< 2 Mafumu 22 >

1 Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
Сын осми лет бе Иосиа, егда нача царствовати, и тридесять едино лето царствова во Иерусалиме. Имя же матери его Иедида, дщи Едеева, от Васурофа.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
И сотвори правое пред очима Господнима, и хождаше во всех путех Давида отца своего, не совратися ни на десно, ни на шуее.
3 Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
И бысть во осмоенадесять лето царства Иосиина, в седмый месяц, посла царь Сафана, сына Езелиина, сына Месолламля, книгочию дому Господня, глаголя:
4 “Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
взыди к Хелкии жерцу великому и запечатлей сребро внесеное в дом Господень, еже собраша стрегущии врат от людий,
5 Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
и да дадут е в руки творящих дела приставником в храме Господни: да дадят е творящым дела в дому Господни, еже подкрепляти разселины храма,
6 amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
древоделем и каменосечцем и покупающым древа и камение тесаное на утверждение разселин храма.
7 Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
Обаче не сочисляху их о сребре даемем им, яко верно тии творяху.
8 Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
И рече Хелкиа жрец великий ко Сафану книгочию: книгу закона (Божия) обретох в дому Господни. И даде Хелкиа книгу Сафану, и прочте ю.
9 Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
И вниде в дом Господень и царю Иосии, и возвести царю слово и рече: слияша раби твои сребро обретшееся в дому Господни, и даша е приставницы в руки творящым дела в храме Господни.
10 Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
И рече Сафан книгочия к царю, глаголя книгу закона даде ми Хелкиа жрец. И прочте ю Сафан пред царем.
11 Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
И бысть яко услыша царь словеса книги законныя, и раздра ризы своя,
12 Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
и заповеда царь Хелкии жрецу и Ахикаму сыну Сафаню, и Аховору сыну Михеину и Сафану книгочию и Асаию рабу цареву, глаголя:
13 “Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
приидите, испросите Господа о мне и о всех людех и о всем Иуде, и о словесех книги обретшияся сея, яко велик гнев Господень разжженый на нас, понеже не послушаша отцы наши словес книги сея, еже творити по всем написанным на ны.
14 Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
И иде Хелкиа жрец и Ахикам, и Аховор и Сафан и Асаиас ко Олдаме пророчице, жене Селима сына Фекуева, сына Араса ризохранителя: и сия живяше во Иерусалиме в масене: и глаголаша к ней по сему.
15 Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
И рече им: сице глаголет Господь Бог Израилев: рцыте мужеви пославшему вы ко мне:
16 ‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
тако глаголет Господь: се, Аз наведу злая на место сие и на живущыя в нем, вся словеса книжная, яже прочте царь Иудин:
17 Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
понеже оставиша Мя и кадяху богом другим, яко да прогневают Мя делесы рук своих, и разжжется ярость Моя на место сие и не угаснет:
18 Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
и ко царю Иудину пославшему вас вопросити Господа, сице рцыте ему: тако глаголет Господь Бог Израилев: словеса, яже слышал еси,
19 Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
за сия, яко умягчися сердце твое и смирился еси пред лицем Господним, услышав елика глаголах на место сие и на живущыя в нем, еже быти в погубление и в проклятие, и раздрал еси ризы твоя, и плакался предо Мною, и Аз убо услышах, глаголет Господь:
20 Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.
сего ради Аз приложу тя ко отцем твоим, и соберешися во гроб твой в мире, и не узриши очима твоима всех злых, яже Аз имам навести на место сие и на живущыя в нем.

< 2 Mafumu 22 >