< 2 Mafumu 23 >
1 Pamenepo mfumu inayitanitsa akuluakulu onse a ku Yuda ndi Yerusalemu.
And thei telden to the kyng that, that sche seide; `which kyng sente, and alle the elde men of Juda, and of Jerusalem, weren gaderid to hym.
2 Mfumuyo inapita ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi anthu onse a ku Yuda, ndi onse okhala mu Yerusalemu, ansembe ndi aneneri, ndiponso anthu ena onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. Mfumuyo inawerenga mawu onse a mʼBuku la Chipangano limene linapezeka mʼNyumba ya Yehova, anthu onse akumva.
And the kyng stiede in to the temple of the Lord, and alle the men of Juda, and alle men that dwelliden in Jerusalem with hym, the preestis, and the prophetis, and al the puple, fro litil `til to greet; and he redde, while alle men herden, alle the wordis of the book of boond of pees of the Lord, which book was foundun in the hows of the Lord.
3 Mfumu inayimirira pambali pa chipilala ndi kuchita pangano pamaso pa Yehova kuti idzatsatira Yehova ndi kusunga malamulo, mawu ndi malangizo ake ndi mtima wonse ndi moyo wonse, kukwaniritsa mawu a mʼpanganoli, olembedwa mʼbukuli. Pamenepo anthu onse anadzipereka kutsatira panganoli.
And the kyng stood on the grees; and he smoot boond of pees bifor the Lord, that thei schulden go aftir the Lord, and kepe hise comaundementis and witnessyngis and cerymonyes in al the herte and in al the soule, that thei schulden reise the wordis of this boond of pees, that weren writun in that book; and the puple assentide to the couenaunt.
4 Mfumu inalamula wansembe wamkulu Hilikiya, ansembe othandizana naye ndi alonda a pa khomo kuti achotse mʼNyumba ya Yehova ziwiya zonse zopembedzera Baala ndi Asera ndiponso mafano a zinthu zamlengalenga. Yosiya anazitentha kunja kwa Yerusalemu, ku minda ya ku Chigwa cha Kidroni ndipo phulusa lake anapita nalo ku Beteli.
And the kyng comaundide to Helchie, the bischop, and to the preestis of the secounde ordre, and to the porteris, that thei schulden caste out of the temple alle the vesselis, that weren maad to Baal, and in the wode, and to al the knyythod of heuene; and he brente tho vessels with out Jerusalem, in the euene valey of Cedron, and he bar the poudir of tho `vessels in to Bethel.
5 Iye anachotsa ansembe a mafano amene anayikidwa ndi mafumu a Yuda kuti azifukiza lubani ku malo opembedzera mafano a ku mizinda ya ku Yuda ndi kumalo ozungulira Yerusalemu, amene ankafukiza lubani kwa Baala, dzuwa, mwezi, nyenyezi ndi zinthu zonse zamlengalenga.
And he dide awei false dyuynours `that dyuynyden in the entrailis of beestis sacrified to idols, whiche the kingis of Juda hadden sett to make sacrifice in hiy thingis bi the citees of Juda, and in the cumpas of Jerusalem; and he dide awey hem that brenten encense to Baal, and to the sunne, and to the moone, and to twelue signes, and to al the knyythod of heuene.
6 Anachotsa fano la Asera mʼNyumba ya Yehova napita nalo kunja kwa Yerusalemu, ku Chigwa cha Kidroni, nalitentha kumeneko. Anapera fanolo ndi kukataya phulusa lake pa manda a anthu wamba.
And he made the wode to be borun out of the hows of the Lord without Jerusalem in the euene valey of Cedron, and he brente it there; and he droof it in to poudir, and castide it forth on the sepulcris of the comyn puple.
7 Iye anagwetsanso tinyumba ta ochita zachiwerewere, timene tinali mʼNyumba ya Yehova, kumene akazi ankalukirako mikanjo yovala popembedza Asera.
Also he distriede the litle housis of `men turnyd into wommens condiciouns, whiche housis weren in the hows of the Lord; for whiche the wymmen `maden as litil howsis of the wode.
8 Yosiya anabweretsanso ansembe onse kuchokera mʼmizinda ya Yuda, nawononga malo opembedzera mafano, kuyambira ku Geba mpaka ku Beeriseba, kumene ansembe ankafukizako lubani. Anagwetsa nyumba za milungu zimene zinali pa chipata cha Yoswa, bwanamkubwa wa mzindawo, kumanzere kwa chipata cha mzinda.
