< 2 Mafumu 23 >

1 Pamenepo mfumu inayitanitsa akuluakulu onse a ku Yuda ndi Yerusalemu.
Nampañitrike i mpanjakay, le natontoñ’ ama’e ze hene androanavi’ Iehoda naho Ierosalaimeo.
2 Mfumuyo inapita ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi anthu onse a ku Yuda, ndi onse okhala mu Yerusalemu, ansembe ndi aneneri, ndiponso anthu ena onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. Mfumuyo inawerenga mawu onse a mʼBuku la Chipangano limene linapezeka mʼNyumba ya Yehova, anthu onse akumva.
Le nionjomb’ añ’ anjomba’ Iehovà mb’eo i mpanjakay rekets’ ondati’ Iehoda iabio naho ze fonga mpimone’ Ierosalaime naho mpisoroñe naho mpitoky, naho ze kila ondaty, ty kede naho ty bey, vaho hene vinaki’e an-dravembia’ iareo ze tsara amy bokem-pañina nitendrek’ añ’ anjomba’ Iehovày.
3 Mfumu inayimirira pambali pa chipilala ndi kuchita pangano pamaso pa Yehova kuti idzatsatira Yehova ndi kusunga malamulo, mawu ndi malangizo ake ndi mtima wonse ndi moyo wonse, kukwaniritsa mawu a mʼpanganoli, olembedwa mʼbukuli. Pamenepo anthu onse anadzipereka kutsatira panganoli.
Nijohañe ami’ty fahañe eo i mpanjakay naho nifañina añatrefa’ Iehovà, t’ie hañavelo am-pañorihañe Iehovà naho hiambeñe o lili’eo naho o taro’eo vaho o fañè’eo añ’ ampon’ arofo naho an-kaliforam-pañova, hahatafetera’e o tsara’ i fañina sinokitse amy bokeio; le niantofa’ o fonga ondatio i fañinay.
4 Mfumu inalamula wansembe wamkulu Hilikiya, ansembe othandizana naye ndi alonda a pa khomo kuti achotse mʼNyumba ya Yehova ziwiya zonse zopembedzera Baala ndi Asera ndiponso mafano a zinthu zamlengalenga. Yosiya anazitentha kunja kwa Yerusalemu, ku minda ya ku Chigwa cha Kidroni ndipo phulusa lake anapita nalo ku Beteli.
Linili’ i mpanjakay amy zao t’i Kil­kià mpisoroñe naho o mpisoroñe am-pi­rim­­boñañe faha-roe naho o mpitan-dalam­beio, ty hañakara’ iareo an-kivoho’ Iehovà ze fanake nanoeñe amy Baale naho an-tsamposampo naho amy valobohòn-dikerañey; le niforototoe’e alafe’ Ierosalaime an-kivo’ i Kidrone ao vaho nendese’e mb’e Betele añe ty laveno’e.
5 Iye anachotsa ansembe a mafano amene anayikidwa ndi mafumu a Yuda kuti azifukiza lubani ku malo opembedzera mafano a ku mizinda ya ku Yuda ndi kumalo ozungulira Yerusalemu, amene ankafukiza lubani kwa Baala, dzuwa, mwezi, nyenyezi ndi zinthu zonse zamlengalenga.
Nafotsa’e iaby o mpisorom-pahasive noriza’ o mpanjaka’ Iehodao hañenga amy ze toets’ abo amo rova’ Iehodào, naho amo toetse mañohoke Ierosalaimeo; le o nañenga amy Baale, amy àndroy, amy volañey, amo vasiañe mifamorohotseo, vaho amy valobohòn-dikerañeio.
6 Anachotsa fano la Asera mʼNyumba ya Yehova napita nalo kunja kwa Yerusalemu, ku Chigwa cha Kidroni, nalitentha kumeneko. Anapera fanolo ndi kukataya phulusa lake pa manda a anthu wamba.
