< 2 Mafumu 23 >

1 Pamenepo mfumu inayitanitsa akuluakulu onse a ku Yuda ndi Yerusalemu.
Inkosi yasibiza bonke abadala bakoJuda labeJerusalema.
2 Mfumuyo inapita ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi anthu onse a ku Yuda, ndi onse okhala mu Yerusalemu, ansembe ndi aneneri, ndiponso anthu ena onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. Mfumuyo inawerenga mawu onse a mʼBuku la Chipangano limene linapezeka mʼNyumba ya Yehova, anthu onse akumva.
Yasuka yaya ethempelini likaThixo lamadoda akoJuda, abantu baseJerusalema, abaphristi labaphrofethi, abantu bonke kusukela kubantukazana kusiya kuzo kanye izikhulu. Yabafundela bonke besizwa wonke amazwi oGwalo lweSivumelwano, olwatholakala ethempelini likaThixo.
3 Mfumu inayimirira pambali pa chipilala ndi kuchita pangano pamaso pa Yehova kuti idzatsatira Yehova ndi kusunga malamulo, mawu ndi malangizo ake ndi mtima wonse ndi moyo wonse, kukwaniritsa mawu a mʼpanganoli, olembedwa mʼbukuli. Pamenepo anthu onse anadzipereka kutsatira panganoli.
Inkosi yema ngasensikeni, yavuselela isivumelwano phambi kukaThixo sokumlandela lokugcina imilayo yakhe lemithetho yakhe lezimiso zakhe ngenhliziyo yayo yonke langomoya wayo wonke, ngalokho iqinisa amazwi esivumelwano ayebhaliwe kulolugwalo. Ngakho bonke abantu bazinikela kuso isivumelwano.
4 Mfumu inalamula wansembe wamkulu Hilikiya, ansembe othandizana naye ndi alonda a pa khomo kuti achotse mʼNyumba ya Yehova ziwiya zonse zopembedzera Baala ndi Asera ndiponso mafano a zinthu zamlengalenga. Yosiya anazitentha kunja kwa Yerusalemu, ku minda ya ku Chigwa cha Kidroni ndipo phulusa lake anapita nalo ku Beteli.
Inkosi yalaya uHilikhiya umphristi omkhulu labaphristi abalandelayo labalindi beminyango ukuba bakhuphe ethempelini likaThixo zonke izitsha ezazenzelwe uBhali lo-Ashera, lazozonke izinkanyezi zaphezulu, wazitshisela ngaphandle kweJerusalema eziqintini zeSigodi saseKhidironi, umlotha wazo wawuthwalela eBhetheli.
5 Iye anachotsa ansembe a mafano amene anayikidwa ndi mafumu a Yuda kuti azifukiza lubani ku malo opembedzera mafano a ku mizinda ya ku Yuda ndi kumalo ozungulira Yerusalemu, amene ankafukiza lubani kwa Baala, dzuwa, mwezi, nyenyezi ndi zinthu zonse zamlengalenga.
Wakhupha abaphristi bezithombe ababekhethwe yinkosi yakoJuda ukuba batshise impepha emizini yakoJuda lakuleyo ephansi kweJerusalema, labo ababetshisa impepha kuBhali lelanga lenyanga lezinkanyezi zonke zaphezulu.
6 Anachotsa fano la Asera mʼNyumba ya Yehova napita nalo kunja kwa Yerusalemu, ku Chigwa cha Kidroni, nalitentha kumeneko. Anapera fanolo ndi kukataya phulusa lake pa manda a anthu wamba.
Wakhupha ethempelini likaThixo insika ka-Ashera, wayisa esigodini seKhidironi ngaphandle kweJerusalema, wayitshisela khona, wayichola yaba luthuli wasechithachithela umlotha wayo phezu kwamangcwaba abantukazana.
7 Iye anagwetsanso tinyumba ta ochita zachiwerewere, timene tinali mʼNyumba ya Yehova, kumene akazi ankalukirako mikanjo yovala popembedza Asera.
Wadiliza izindlu zabesilisa ababefeba ethempelini likaThixo lapho abesifazane ababethungela khona u-Ashera amaveli.
8 Yosiya anabweretsanso ansembe onse kuchokera mʼmizinda ya Yuda, nawononga malo opembedzera mafano, kuyambira ku Geba mpaka ku Beeriseba, kumene ansembe ankafukizako lubani. Anagwetsa nyumba za milungu zimene zinali pa chipata cha Yoswa, bwanamkubwa wa mzindawo, kumanzere kwa chipata cha mzinda.
UJosiya waletha bonke abaphristi besuka emizini yakoJuda, wangcolisa izindawo zokukhonzela, kusukela eGebha kusiya lapho abaphristi ababetshisela khona impepha eBherishebha. Wabhidliza izindawo zokukhonzela emasangweni ekungeneni kwesango likaJoshuwa umphathi womuzi, ngakwesokhohlo kwesango lomuzi.
