< 2 Mafumu 23 >

1 Pamenepo mfumu inayitanitsa akuluakulu onse a ku Yuda ndi Yerusalemu.
Et le roi envoya, et on assembla vers lui tous les anciens de Juda et de Jérusalem.
2 Mfumuyo inapita ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi anthu onse a ku Yuda, ndi onse okhala mu Yerusalemu, ansembe ndi aneneri, ndiponso anthu ena onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. Mfumuyo inawerenga mawu onse a mʼBuku la Chipangano limene linapezeka mʼNyumba ya Yehova, anthu onse akumva.
Et le roi monta à la maison de l’Éternel, et avec lui tous les hommes de Juda, et tous les habitants de Jérusalem, et les sacrificateurs, et les prophètes, et tout le peuple, depuis le petit jusqu’au grand: et on lut, eux l’entendant, toutes les paroles du livre de l’alliance qui avait été trouvé dans la maison de l’Éternel.
3 Mfumu inayimirira pambali pa chipilala ndi kuchita pangano pamaso pa Yehova kuti idzatsatira Yehova ndi kusunga malamulo, mawu ndi malangizo ake ndi mtima wonse ndi moyo wonse, kukwaniritsa mawu a mʼpanganoli, olembedwa mʼbukuli. Pamenepo anthu onse anadzipereka kutsatira panganoli.
Et le roi se tint debout sur l’estrade, et fit cette alliance devant l’Éternel, de marcher après l’Éternel, et de garder ses commandements, et ses témoignages, et ses statuts, de tout [son] cœur et de toute [son] âme, pour accomplir les paroles de cette alliance, écrites dans ce livre; et tout le peuple entra dans l’alliance.
4 Mfumu inalamula wansembe wamkulu Hilikiya, ansembe othandizana naye ndi alonda a pa khomo kuti achotse mʼNyumba ya Yehova ziwiya zonse zopembedzera Baala ndi Asera ndiponso mafano a zinthu zamlengalenga. Yosiya anazitentha kunja kwa Yerusalemu, ku minda ya ku Chigwa cha Kidroni ndipo phulusa lake anapita nalo ku Beteli.
Et le roi commanda à Hilkija, le grand sacrificateur, et aux sacrificateurs de la seconde [classe], et aux gardiens du seuil, d’emporter hors du temple de l’Éternel tous les objets qui avaient été faits pour Baal, et pour l’ashère, et pour toute l’armée des cieux; et il les brûla en dehors de Jérusalem, dans les champs du Cédron, et il en porta la poussière à Béthel.
5 Iye anachotsa ansembe a mafano amene anayikidwa ndi mafumu a Yuda kuti azifukiza lubani ku malo opembedzera mafano a ku mizinda ya ku Yuda ndi kumalo ozungulira Yerusalemu, amene ankafukiza lubani kwa Baala, dzuwa, mwezi, nyenyezi ndi zinthu zonse zamlengalenga.
Et il supprima les Camarim, que les rois de Juda avaient établis pour faire fumer l’encens sur les hauts lieux dans les villes de Juda et dans les environs de Jérusalem, et ceux qui brûlaient de l’encens à Baal, au soleil, et à la lune, et au zodiaque, et à toute l’armée des cieux.
6 Anachotsa fano la Asera mʼNyumba ya Yehova napita nalo kunja kwa Yerusalemu, ku Chigwa cha Kidroni, nalitentha kumeneko. Anapera fanolo ndi kukataya phulusa lake pa manda a anthu wamba.
Et il fit emporter l’ashère hors de la maison de l’Éternel, hors de Jérusalem, dans la vallée du Cédron, et il la brûla dans la vallée du Cédron, et la réduisit en poussière, et en jeta la poussière sur les sépulcres des fils du peuple.
7 Iye anagwetsanso tinyumba ta ochita zachiwerewere, timene tinali mʼNyumba ya Yehova, kumene akazi ankalukirako mikanjo yovala popembedza Asera.
Et il démolit les maisons des prostituées qui étaient dans la maison de l’Éternel, [et] où les femmes tissaient des tentes pour l’ashère.
8 Yosiya anabweretsanso ansembe onse kuchokera mʼmizinda ya Yuda, nawononga malo opembedzera mafano, kuyambira ku Geba mpaka ku Beeriseba, kumene ansembe ankafukizako lubani. Anagwetsa nyumba za milungu zimene zinali pa chipata cha Yoswa, bwanamkubwa wa mzindawo, kumanzere kwa chipata cha mzinda.
