fut entourée de fortifications.
11 ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
Nabuchodonosor, roi de Babylone, vint aussi avec ses serviteurs pour l’attaquer.
12 Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
Et Joachin, roi de Juda, sortit vers le roi de Babylone, lui, sa mère, ses serviteurs, ses princes et ses eunuques; et le roi de Babylone le reçut la huitième année de son règne.
13 Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
Et il emporta de Jérusalem tous les trésors de la maison du Seigneur, et les trésors de la maison du roi; et il brisa tous les vases d’or que Salomon, roi d’Israël, avait faits dans le temple du Seigneur, selon la parole du Seigneur.
14 Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
Et il transféra toute la ville de Jérusalem, tous les princes et tous les forts de l’armée, au nombre de dix mille, en captivité, et aussi tous les ouvriers et tous les lapidaires, et rien ne fut laissé, excepté les pauvres du peuple du pays.
15 Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
Il transféra aussi à Babylone Joachin, la mère du roi, les femmes du roi, ses eunuques; et les juges du pays, il les emmena en captivité de Jérusalem à Babylone.
16 Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
Il transféra encore tous les hommes vigoureux, au nombre de sept mille, les ouvriers et les lapidaires au nombre de mille, tous les hommes courageux et guerriers; et le roi de Babylone les emmena captifs à Babylone.
17 Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
Il établit, en la place de Joachin, Matthanias son oncle, et il lui imposa le nom de Sédécias.
18 Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Sédécias avait vingt-un ans d’âge lorsqu’il commença à régner, et il régna onze ans à Jérusalem: le nom de sa mère était Amital, fille de Jérémie, de Lobna.
19 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
Et il fit le mal devant le Seigneur, selon tout ce qu’avait fait Joakim.
20 Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.
Car le Seigneur s’irritait contre Jérusalem et contre Juda, jusqu’à ce qu’il les rejetât de devant sa face; et Sédécias se détacha du roi de Babylone.

< 2 Mafumu 24 >