< 2 Mafumu 24 >

1 Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
in/on/with day his to ascend: rise Nebuchadnezzar king Babylon and to be to/for him Jehoiakim servant/slave three year and to return: turn back and to rebel in/on/with him
2 Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
and to send: depart LORD in/on/with him [obj] band Chaldea and [obj] band Syria and [obj] band Moab and [obj] band son: descendant/people Ammon and to send: depart them in/on/with Judah to/for to perish him like/as word LORD which to speak: speak in/on/with hand: by servant/slave his [the] prophet
3 Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
surely upon lip: word LORD to be in/on/with Judah to/for to turn aside: remove from upon face his in/on/with sin Manasseh like/as all which to make: do
4 kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
and also blood [the] innocent which to pour: kill and to fill [obj] Jerusalem blood innocent and not be willing LORD to/for to forgive
5 Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
and remainder word: deed Jehoiakim and all which to make: do not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Judah
6 Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
and to lie down: be dead Jehoiakim with father his and to reign Jehoiachin son: child his underneath: instead him
7 Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
and not to add: again still king Egypt to/for to come out: come from land: country/planet his for to take: take king Babylon from Brook Egypt till river Euphrates all which to be to/for king Egypt
8 Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
son: aged eight ten year Jehoiachin in/on/with to reign he and three month to reign in/on/with Jerusalem and name mother his Nehushta daughter Elnathan from Jerusalem
9 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD like/as all which to make: do father his
10 Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
in/on/with time [the] he/she/it (to ascend: rise *Q(K)*) servant/slave Nebuchadnezzar king Babylon Jerusalem and to come (in): besiege [the] city in/on/with siege
11 ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
and to come (in): come Nebuchadnezzar king Babylon upon [the] city and servant/slave his to confine upon her
12 Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
and to come out: come Jehoiachin king Judah upon king Babylon he/she/it and mother his and servant/slave his and ruler his and eunuch his and to take: take [obj] him king Babylon in/on/with year eight to/for to reign him
13 Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
and to come out: send from there [obj] all treasure house: temple LORD and treasure house: home [the] king and to cut [obj] all article/utensil [the] gold which to make Solomon king Israel in/on/with temple LORD like/as as which to speak: promise LORD
14 Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
and to reveal: remove [obj] all Jerusalem and [obj] all [the] ruler and [obj] all mighty man [the] strength (ten *Q(K)*) thousand captivity and all [the] artificer and [the] locksmith not to remain exception poor people [the] land: country/planet
15 Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
and to reveal: remove [obj] Jehoiachin Babylon [to] and [obj] mother [the] king and [obj] woman: wife [the] king and [obj] eunuch his and [obj] (leader *Q(K)*) [the] land: country/planet to go: take captivity from Jerusalem Babylon [to]
16 Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
and [obj] all human [the] strength seven thousand and [the] artificer and [the] locksmith thousand [the] all mighty man to make battle and to come (in): bring them king Babylon captivity Babylon [to]
17 Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
and to reign king Babylon [obj] Mattaniah beloved: male relative his underneath: instead him and to turn: changed [obj] name his Zedekiah
18 Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
son: aged twenty and one year Zedekiah in/on/with to reign he and one ten year to reign in/on/with Jerusalem and name mother his (Hamutal *Q(K)*) daughter Jeremiah from Libnah
19 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD like/as all which to make: do Jehoiakim
20 Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.
for upon face: anger LORD to be in/on/with Jerusalem and in/on/with Judah till to throw he [obj] them from upon face: before his and to rebel Zedekiah in/on/with king Babylon

< 2 Mafumu 24 >