Et il fit venir des villes de Juda tous les sacrificateurs, et souilla les hauts lieux où les sacrificateurs faisaient fumer de l’encens, depuis Guéba jusqu’à Beër-Shéba; et il démolit les hauts lieux des portes, qui étaient à l’entrée de la porte de Josué, chef de la ville, [et ceux] qui étaient à la gauche d’un homme [entrant] dans la porte de la ville.
9 Ngakhale kuti ansembe a ku malo opembedzera mafanowo sanawalole kuti atumikire pa guwa lansembe la Yehova mu Yerusalemu, koma ankadya buledi wopanda yisiti pamodzi ndi ansembe anzawo.
Toutefois les sacrificateurs des hauts lieux ne montaient pas vers l’autel de l’Éternel à Jérusalem, mais ils mangeaient des pains sans levain au milieu de leurs frères.
10 Mfumu Yosiya anawononganso Tofeti, amene anali ku Chigwa cha Hinomu, kuti wina aliyense asagwiritse ntchito malowo popereka mwana wake wamwamuna kapena wamkazi pa moto kwa Moleki.
Et il souilla Topheth, qui est dans la vallée des fils de Hinnom, afin que personne ne fasse passer par le feu son fils ou sa fille au Moloc.
11 Anachotsa pa chipata cholowera ku Nyumba ya Yehova akavalo amene mafumu a Yuda anawapereka ngati nsembe kwa dzuwa. Akavalo anali pafupi ndi bwalo la chipinda cha mkulu wina wotchedwa Natani-Meleki. Ndipo Yosiya anatentha magaleta opembedzera dzuwa.
Et il abolit les chevaux que les rois de Juda avaient donnés au soleil, à l’entrée de la maison de l’Éternel, vers la chambre de Nethan-Mélec, l’eunuque, qui était dans les dépendances [du temple]; et il brûla au feu les chars du soleil.
12 Anagwetsa maguwa amene mafumu a Yuda anawamanga pa denga pafupi ndi chipinda chapamwamba cha Ahazi, ndiponso maguwa amene Manase anamanga mʼmabwalo awiri a Nyumba ya Yehova. Yosiya anawachotsa kumeneko nawaphwanya ndi kutaya zidutswa zake mʼChigwa cha Kidroni.
Et le roi démolit les autels qui étaient sur le toit de la chambre haute d’Achaz, que les rois de Juda avaient faits, et les autels que Manassé avait faits dans les deux parvis de la maison de l’Éternel; et il les brisa, [les ôtant] de là, et en jeta la poussière dans la vallée du Cédron.
13 Mfumuyo inawononga malo opembedzera mafano amene ali kummawa kwa Yerusalemu cha kumpoto kwa Phiri la Chiwonongeko. Maguwawa Solomoni mfumu ya Israeli inamangira Asitoreti, fano lalikazi lonyansa la Asidoni, Kemosi, fano lonyansa la Amowabu, ndi Moleki, fano lonyansa la anthu a ku Amoni.
Et le roi souilla les hauts lieux qui étaient en face de Jérusalem, à la droite de la montagne de corruption, que Salomon, roi d’Israël, avait bâtis pour Ashtoreth, l’abomination des Sidoniens, et pour Kemosh, l’abomination de Moab, et pour Milcom, l’abomination des fils d’Ammon;
14 Yosiya anaphwanya miyala ya chipembedzo ndiponso anadula mitengo ya fano la Asera ndipo anakwirira malowo ndi mafupa a anthu.
et il brisa les statues, et coupa les ashères, et remplit d’ossements d’hommes les lieux où ils étaient.
15 Ngakhalenso guwa lansembe la ku Beteli, malo opembedzera mafano amene anapanga Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli, Yosiya anawononga guwalo ndi malo opembedzera mafanowo. Iye anatentha malo opembedzera mafanowo ndi kuwapera ndipo anatenthanso fano la Asera.
Et l’autel qui était à Béthel, le haut lieu qu’avait fait Jéroboam, fils de Nebath, qui fit pécher Israël, cet autel-là aussi et le haut lieu, il les démolit; et il brûla le haut lieu, le réduisit en poussière, et brûla l’ashère.
16 Kenaka Yosiya anayangʼanayangʼana ndipo ataona manda amene anali pomwepo, mʼmbali mwa phiri, analamula kuti afukule mandawo ndi kutulutsa mafupa kuti awatenthe paguwapo kuti alidetse, potsatira mawu a Yehova amene munthu wa Mulungu analoseratu za zimenezi.