Naaka’e añ’ anjomba’ Iehovà mb’ alafe’ Ierosalaime mb’eo, mb’an toraha’ i Kidroney o Aserào naho finorototo’e an-toraha’ i Kidrone ey naho dinemodemo’e ho bo vaho nafitse’e amo kibori’ o ana’ ondatio i debokey.
7 Iye anagwetsanso tinyumba ta ochita zachiwerewere, timene tinali mʼNyumba ya Yehova, kumene akazi ankalukirako mikanjo yovala popembedza Asera.
Narotsa’e o kibohom-borololo añ’ila’ i anjomba’ Iehovày amy fanenoñan-drakemba o tèmen’ Aseràoy.
8 Yosiya anabweretsanso ansembe onse kuchokera mʼmizinda ya Yuda, nawononga malo opembedzera mafano, kuyambira ku Geba mpaka ku Beeriseba, kumene ansembe ankafukizako lubani. Anagwetsa nyumba za milungu zimene zinali pa chipata cha Yoswa, bwanamkubwa wa mzindawo, kumanzere kwa chipata cha mzinda.
Fonga nakare’e amo rova’ Iehodao o mpisoroñeo naho nileore’e o toets’ abo nañemboha’ o mpisoroñeo mifototse e Geba pake Beeresebà vaho narotsa’e o toets’ abo am-pimoahañe i lalambei’ Iehosoà bein-tanañeio, am-pitàn-kavia an-dalambei’ i rovaio.
9 Ngakhale kuti ansembe a ku malo opembedzera mafanowo sanawalole kuti atumikire pa guwa lansembe la Yehova mu Yerusalemu, koma ankadya buledi wopanda yisiti pamodzi ndi ansembe anzawo.
ie amy zao tsy nionjom-b’ amy kitreli’ Iehovà e Ierosalaimey añe o mpisoron-toets’aboo, f’ie nitrao-pikama mofo tsi-aman-dali­vae amo rahalahi’eo.
10 Mfumu Yosiya anawononganso Tofeti, amene anali ku Chigwa cha Hinomu, kuti wina aliyense asagwiritse ntchito malowo popereka mwana wake wamwamuna kapena wamkazi pa moto kwa Moleki.
Nileore’e ty Topete, am-bavatane’ i ana’ i Hino­mey, tsy hampirangà’ ondaty añ’afo’ i Moleke ao ty ana-dahi’e ndra ty anak’ ampela’e.
11 Anachotsa pa chipata cholowera ku Nyumba ya Yehova akavalo amene mafumu a Yuda anawapereka ngati nsembe kwa dzuwa. Akavalo anali pafupi ndi bwalo la chipinda cha mkulu wina wotchedwa Natani-Meleki. Ndipo Yosiya anatentha magaleta opembedzera dzuwa.
Nafaha’e o soavala noriza’ o mpanjaka’ Iehodao amy àndroy, am-pimoahañe añ’ anjomba’ Iehovà, marine’ ty efe’ i Matane-meleke, vosie, am-pariparitse ey, vaho finorototo’e añ’ afo o sareten’ androo.
12 Anagwetsa maguwa amene mafumu a Yuda anawamanga pa denga pafupi ndi chipinda chapamwamba cha Ahazi, ndiponso maguwa amene Manase anamanga mʼmabwalo awiri a Nyumba ya Yehova. Yosiya anawachotsa kumeneko nawaphwanya ndi kutaya zidutswa zake mʼChigwa cha Kidroni.
Le naro­tsa’ i mpanjakay i kitrely an-tafo’ i efetse ambone’ i Ahkaze namboare’ o mpanjaka’ Ieho­daoy naho o kitreli’ i Menasè niranjie’e an-kiririsa roe’ i anjomba’ Iehovà eio le dinemodemo’e vaho nahifi’e an-tora­han-Kidrone ao ty debo’e.