9 Ngakhale kuti ansembe a ku malo opembedzera mafanowo sanawalole kuti atumikire pa guwa lansembe la Yehova mu Yerusalemu, koma ankadya buledi wopanda yisiti pamodzi ndi ansembe anzawo.
Loba abaphristi bezindawo zokukhonzela bengaphathisanga e-alithareni likaThixo eJerusalema, kodwa badla isinkwa esingelamvubelo kanye labanye abaphristi ababedlelana labo.
10 Mfumu Yosiya anawononganso Tofeti, amene anali ku Chigwa cha Hinomu, kuti wina aliyense asagwiritse ntchito malowo popereka mwana wake wamwamuna kapena wamkazi pa moto kwa Moleki.
Wangcolisa iThofethi elisesihotsheni saseBheni-Hinomu ukuze kungabikhona otshisa indodana yakhe kumbe indodakazi emlilweni kaMoleki.
11 Anachotsa pa chipata cholowera ku Nyumba ya Yehova akavalo amene mafumu a Yuda anawapereka ngati nsembe kwa dzuwa. Akavalo anali pafupi ndi bwalo la chipinda cha mkulu wina wotchedwa Natani-Meleki. Ndipo Yosiya anatentha magaleta opembedzera dzuwa.
Entubeni yethempeli likaThixo wasusa amabhiza amakhosi abakoJuda ayewahlukanisele ilanga, wona ayeseduze lendlu yesikhulu esasithiwa nguNathani-Meleki. UJosiya wasetshisa izinqola zempi ezazehlukaniselwe ilanga.
12 Anagwetsa maguwa amene mafumu a Yuda anawamanga pa denga pafupi ndi chipinda chapamwamba cha Ahazi, ndiponso maguwa amene Manase anamanga mʼmabwalo awiri a Nyumba ya Yehova. Yosiya anawachotsa kumeneko nawaphwanya ndi kutaya zidutswa zake mʼChigwa cha Kidroni.
Wadilizela phansi ama-alithare ayakhiwe ngamakhosi akoJuda ephahleni eduze lendlu ephezulu ka-Ahazi lama-alithare uManase ayewakhile emagumeni womabili ethempeli likaThixo. Wawasusa lapho, wawachoboza, aba yizicucu waziphosela eSigodini seKhidironi.
13 Mfumuyo inawononga malo opembedzera mafano amene ali kummawa kwa Yerusalemu cha kumpoto kwa Phiri la Chiwonongeko. Maguwawa Solomoni mfumu ya Israeli inamangira Asitoreti, fano lalikazi lonyansa la Asidoni, Kemosi, fano lonyansa la Amowabu, ndi Moleki, fano lonyansa la anthu a ku Amoni.
Inkosi yangcolisa izindawo zokukhonzela ezazingempumalanga kweJerusalema, ngaseningizimu kwentaba yokuXhwala, uSolomoni inkosi yako-Israyeli eyayizakhele u-Ashithorethi unkulunkulukazi oyisinengiso wamaSidoni, loKhemoshi uNkulunkulu oyisinengiso wamaMowabi, kanye loMoleki oyisinengiso wama-Amoni.
14 Yosiya anaphwanya miyala ya chipembedzo ndiponso anadula mitengo ya fano la Asera ndipo anakwirira malowo ndi mafupa a anthu.
UJosiya wabhidliza amatshe okukhonza, waquma izinsika zika-Ashera, wafaka amathambo abantu abanengi endaweni yazo.
15 Ngakhalenso guwa lansembe la ku Beteli, malo opembedzera mafano amene anapanga Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli, Yosiya anawononga guwalo ndi malo opembedzera mafanowo. Iye anatentha malo opembedzera mafanowo ndi kuwapera ndipo anatenthanso fano la Asera.
Le-alithari elaliseBhetheli indawo yokukhonzela eyayenziwe nguJerobhowamu indodana kaNebhathi owenza ukuba u-Israyeli one, lalelo-alithare lendawo yokukhonzela, wakubhidliza. Watshisa indawo yokukhonzela wayichola yaba yimpuphu njalo watshisa insika ka-Ashera.
16 Kenaka Yosiya anayangʼanayangʼana ndipo ataona manda amene anali pomwepo, mʼmbali mwa phiri, analamula kuti afukule mandawo ndi kutulutsa mafupa kuti awatenthe paguwapo kuti alidetse, potsatira mawu a Yehova amene munthu wa Mulungu analoseratu za zimenezi.