Et Josias se tourna et vit les sépulcres qui étaient là dans la montagne; et il envoya prendre les ossements des sépulcres, et il les brûla sur l’autel et le souilla, selon la parole de l’Éternel qu’avait proclamée l’homme de Dieu qui proclama ces choses.
17 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi chizindikiro cha manda chimene ndikuwaonawo ndi chayani?” Anthu a mu mzindamo anayankha kuti, “Ndi chizindikiro cha manda a munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda amene ananeneratu zimene inu mwalichita guwa lansembe la Beteli.”
Et [le roi] dit: Quel est ce monument que je vois? Et les hommes de la ville lui dirent: C’est le sépulcre de l’homme de Dieu qui vint de Juda, et qui proclama ces choses que tu as faites sur l’autel de Béthel.
18 Mfumuyo inati, “Alekeni manda amenewo, munthu asachotse mafupa ake.” Choncho anawasiya mafupa akewo pamodzi ndi mafupa a mneneri wa ku Samariya uja.
Et il dit: Laissez-le reposer; que personne ne remue ses os! Et ils préservèrent ses os ainsi que les os du prophète qui était venu de Samarie.
19 Monga momwe Yosiya anachitira ku Beteli, anachotsa ndi kuwononga nyumba za milungu zonse ndi malo opembedzera mafano amene mafumu anamanga mʼmizinda ya ku Samariya omwe anakwiyitsa Yehova.
Et Josias ôta aussi toutes les maisons des hauts lieux que les rois d’Israël avaient faites dans les villes de Samarie pour provoquer à colère [l’Éternel]; et il leur fit selon tout ce qu’il avait fait à Béthel.
20 Yosiya anapha ansembe onse amene ankatumikira ku malo opembedzera mafano, anawaphera pa maguwa awo ndi kutentha mafupa awo. Kenaka iye anapita ku Yerusalemu.
Et il sacrifia sur les autels tous les sacrificateurs des hauts lieux qui étaient là, et y brûla des ossements d’hommes; et il retourna à Jérusalem.
21 Mfumu inalamula anthu onse kuti, “Chitani Chikondwerero cha Paska kulemekeza Yehova Mulungu wanu, motsatira zomwe zalembedwa mʼBuku la Chipangano.”
Et le roi commanda à tout le peuple, disant: Célébrez la Pâque à l’Éternel, votre Dieu, comme il est écrit dans ce livre de l’alliance.
22 Paska yotere inali isanachitikepo kuyambira nthawi ya oweruza amene anatsogolera Israeli, kapenanso nthawi yonse ya mafumu a Yuda sipanachitikenso Paska ngati imeneyo.
Car aucune [Pâque] n’avait été célébrée comme cette Pâque, depuis les jours des juges qui ont jugé Israël, et durant tous les jours des rois d’Israël et des rois de Juda;
23 Koma mʼchaka cha 18 cha Mfumu Yosiya, Paska imeneyi anachitira Yehova mu Yerusalemu.
mais la dix-huitième année du roi Josias, cette Pâque fut célébrée à l’Éternel dans Jérusalem.
24 Kuwonjezera apa, Yosiya anachotsa anthu a mawula, woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, milungu ya mʼnyumba, mafano ndiponso zinthu zonse zonyansa zopezeka mu Yuda ndi Yerusalemu. Iye anachita izi pokwaniritsa lamulo lolembedwa mʼbuku limene Hilikiya analipeza mʼNyumba ya Yehova.
Et Josias extermina aussi les évocateurs d’esprits, et les diseurs de bonne aventure, et les théraphim, et les idoles, et toutes les abominations qui se voyaient dans le pays de Juda et à Jérusalem, afin d’effectuer les paroles de la loi, écrites dans le livre que Hilkija, le sacrificateur, avait trouvé dans la maison de l’Éternel.
25 Yosiyayo asanalowe ufumu, ngakhale atamwalira, panalibenso mfumu ina yofanana naye imene inatembenukira kwa Yehova monga anachitira, ndi mtima wake wonse, ndi moyo wake wonse, ndi mphamvu zake zonse, motsatira Malamulo onse a Mose.
Avant lui il n’y eut pas de roi semblable à lui, qui se soit retourné vers l’Éternel de tout son cœur, et de toute son âme, et de toute sa force, selon toute la loi de Moïse; et après lui, il ne s’en est pas levé de semblable à lui.
26 Komabe Yehova sanachotse mkwiyo wake woopsa, umene anali nawo pa Yuda chifukwa cha zonse zimene anachita Manase poputa mkwiyo wa Mulungu.