13 Mfumuyo inawononga malo opembedzera mafano amene ali kummawa kwa Yerusalemu cha kumpoto kwa Phiri la Chiwonongeko. Maguwawa Solomoni mfumu ya Israeli inamangira Asitoreti, fano lalikazi lonyansa la Asidoni, Kemosi, fano lonyansa la Amowabu, ndi Moleki, fano lonyansa la anthu a ku Amoni.
Le nileore’ i mpanjakay o tamboho aolo’ Ierosalaime am-pitàn-kavanan-kaboan-kaleorañeo, i namboare’ i Selomò mpanjaka’ Israele amy Astorete, ty haloloa’ o nte-Tsidoneo, naho amy Kemose, ty haloloa’ o nte-Moabeo vaho amy Milkome, ty haloloa’ o ana’ i Amoneo.
14 Yosiya anaphwanya miyala ya chipembedzo ndiponso anadula mitengo ya fano la Asera ndipo anakwirira malowo ndi mafupa a anthu.
Dinoro-demo’e o saren-drahao naho finira’e o hazomangao, vaho natsafe’e taola’ ondaty o toe’eo.
15 Ngakhalenso guwa lansembe la ku Beteli, malo opembedzera mafano amene anapanga Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli, Yosiya anawononga guwalo ndi malo opembedzera mafanowo. Iye anatentha malo opembedzera mafanowo ndi kuwapera ndipo anatenthanso fano la Asera.
Le i kitrely e Beteley, naho i toets’ abo’ Iarovame namboare’ i ana’ i Nebate nampanan-kakeo Israeley; fonga narotsa’e i kitreliy naho i toets’ aboy, le finorototo’e i toets’ aboy, naho dinemodemo’e ho deboke vaho hinotomomo’e i Aserày.
16 Kenaka Yosiya anayangʼanayangʼana ndipo ataona manda amene anali pomwepo, mʼmbali mwa phiri, analamula kuti afukule mandawo ndi kutulutsa mafupa kuti awatenthe paguwapo kuti alidetse, potsatira mawu a Yehova amene munthu wa Mulungu analoseratu za zimenezi.
Ie nitolike t’Iosià, le niisa’e o kibory an-kaboañeio naho nampañitrife’e naho nakare’e amy kibory rey o taolañeo vaho finorototo’e ambone’ i kitreliy handeora’e aze, hambañe amy tsara’ Iehovà tsinei’ indatin’ Añahare nikoike irezaiy.
17 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi chizindikiro cha manda chimene ndikuwaonawo ndi chayani?” Anthu a mu mzindamo anayankha kuti, “Ndi chizindikiro cha manda a munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda amene ananeneratu zimene inu mwalichita guwa lansembe la Beteli.”
Aa hoe re, Lona’ ia o treakoo? Le hoe ondati’ i rovaio ama’e: Kibori’ indatin’ Añahare niheo mb’etoa boak’ Iehoda nitsey o raha anoe’o amy kitreli’ i Beteleioy.
18 Mfumuyo inati, “Alekeni manda amenewo, munthu asachotse mafupa ake.” Choncho anawasiya mafupa akewo pamodzi ndi mafupa a mneneri wa ku Samariya uja.
Le hoe re: Adono; ko apo’ areo ho tsiborè’ ondaty o taola’eo. Aa le nado’ iareo o taola’eo, rekets’ o taola’ i mpitoky boake Someroneio.
19 Monga momwe Yosiya anachitira ku Beteli, anachotsa ndi kuwononga nyumba za milungu zonse ndi malo opembedzera mafano amene mafumu anamanga mʼmizinda ya ku Samariya omwe anakwiyitsa Yehova.
Nafaha’ Iosià iaby o anjomban-toets’ abo an-drova’ i Somerone namboare’ o mpanjaka’ Israeleo nampiviñetse Iehovào, le hene nanoe’e am’ iereo i nanoe’e e Beteley.
20 Yosiya anapha ansembe onse amene ankatumikira ku malo opembedzera mafano, anawaphera pa maguwa awo ndi kutentha mafupa awo. Kenaka iye anapita ku Yerusalemu.