UJosiya wathalaza ngapha langapha, kwathi ebona amangcwaba amanengi ayelapho ewatheni loqaqa wathi kawasuswe, atshiswe e-alithareni ukulingcolisa mayelana lelizwi likaThixo elamenyezelwa ngumuntu kaThixo owaziphrofethayo lezizinto.
17 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi chizindikiro cha manda chimene ndikuwaonawo ndi chayani?” Anthu a mu mzindamo anayankha kuti, “Ndi chizindikiro cha manda a munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda amene ananeneratu zimene inu mwalichita guwa lansembe la Beteli.”
Inkosi yabuza yathi, “Ilitshe lesikhumbuzo sengcwaba leliyana engilibonayo ngelani?” Abantu bomuzi bathi, “Liphawule ingcwaba lenceku kaNkulunkulu eyavela koJuda, yaqalekisa i-alithari laseBhetheli ngalezizinto ozenze kulo.”
18 Mfumuyo inati, “Alekeni manda amenewo, munthu asachotse mafupa ake.” Choncho anawasiya mafupa akewo pamodzi ndi mafupa a mneneri wa ku Samariya uja.
Yena wasesithi, “Liyekeleni lingavumeli muntu awathinte amathambo akhe.” Ngakho bawayekela amathambo akhe kanye lalawo awomphrofethi owavela eSamariya.
19 Monga momwe Yosiya anachitira ku Beteli, anachotsa ndi kuwononga nyumba za milungu zonse ndi malo opembedzera mafano amene mafumu anamanga mʼmizinda ya ku Samariya omwe anakwiyitsa Yehova.
UJosiya wasusa amathempeli ezindawo zokukhonzela ezisemizini yaseSamariya ayekade akhiwe ngamakhosi ako-Israyeli, ethukuthelisa uThixo, wenza kiwo lokho ayekwenze eBhetheli.
20 Yosiya anapha ansembe onse amene ankatumikira ku malo opembedzera mafano, anawaphera pa maguwa awo ndi kutentha mafupa awo. Kenaka iye anapita ku Yerusalemu.
UJosiya wabulalela abaphristi bezindawo zokukhonzela phezu kwama-alithare, watshisela amathambo abantu phezu kwawo. Wasebuyela eJerusalema.
21 Mfumu inalamula anthu onse kuti, “Chitani Chikondwerero cha Paska kulemekeza Yehova Mulungu wanu, motsatira zomwe zalembedwa mʼBuku la Chipangano.”
Inkosi uJosiya yalaya bonke abantu yathi, “Ligcine iPhasika likaThixo uNkulunkulu wenu, njengoba kulotshiwe eGwalweni LweSivumelwano.”
22 Paska yotere inali isanachitikepo kuyambira nthawi ya oweruza amene anatsogolera Israeli, kapenanso nthawi yonse ya mafumu a Yuda sipanachitikenso Paska ngati imeneyo.
Lalingagcinwa iPhasika elinjalo kusukela ensukwini zabehluleli abaphatha u-Israyeli, lakuzo zonke insuku zamakhosi ako-Israyeli lezamakhosi akoJuda.
23 Koma mʼchaka cha 18 cha Mfumu Yosiya, Paska imeneyi anachitira Yehova mu Yerusalemu.
Kodwa ngomnyaka wetshumi lasificaminwembili wenkosi uJosiya, lagcinwa iPhasika likaThixo eJerusalema.
24 Kuwonjezera apa, Yosiya anachotsa anthu a mawula, woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, milungu ya mʼnyumba, mafano ndiponso zinthu zonse zonyansa zopezeka mu Yuda ndi Yerusalemu. Iye anachita izi pokwaniritsa lamulo lolembedwa mʼbuku limene Hilikiya analipeza mʼNyumba ya Yehova.
Wakwenza njalo uJosiya ukususa izangoma, labahlahluli, labonkulunkulu basezindlini, lezithombe kanye lazozonke izinto zamanyala ezazikhona koJuda laseJerusalema. Lokhu kwakuyikugcwalisa izimiso zomlayo owawulotshwe encwadini umphristi uHilikhiya ayithola ethempelini likaThixo.
25 Yosiyayo asanalowe ufumu, ngakhale atamwalira, panalibenso mfumu ina yofanana naye imene inatembenukira kwa Yehova monga anachitira, ndi mtima wake wonse, ndi moyo wake wonse, ndi mphamvu zake zonse, motsatira Malamulo onse a Mose.
Ngaphambi kwakhe noma ngemva kwakhe uJosiya kakubanga khona inkosi eyafanana laye eyaphendukela kuThixo njengalokhu akwenzayo ngenhliziyo yakhe langomphefumulo wakhe wonke njalo langamandla akhe wonke mayelana lawo wonke uMthetho kaMosi.
26 Komabe Yehova sanachotse mkwiyo wake woopsa, umene anali nawo pa Yuda chifukwa cha zonse zimene anachita Manase poputa mkwiyo wa Mulungu.