Toutefois l’Éternel ne revint point de l’ardeur de sa grande colère, dont il était embrasé contre Juda, à cause de toutes les provocations par lesquelles Manassé l’avait provoqué.
27 Choncho Yehova anati, “Ndidzawachotsanso anthu a ku Yuda pamaso panga monga ndinachotsera anthu a ku Israeli ndipo ndidzawukana mzinda wa Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha, pamodzi ndi Nyumba ino imene ndinati, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo.’”
Et l’Éternel dit: J’ôterai aussi Juda de devant ma face comme j’ai ôté Israël; et je rejetterai cette ville de Jérusalem que j’ai choisie, et la maison de laquelle j’ai dit: Mon nom sera là.
28 Ntchito zina za Yosiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Et le reste des actes de Josias, et tout ce qu’il fit, cela n’est-il pas écrit dans le livre des chroniques des rois de Juda?
29 Yosiya akanali mfumu, Farao wotchedwa Neko, mfumu ya Igupto, anapita ku Mtsinje wa Yufurate kukathandiza mfumu ya ku Asiriya. Mfumu Yosiya anapita kukachita naye nkhondo, koma Neko anakumana naye ndi kumupha ku Megido.
Dans ses jours, le Pharaon Neco, roi d’Égypte, monta contre le roi d’Assyrie, vers le fleuve Euphrate, et le roi Josias alla à sa rencontre; et [Neco] le tua à Meguiddo, dès qu’il le vit.
30 Atumiki a Yosiyayo ananyamula mtembo wake mu galeta kuchokera ku Megido mpaka ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda akeake. Ndipo anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namudzoza, ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
Et de Meguiddo, ses serviteurs l’emportèrent mort sur un char, et l’amenèrent à Jérusalem, et l’enterrèrent dans son sépulcre. Et le peuple du pays prit Joakhaz, fils de Josias, et ils l’oignirent et le firent roi à la place de son père.
31 Yehowahazi anakhala mfumu ali ndi 23 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Hamutali, mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Joakhaz était âgé de 23 ans lorsqu’il commença de régner; et il régna trois mois à Jérusalem; et le nom de sa mère était Hamutal, fille de Jérémie de Libna.
32 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Et il fit ce qui est mauvais aux yeux de l’Éternel, selon tout ce que ses pères avaient fait.
33 Farao Neko anamuyika mʼndende ku Ribula mʼdziko la Hamati kuti asalamulirenso mu Yerusalemu. Farao analamula Yuda kuti azikhoma msonkho wa siliva wolemera makilogalamu 3,400, ndiponso golide wolemera makilogalamu 34.
Et le Pharaon Neco le lia à Ribla, dans le pays de Hamath, pour qu’il ne règne plus à Jérusalem; et il imposa sur le pays une amende de 100 talents d’argent et d’un talent d’or.
34 Farao Neko anayika Eliyakimu mwana wa Yosiya kuti akhale mfumu mʼmalo mwa abambo ake Yosiya, ndipo anasintha dzina lake kukhala Yehoyakimu. Koma iye anatenga Yehowahazi kupita naye ku Igupto ndipo anakafera kumeneko.
Et le Pharaon Neco établit roi Éliakim, fils de Josias, à la place de Josias, son père, et changea son nom en celui de Jehoïakim; et il prit Joakhaz, qui vint en Égypte et y mourut.
35 Yehoyakimu anapereka kwa Farao Neko siliva ndi golide amene anamufuna uja. Koma kuti iye apereke zimenezi, amankhometsa msonkho mʼdziko mwakemo ndipo amalandira siliva ndi golide kuchokera kwa anthu a mʼdzikomo molingana ndi chuma cha munthu aliyense.
Et Jehoïakim donna l’argent et l’or au Pharaon; seulement il établit une taxe proportionnelle sur le pays, pour donner l’argent selon le commandement du Pharaon: il exigea l’argent et l’or du peuple du pays, de chacun selon son estimation, pour le donner au Pharaon Neco.
36 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Zebuda, mwana wa Pedaya wa ku Ruma.
Jehoïakim était âgé de 25 ans lorsqu’il commença de régner; et il régna onze ans à Jérusalem; et le nom de sa mère était Zebudda, fille de Pedaïa, de Ruma.
37 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
Et il fit ce qui est mauvais aux yeux de l’Éternel, selon tout ce que ses pères avaient fait.

< 2 Mafumu 23 >