Fonga zinevo’e ambone kitrely eo o mpisoron-toets’ abo taoo naho noroa’e ambone’ iereo ty taola’ ondaty; vaho nimpoly mb’e Ierosala­ime mb’eo.
21 Mfumu inalamula anthu onse kuti, “Chitani Chikondwerero cha Paska kulemekeza Yehova Mulungu wanu, motsatira zomwe zalembedwa mʼBuku la Chipangano.”
Linili’ i mpanjakay o hene ondatio, ami’ty hoe: Ambeno i fihelañ’ ambone’ Iehovà Andria­nañahare’oy, i sinokitse amy bokem-pañinaiy.
22 Paska yotere inali isanachitikepo kuyambira nthawi ya oweruza amene anatsogolera Israeli, kapenanso nthawi yonse ya mafumu a Yuda sipanachitikenso Paska ngati imeneyo.
Aa le mboe lia’e tsy nanoeñe ty fihelañ’ ambone manahake izay boak’ añ’andro’ o mpizaka nizaka Israeleo ndra amo androm-panjaka’ Israeleo naho o mpanjaka’ Iehodào;
23 Koma mʼchaka cha 18 cha Mfumu Yosiya, Paska imeneyi anachitira Yehova mu Yerusalemu.
amy taom-paha-folo-valo’ ambi’ Iosià mpanjakay ty nañambenañe i fihelañ’ ambone am’ Iehovày e Ierosalaime ao.
24 Kuwonjezera apa, Yosiya anachotsa anthu a mawula, woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, milungu ya mʼnyumba, mafano ndiponso zinthu zonse zonyansa zopezeka mu Yuda ndi Yerusalemu. Iye anachita izi pokwaniritsa lamulo lolembedwa mʼbuku limene Hilikiya analipeza mʼNyumba ya Yehova.
Fonga nafaha’ Iosià ze mpandrombo anga­tse naho jiny naho terafime naho hazomanga vaho ze hene haloloañe nizoeñe an-tane’ Iehoda naho e Ierosa­laime ao hamente ty enta’ i Hake sinokitse amy boke nioni’ i Kilkià mpisoroñey añ’anjomba’ Iehovà aoiy.
25 Yosiyayo asanalowe ufumu, ngakhale atamwalira, panalibenso mfumu ina yofanana naye imene inatembenukira kwa Yehova monga anachitira, ndi mtima wake wonse, ndi moyo wake wonse, ndi mphamvu zake zonse, motsatira Malamulo onse a Mose.
Le tsy eo ty nañirinkiriñe aze amy ze mpanjaka niaolo aze, ie nitolik’ am’ Iehovà an-kaampon’ arofo naho an-kalifo­ram-pa­ñova vaho an-kene hao­zara’e, ty amy Hà’ i Mosey; ie tsy amam-panonjohy nitroatse nanahak’ aze.
26 Komabe Yehova sanachotse mkwiyo wake woopsa, umene anali nawo pa Yuda chifukwa cha zonse zimene anachita Manase poputa mkwiyo wa Mulungu.
Fe tsy nitolik’ amy fifombo’e niforoforoy t’Iehovà, amy haviñera’e nisolebotse am’ Iehodà, ty amo fonga sigý nisigihe’ i Menasè Azeo.
27 Choncho Yehova anati, “Ndidzawachotsanso anthu a ku Yuda pamaso panga monga ndinachotsera anthu a ku Israeli ndipo ndidzawukana mzinda wa Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha, pamodzi ndi Nyumba ino imene ndinati, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo.’”
Le hoe t’Iehovà, hafahako am-pahatreavako t’Iehoda, manahake ty nañafahako Israele vaho hahifiko añe ty rova jinoboko toy naho i anjom­ba nataoko ty hoe: Ho ao i añarakoiy.
28 Ntchito zina za Yosiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Aa naho o fitoloña’ Iosià ila’eo, o raha nanoe’e iabio, tsy fa sinokitse amy bokem-pamoliliañe o mpanjaka’ Iehodaoy hao?