And he gaderide alle the preestis fro the citees of Juda, and he defoulide the hiye thingis, where the preestis maden sacrifice, fro Gabaa `til to Bersabee; and he distriede the auters of yatis in the entryng of the dore of Josie, prince of a citee, which dore was at the lift half of the yate of the cytee.
9 Ngakhale kuti ansembe a ku malo opembedzera mafanowo sanawalole kuti atumikire pa guwa lansembe la Yehova mu Yerusalemu, koma ankadya buledi wopanda yisiti pamodzi ndi ansembe anzawo.
Netheles the preestis of hiye thingis stieden not to the auter of the Lord in Jerusalem, but oneli thei eten therf looues in the myddis of her britheren.
10 Mfumu Yosiya anawononganso Tofeti, amene anali ku Chigwa cha Hinomu, kuti wina aliyense asagwiritse ntchito malowo popereka mwana wake wamwamuna kapena wamkazi pa moto kwa Moleki.
Also he defoulide Tophet, which is in the euene valey of the sone of Ennon, that no man schulde halewe his sone ether his douytir bi fier to Moloch.
11 Anachotsa pa chipata cholowera ku Nyumba ya Yehova akavalo amene mafumu a Yuda anawapereka ngati nsembe kwa dzuwa. Akavalo anali pafupi ndi bwalo la chipinda cha mkulu wina wotchedwa Natani-Meleki. Ndipo Yosiya anatentha magaleta opembedzera dzuwa.
Also he dide awei horsis, whiche the kyngis of Juda hadden youe to the sunne, in the entryng of the temple of the Lord, bisidis the chaumbir of Nathanmalech, geldyng, that was in Pharurym; forsothe he brente bi fier the charis of the sunne.
12 Anagwetsa maguwa amene mafumu a Yuda anawamanga pa denga pafupi ndi chipinda chapamwamba cha Ahazi, ndiponso maguwa amene Manase anamanga mʼmabwalo awiri a Nyumba ya Yehova. Yosiya anawachotsa kumeneko nawaphwanya ndi kutaya zidutswa zake mʼChigwa cha Kidroni.
Also the kyng distriede the auteris, that weren on the roouys of the soler of Achaz, whiche auteris the kyngis of Juda hadden maad; and the kyng distriede the auteris, whiche Manasses hadde maad in the twei grete placis of the temple of the Lord; and he ran fro thennus, and scateride the askis of tho in to the strond of Cedron.
13 Mfumuyo inawononga malo opembedzera mafano amene ali kummawa kwa Yerusalemu cha kumpoto kwa Phiri la Chiwonongeko. Maguwawa Solomoni mfumu ya Israeli inamangira Asitoreti, fano lalikazi lonyansa la Asidoni, Kemosi, fano lonyansa la Amowabu, ndi Moleki, fano lonyansa la anthu a ku Amoni.
Also the kyng defoulide the hiye thingis, that weren in Jerusalem at the riyt part of the hil of offencioun, whiche Salomon, kyng of Israel, hadde bildid to Astroth, the ydol of Sidoneis, and to Chamos, the offencioun of Moab, and to Melchon, abhominacioun of the sones of Amon;
14 Yosiya anaphwanya miyala ya chipembedzo ndiponso anadula mitengo ya fano la Asera ndipo anakwirira malowo ndi mafupa a anthu.
and he al to-brak ymagis, and kittide doun wodis, and fillide the places of tho with the boonys of deed men.
15 Ngakhalenso guwa lansembe la ku Beteli, malo opembedzera mafano amene anapanga Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli, Yosiya anawononga guwalo ndi malo opembedzera mafanowo. Iye anatentha malo opembedzera mafanowo ndi kuwapera ndipo anatenthanso fano la Asera.
Ferthermore also he distriede the auter that was in Bethel, and `he distriede the hiye thing, which Jeroboam, sone of Nabath, hadde maad, that made Israel to do synne; and he distriede that hiy autir, and brente it, and al to brak it in to poudir, and kittide doun also the wode.
16 Kenaka Yosiya anayangʼanayangʼana ndipo ataona manda amene anali pomwepo, mʼmbali mwa phiri, analamula kuti afukule mandawo ndi kutulutsa mafupa kuti awatenthe paguwapo kuti alidetse, potsatira mawu a Yehova amene munthu wa Mulungu analoseratu za zimenezi.
