< 2 Mafumu 22 >

1 Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
UJosiya waba yinkosi eleminyaka eyisificaminwembili eqalisa ukubusa njalo wabusa eJerusalema okweminyaka engamatshumi amathathu lowodwa. Ibizo likanina lalinguJedida indodakazi ka-Adaya; wayevela eBhozikhathi.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
Wenza okulungileyo emehlweni kaThixo njalo wahamba ezindleleni zonke zikayise uDavida, engaphambukeli eceleni kwesokudla loba esenxele.
3 Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
Ngomnyaka wetshumi lasificaminwembili wokubusa kwakhe, uJosiya inkosi wathumela unobhala wakhe, uShafani indodana ka-Azaliya, indodana kaMeshulami, ethempelini likaThixo. Wathi,
4 “Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
“Hamba uye kuHilikhiya umphristi omkhulu uyekuthi kalungise imali elethwe ethempelini likaThixo, ekade iqoqwa ebantwini ngabalindi beminyango.
5 Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
Abayigcinise amadoda akhethelwe ukukhangela ukuqhubeka komsebenzi ethempelini. Babe yibo abazaholisa abasebenza ukulungisa kutsha ithempeli likaThixo,
6 amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
ababazi, abakhi, lababazi bamatshe. Babe yibo njalo abazathenga amapulanka lamatshe abaziweyo okulungisa kutsha ithempeli.
7 Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
Kodwa akudingeki ukuthi babike ngokusetshenziswa kwemali abayigcinisiweyo, ngoba basebenza ngokwethembeka.”
8 Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
UHilikhiya umphristi omkhulu wathi kuShafani unobhala, “Sengithole uGwalo lwemiThetho ethempelini likaThixo.” Walunika uShafani walufunda.
9 Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
Ngakho uShafani waya enkosini, wayibikela wathi, “Izikhulu zakho sezibhadele imali ebisethempelini likaThixo njalo seziyigcinise izisebenzi kanye labakhangela ethempelini.”
10 Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
UShafani unobhala wasebikela inkosi esithi, “UHilikhiya umphristi usenginike ugwalo.” Ngakho uShafani waselubala phambi kwenkosi.
11 Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
Inkosi ithe isizwile amazwi eNcwadi yoMthetho, yadabula izembatho zayo.
12 Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
Yapha leziziqondiso kuHilikhiya umphristi, lo-Ahikhami indodana kaShafani, lo-Akhibhori indodana kaMikhaya loShafani unobhala kanye lo-Asaya inceku yenkosi, yathi:
13 “Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
“Hambani kuThixo liyengibuzela mina labantu kanye loJuda wonke ngalokhu okulotshwe kulolugwalo osolutholakele. Lukhulu ulaka lukaThixo oluvuthayo kithi ngoba okhokho bethu kabawalalelanga amazwi alolugwalo: abakulandelanga konke okulotshiweyo kulo mayelana lathi.”
14 Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
UHilikhiya umphristi, lo-Ahikhami, lo-Akhibhori, loShafani lo-Asaya bayakhuluma lomphrofethikazi uHulida umkaShalumi indodana kaThikhiva, indodana kaHarihasi, umgcini wezigqoko. UHulida wayehlala eJerusalema Esigabeni Sesibili.
15 Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
Yena wathi kubo: “Nanku okutshiwo nguThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli ukuthi, tshelani indoda elithume kimi ukuthi,
16 ‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
‘Nanku okutshiwo nguThixo: Ngizakwehlisela incithakalo kulindawo lasebantwini bayo ngakho konke okulotshwe egwalweni olubalwa yinkosi yakoJuda.
17 Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
Ngoba bangihlamukele, batshisela abanye onkulunkulu impepha, njalo bangithukuthelisile ngazozonke izithombe abazenze ngezandla zabo, ulaka lwami luzavutha kule indawo lungacitshwa muntu.’
18 Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
Tshelani inkosi yakoJuda yona elithume ukuzabuza kuThixo, lithi, ‘Nanku okutshiwo nguThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, mayelana lamazwi eliwazwileyo:
19 Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
Ngenxa yokuthi inhliziyo yakho ivumile njalo uzithobile phambi kukaThixo lapho usizwa engikukhulume ngendawo le labantu bayo, ukuthi bazakuba ngabaqalekisiweyo bachithwe, njalo ngenxa yokuthi udabule izigqoko zakho wakhala phambi kwami, ngikuzwile, kutsho uThixo.
20 Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.
Ngakho ngizakusa kubokhokho bakho, njalo uzangcwatshwa ngokuthula. Amehlo akho awayikuyibona incithakalo engizayehlisela kule indawo.’” Ngakho izithunywa zayithatha leyompendulo zayisa enkosini.

< 2 Mafumu 22 >