29 Yosiya akanali mfumu, Farao wotchedwa Neko, mfumu ya Igupto, anapita ku Mtsinje wa Yufurate kukathandiza mfumu ya ku Asiriya. Mfumu Yosiya anapita kukachita naye nkhondo, koma Neko anakumana naye ndi kumupha ku Megido.
Ie tañ’ andro’e le nionjo haname ty mpanjaka’ i Asore t’i Parò-Nekò mpanjaka’ i Mitsraime mb’an-tsaka Perate añe; nomb’ ama’e mb’eo t’Ioase, mpanjaka, fe vata’e niisa’e le zinevo’e e Megidò añe.
30 Atumiki a Yosiyayo ananyamula mtembo wake mu galeta kuchokera ku Megido mpaka ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda akeake. Ndipo anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namudzoza, ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
Nitakone’ o mpi­toro’eo an-tsarete i fañova’ey, nendese’ iereo mb’e Ierosalaime mb’eo vaho nalentek’ an-kibori’e ao. Rinambe ondati’ i taneio t’Ie­hoakaze, ie ty noriza’ iareo ho mpanjaka handimbe an-drae’e.
31 Yehowahazi anakhala mfumu ali ndi 23 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Hamutali, mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Roapolo-taoñe telo’ amby t’Ie­ho­­akaze te niorotse nifehe, le nifeleke telo volañe e Ierosalaime ao; i Kamotale, ana’ Irm-meà nte-Libnà, ty tahi­nan-drene’e.
32 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Nanao haratiañe am-pivazohoa’ Iehovà re manahake o fonga satan-droae’eo.
33 Farao Neko anamuyika mʼndende ku Ribula mʼdziko la Hamati kuti asalamulirenso mu Yerusalemu. Farao analamula Yuda kuti azikhoma msonkho wa siliva wolemera makilogalamu 3,400, ndiponso golide wolemera makilogalamu 34.
Le vinaho’ i Parò-Neko e Ribà an-tane Kamate añe re, tsy hameleha’e t’Ierosalaime; le sinaze’e ta­lenta zato volafoty naho talenta volamena raike i taney.
34 Farao Neko anayika Eliyakimu mwana wa Yosiya kuti akhale mfumu mʼmalo mwa abambo ake Yosiya, ndipo anasintha dzina lake kukhala Yehoyakimu. Koma iye anatenga Yehowahazi kupita naye ku Igupto ndipo anakafera kumeneko.
Le nanoe’ i Parò-Neko mpanjaka t’i Eliakime ana’ Iosia han­dimbe an-drae’e Iosia naho novae’e ho Iehoiakime ty tahina’e naho nendese’e mb’e Mitsraime mb’eo t’Iehoakaze, vaho nihomake añe.
35 Yehoyakimu anapereka kwa Farao Neko siliva ndi golide amene anamufuna uja. Koma kuti iye apereke zimenezi, amankhometsa msonkho mʼdziko mwakemo ndipo amalandira siliva ndi golide kuchokera kwa anthu a mʼdzikomo molingana ndi chuma cha munthu aliyense.
Natolo’ Iehoiakime amy Parò i volafoty naho volamenay, le nangalà’e haba i taney ty amy lili’ i Paròy; rinambe’e am’ ondati’ i taneio i volafoty naho volamenay, sambe ty amy vili-loha’ey, hanolotse aze amy Parò-Neko.
36 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Zebuda, mwana wa Pedaya wa ku Ruma.
Roapolo-taoñe lime amby t’Iehoiakime te niorotse nifehe; vaho nifeleke folo-taoñe raik’ amby e Ierosalaime ao; i Zebidà, ana’ i Pedaià nte-Romà, ty tahinan-drene’e.
37 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Le nanao haratiañe am-pivazohoa’ Iehovà re manahake o satan-droae’eo.

< 2 Mafumu 23 >