And Josias turnyde, and siy there sepulcris that weren in the hil; and he sente, and took the boonys fro the sepulcris, and brente tho on the auter, and defoulide it bi the word of the Lord, which word the man of God spak, that biforseide these wordis.
17 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi chizindikiro cha manda chimene ndikuwaonawo ndi chayani?” Anthu a mu mzindamo anayankha kuti, “Ndi chizindikiro cha manda a munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda amene ananeneratu zimene inu mwalichita guwa lansembe la Beteli.”
And the kyng seide, What is this biriel, which Y se? And the citeseyns of that citee answeriden to hym, It is the sepulcre of the man of God, that cam fro Juda, and biforseide these wordis, whiche thou hast doon on the auter of Bethel.
18 Mfumuyo inati, “Alekeni manda amenewo, munthu asachotse mafupa ake.” Choncho anawasiya mafupa akewo pamodzi ndi mafupa a mneneri wa ku Samariya uja.
And the kyng seide, Suffre ye hym; no man moue hise boonys. And hise boonys dwelliden vntouchid with the boones of the prophete, that cam fro Samarie.
19 Monga momwe Yosiya anachitira ku Beteli, anachotsa ndi kuwononga nyumba za milungu zonse ndi malo opembedzera mafano amene mafumu anamanga mʼmizinda ya ku Samariya omwe anakwiyitsa Yehova.
Ferthermore also Josias dide awei alle the templis of hiye thingis, that weren in the citees of Samarie, whiche the kyngis of Israel hadden maad to terre the Lord to ire; and he dide to tho templis bi alle thingis whiche he hadde do in Bethel.
20 Yosiya anapha ansembe onse amene ankatumikira ku malo opembedzera mafano, anawaphera pa maguwa awo ndi kutentha mafupa awo. Kenaka iye anapita ku Yerusalemu.
And he killide alle the preestis of hiye thingis, that weren there on the auteris, and he brente mennus boonus on tho auteris; and he turnede ayen to Jerusalem;
21 Mfumu inalamula anthu onse kuti, “Chitani Chikondwerero cha Paska kulemekeza Yehova Mulungu wanu, motsatira zomwe zalembedwa mʼBuku la Chipangano.”
and comaundide to al the puple, and seide, Make ye pask to `youre Lord God, vp that, that is writun in the book of this boond of pees.
22 Paska yotere inali isanachitikepo kuyambira nthawi ya oweruza amene anatsogolera Israeli, kapenanso nthawi yonse ya mafumu a Yuda sipanachitikenso Paska ngati imeneyo.
Forsothe sich pask was not maad, fro the daies of iugis that demyden Israel, and of alle daies of the kyngis of Israel and of Juda,
23 Koma mʼchaka cha 18 cha Mfumu Yosiya, Paska imeneyi anachitira Yehova mu Yerusalemu.
as this pask was maad to the Lord in Jerusalem in the eiytenthe yeer of kyng Josias.
24 Kuwonjezera apa, Yosiya anachotsa anthu a mawula, woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, milungu ya mʼnyumba, mafano ndiponso zinthu zonse zonyansa zopezeka mu Yuda ndi Yerusalemu. Iye anachita izi pokwaniritsa lamulo lolembedwa mʼbuku limene Hilikiya analipeza mʼNyumba ya Yehova.
But also Josias dide awei men hauynge fendis spekinge in her wombis, and false diuinouris in auteris, and `he dide awei the figuris of idols, and alle vnclennessis, and abhomynaciouns, that weren in the lond of Juda and in Jerusalem, that he schulde do the wordis of the lawe, that weren writun in the book, `which book Elchie, the preest, foond in the temple of the Lord.
25 Yosiyayo asanalowe ufumu, ngakhale atamwalira, panalibenso mfumu ina yofanana naye imene inatembenukira kwa Yehova monga anachitira, ndi mtima wake wonse, ndi moyo wake wonse, ndi mphamvu zake zonse, motsatira Malamulo onse a Mose.
No kyng bifor him was lijk hym, `that turnede ayen to the Lord in al his herte, and in al his soule, and in al his vertu, bi al the lawe of Moises; nether aftir hym roos ony lijk hym.
