< 2 Mafumu 24 >

1 Pa nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anadzathira nkhondo dzikolo ndipo Yehoyakimu anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zitatu. Koma kenaka anasintha maganizo ake nawukira Nebukadinezara.
Za dnů jeho přitáhl Nabuchodonozor král Babylonský, i učiněn jest Joakim služebníkem jeho za tři léta. Potom odvrátiv se, zprotivil se jemu.
2 Yehova anatumiza magulu a Ababuloni, Aaramu, Amowabu ndi Aamoni, kudzathira nkhondo Yuda. Iye anawatumiza kudzawononga Yuda molingana ndi mawu amene Yehova ananeneratu kudzera mwa aneneri ake.
Protož poslal Hospodin na něj lotříky Kaldejské a lotříky Syrské, i lotříky Moábské a lotříky synů Ammon, poslal je, pravím, na Judu, aby ho zkazili vedlé řeči Hospodinovy, kterouž byl mluvil skrze služebníky své proroky.
3 Ndithu, izi zinachitikira Yuda monga momwe Yehova analamulira nʼcholinga choti awachotse pamaso pake chifukwa cha machimo a Manase ndi zonse zimene anachita,
A jistě podlé řeči Hospodinovy to se dálo proti Judovi, aby jej zavrhl od tváři své pro hříchy Manassesovy, vedlé toho všeho, což byl činil,
4 kuphatikizapo kukhetsa magazi a anthu osalakwa. Chifukwa iye anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kumukhululukira.
Ano i pro krev nevinnou, kterouž vylil, naplniv Jeruzalém krví nevinnou, čehož nechtěl Hospodin prominouti.
5 Ntchito zina za Yehoyakimu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
O jiných pak věcech Joakimových, a cožkoli činil, psáno jest v knize o králích Judských.
6 Yehoyakimu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
A tak usnul Joakim s otci svými, a kraloval Joachin syn jeho místo něho.
7 Mfumu ya Igupto sinatulukenso mʼdziko lake chifukwa mfumu ya Babuloni inalanda mayiko onse kuchokera ku Mtsinje wa ku Igupto mpaka ku Mtsinje wa Yufurate.
Král pak Egyptský nikdy více nevytáhl z země své; nebo král Babylonský pobral od řeky Egyptské až k řece Eufraten všecko, cožkoli měl král Egyptský.
8 Yehoyakini anakhala mfumu ali ndi zaka 18 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Nehusita mwana wa Elinatani wa ku Yerusalemu.
V osmnácti letech byl Joachin, když počal kralovati, a tři měsíce kraloval v Jeruzalémě. Jméno matky jeho Nechusta, dcera Elnatanova z Jeruzaléma.
9 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira abambo ake.
I činil to, což jest zlého před očima Hospodinovýma, všecko tak, jakž byl činil otec jeho.
10 Nthawi imeneyo ankhondo a Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ku Yerusalemu nazinga mzindawo ndi misasa ya nkhondo
Toho času vytáhli služebníci Nabuchodonozora krále Babylonského proti Jeruzalému, a obleženo jest město.
11 ndipo Nebukadinezara anafika ku mzindawo pamene ankhondo ake anawuzinga.
Ano i Nabuchodonozor král Babylonský přitáhl proti městu, když služebníci jeho leželi vůkol něho.
12 Yehoyakini mfumu ya Yuda pamodzi ndi amayi ake, atumiki ake, anthu ake olemekezeka ndiponso akuluakulu onse anadzipereka kwa mfumu ya ku Babuloni. Mfumu ya Babuloni inagwira Yoyakini ukapolo mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ufumu wake.
Tedy vyšel Joachin král Judský k králi Babylonskému, i s matkou svou i s služebníky, knížaty i komorníky svými, kteréhož vzal král Babylonský léta osmého kralování svého.
13 Monga ananenera Yehova, Nebukadinezara anachotsa chuma chonse cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso cha mʼnyumba ya mfumu ndipo anatenga ziwiya zonse zagolide za ku Nyumba ya Yehova zimene Solomoni mfumu ya Israeli anapanga.
A vynesl odtud všecky poklady domu Hospodinova, a poklady domu královského, a ztloukl všecky nádoby zlaté, jichž byl nadělal Šalomoun král Izraelský do domu Hospodinova, jakož byl mluvil Hospodin.
14 Anatenga anthu onse a mu Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo. Akuluakulu onse pamodzi ndi anthu ankhondo, anthu onse aluso ndi amisiri osula onse pamodzi analipo 10,000. Osauka okha ndiye anatsala mʼdzikomo.
Při tom přenesl všecken Jeruzalém a všecka knížata i všecky muže udatné, deset tisíců zajatých, i všecky tesaře a kováře. Žádného nezanechal, kromě chaterných lidí země.
15 Nebukadinezara anatenga Yehoyakini ngati kapolo kupita naye ku Babuloni. Mu Yerusalemu anatenganso amayi a mfumu, akazi ake, akuluakulu ake ndiponso anthu olemekezeka mʼdzikomo.
Zavedl také i Joachina do Babylona, a matku jeho i ženy královské i komorníky jeho; silné také země zavedl do vězení z Jeruzaléma do Babylona.
16 Mfumu ya Babuloni inatumizanso ku Babuloni anthu ankhondo 70,000, anthu amphamvu ndi okonzeka kupita ku nkhondo, anthu aluso ndi amisiri osula 1,000.
Všech také mužů udatných sedm tisíců, tesařů také a kovářů tisíc, všecky též zmužilé bojovníky zavedl jaté král Babylonský do Babylona.
17 Iye analonga ufumu Mataniya, malume wa Yoyakini mʼmalo mwake ndipo anasintha dzina lake kuti akhale Zedekiya.
Ustanovil pak král Babylonský Mataniáše, strýce jeho, králem místo něho, a změnil mu jméno, aby sloul Sedechiáš.
18 Zedekiya anakhala mfumu ali ndi zaka 21 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
V jedenmecítma letech byl Sedechiáš, když počal kralovati a jedenácte let kraloval v Jeruzalémě. Jméno matky jeho bylo Chamutal, dcera Jeremiášova z Lebna.
19 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Yehoyakimu.
I činil to, což jest zlého před očima Hospodinovýma, všecko tak, jakž byl dělal Joakim.
20 Zonsezi zinachitikira Yerusalemu ndi Yuda chifukwa cha mkwiyo wa Mulungu ndipo pa mapeto pake anawachotsa pamaso pake. Ndipo Zedekiya anawukira mfumu ya Babuloni.
Nebo se to dálo pro rozhněvání Hospodinovo proti Jeruzalému a Judovi, až je i zavrhl od tváři své. V tom opět zprotivil se Sedechiáš králi Babylonskému.

< 2 Mafumu 24 >