Kanti uThixo kadedanga ekuvutheni kolaka lwakhe olwavutha kakhulu koJuda ngenxa yazo zonke izinto uManase amthukuthelisa ngazo.
27 Choncho Yehova anati, “Ndidzawachotsanso anthu a ku Yuda pamaso panga monga ndinachotsera anthu a ku Israeli ndipo ndidzawukana mzinda wa Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha, pamodzi ndi Nyumba ino imene ndinati, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo.’”
Ngakho uThixo wathi, “Ngizamsusa phambi kwami uJuda njengoba ngasusa u-Israyeli, ngiwulahle lumuzi waseJerusalema engawukhethayo, lethempeli leli engathi ngalo, ‘Ibizo lami lizakuba kulo.’”
28 Ntchito zina za Yosiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Ezinye izehlakalo ngombuso kaJosiya, lakho konke akwenzayo, akulotshwanga yini egwalweni lwembali yamakhosi akoJuda na?
29 Yosiya akanali mfumu, Farao wotchedwa Neko, mfumu ya Igupto, anapita ku Mtsinje wa Yufurate kukathandiza mfumu ya ku Asiriya. Mfumu Yosiya anapita kukachita naye nkhondo, koma Neko anakumana naye ndi kumupha ku Megido.
Ngesikhathi sokubusa kukaJosiya, uFaro Nekho inkosi yaseGibhithe waya eMfuleni uYufrathe ukuyancedisa inkosi yase-Asiriya. Inkosi uJosiya wamhlangabeza empini kodwa uNekho waqondana laye wambulala eMegido.
30 Atumiki a Yosiyayo ananyamula mtembo wake mu galeta kuchokera ku Megido mpaka ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda akeake. Ndipo anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namudzoza, ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
Izisebenzi zikaJosiya zaletha isidumbu sakhe ngenqola yokulwa zisuka eMegido zisiya eJerusalema njalo zamngcwabela ethuneni lakhe. Ngakho abantu elizweni bathatha uJehowahazi indodana kaJosiya bamgcoba ubukhosi bukayise.
31 Yehowahazi anakhala mfumu ali ndi 23 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Hamutali, mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
UJehowahazi wayeleminyaka engamatshumi amabili lantathu ubudala bakhe esiba yinkosi, njalo wabusa eJerusalema inyanga ezintathu. Ibizo likanina kwakunguHamuthali indodakazi kaJeremiya njalo wayevela eLibhina.
32 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Wenza ububi emehlweni kaThixo njengabokhokho bakhe.
33 Farao Neko anamuyika mʼndende ku Ribula mʼdziko la Hamati kuti asalamulirenso mu Yerusalemu. Farao analamula Yuda kuti azikhoma msonkho wa siliva wolemera makilogalamu 3,400, ndiponso golide wolemera makilogalamu 34.
Inkosi uFaro Nekho wambopha ngamaketani eRibhila elizweni lamaHamathi ukuze angabusi eJerusalema, wamthelisa kakhulu uJuda amathalenta alikhulu esiliva, lethalenta legolide.
34 Farao Neko anayika Eliyakimu mwana wa Yosiya kuti akhale mfumu mʼmalo mwa abambo ake Yosiya, ndipo anasintha dzina lake kukhala Yehoyakimu. Koma iye anatenga Yehowahazi kupita naye ku Igupto ndipo anakafera kumeneko.
UFaro Nekho wabeka u-Eliyakhimu indodana kaJosiya esihlalweni sobukhosi esikhundleni sikayise uJosiya waseguqula ibizo lakhe wathi nguJehoyakhimi. Kodwa wathatha uJehowahazi waya laye eGibhithe, wafela khonale.
35 Yehoyakimu anapereka kwa Farao Neko siliva ndi golide amene anamufuna uja. Koma kuti iye apereke zimenezi, amankhometsa msonkho mʼdziko mwakemo ndipo amalandira siliva ndi golide kuchokera kwa anthu a mʼdzikomo molingana ndi chuma cha munthu aliyense.
UJehoyakhimi wathela ngenani lesiliva legolide elalifunwa nguFaro Nekho. Ukuze akwenelise lokho wayethelisa abantu elizweni ngesiliva legolide ngesilinganiso ayebona sibalingene.
36 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Zebuda, mwana wa Pedaya wa ku Ruma.
UJehoyakhimi wayeleminyaka engamatshumi amabili lanhlanu ubudala bakhe ethatha ubukhosi, yena wabusa eJerusalema iminyaka elitshumi lanye. Ibizo likanina lalinguZebhuda indodakazi kaPhedaya owayevela eRuma.
37 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Wenza ububi phambi kukaThixo, njengabokhokho bakhe.

< 2 Mafumu 23 >