26 Komabe Yehova sanachotse mkwiyo wake woopsa, umene anali nawo pa Yuda chifukwa cha zonse zimene anachita Manase poputa mkwiyo wa Mulungu.
Netheles the Lord was not turned awei fro the ire of his greet veniaunce, bi which his strong veniaunce was wrooth ayens Juda, for the terryngis to ire by whiche Manasses hadde terrid hym to ire.
27 Choncho Yehova anati, “Ndidzawachotsanso anthu a ku Yuda pamaso panga monga ndinachotsera anthu a ku Israeli ndipo ndidzawukana mzinda wa Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha, pamodzi ndi Nyumba ino imene ndinati, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo.’”
Therfor the Lord seide, Y schal do awei also Juda fro my face, as Y dide awei Israel; and Y schal caste awei this citee, which Y chees, Jerusalem, and the hows `of which Y seide, My name schal be there.
28 Ntchito zina za Yosiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Forsothe the residue of wordis of Josias, and alle thingis whiche he dide, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Juda?
29 Yosiya akanali mfumu, Farao wotchedwa Neko, mfumu ya Igupto, anapita ku Mtsinje wa Yufurate kukathandiza mfumu ya ku Asiriya. Mfumu Yosiya anapita kukachita naye nkhondo, koma Neko anakumana naye ndi kumupha ku Megido.
In the daies of hym Farao Nechao, kyng of Egipt, stiede ayens the kyng of Assiriens, to the flood Eufrates; and Josias, kyng of Juda, yede in to metyng of hym, and Josias was slayn in Magedo, whanne he hadde seyn hym.
30 Atumiki a Yosiyayo ananyamula mtembo wake mu galeta kuchokera ku Megido mpaka ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda akeake. Ndipo anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namudzoza, ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.
And `hise seruauntis baren hym deed fro Magedo, and brouyte him in to Jerusalem, and birieden hym in his sepulcre; and the puple of the lond took Joachaz, sone of Josias, and anoyntiden hym, and maden hym kyng for his fadir.
31 Yehowahazi anakhala mfumu ali ndi 23 ndipo analamulira mu Yerusalemu miyezi itatu. Amayi ake anali Hamutali, mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
Joachaz was of thre and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede thre monethis in Jerusalem; the name of his modir was Amychal, douyter of Jeremye of Lobna.
32 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
And he dide yuel bifor the Lord, bi alle thingis which hise fadris hadden do.
33 Farao Neko anamuyika mʼndende ku Ribula mʼdziko la Hamati kuti asalamulirenso mu Yerusalemu. Farao analamula Yuda kuti azikhoma msonkho wa siliva wolemera makilogalamu 3,400, ndiponso golide wolemera makilogalamu 34.
And Farao Nechao boond hym in Reblatha, which is in the lond of Emath, that he schulde not regne in Jerusalem; and he settide `peyne, ether raunsum, to the lond, in an hundrid talentis of siluer, and in a talent of gold.
34 Farao Neko anayika Eliyakimu mwana wa Yosiya kuti akhale mfumu mʼmalo mwa abambo ake Yosiya, ndipo anasintha dzina lake kukhala Yehoyakimu. Koma iye anatenga Yehowahazi kupita naye ku Igupto ndipo anakafera kumeneko.
And Farao Nechao made kyng Eliachim, sone of Josias, for Josias, his fadir; and he turnede the name of hym Joachym; forsothe Farao took Joachaz, and ledde hym in to Egipt.
35 Yehoyakimu anapereka kwa Farao Neko siliva ndi golide amene anamufuna uja. Koma kuti iye apereke zimenezi, amankhometsa msonkho mʼdziko mwakemo ndipo amalandira siliva ndi golide kuchokera kwa anthu a mʼdzikomo molingana ndi chuma cha munthu aliyense.
Sotheli Joachym yaf siluer and gold to Farao, whanne he hadde comaundid to the lond bi alle yeeris, that it schulde be brouyt, bi the comaundement of Farao; and he reiside of ech man bi hise myytis bothe siluer and gold, of the puple of the lond, that he schulde yyue to Pharao Nechao.
36 Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Amayi ake anali Zebuda, mwana wa Pedaya wa ku Ruma.
Joachym was of fyue and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede eleuene yeer in Jerusalem; the name of his modir was Zebida, douyter of Phadaia of Ruma.
37 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe anachitira makolo ake.
And he dide yuel bifor the Lord, bi alle thingis which hise fadris hadden do.