< 2 Mafumu 22 >
1 Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
Josiah was eight years old when he became the king [of Judah]. He ruled from Jerusalem for 31 years. His mother was Jedidah and his grandfather was Adaiah from Bozkath [town].
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
Josiah did things that were pleasing to Yahweh and conducted his life as his ancestor King David had done. He completely obeyed [IDM] all the laws of God.
3 Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
After Josiah had been ruling for almost 18 years, he sent his secretary Shaphan, the son of Azaliah and grandson of Meshullam, to the temple with these instructions:
4 “Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
“Go to Hilkiah, the Supreme Priest, and tell him to give me a report, telling me how much money the men who guard the doors of the temple have collected from the people [as offerings].
5 Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
Then tell him to give all that money to the men who are supervising the work of repairing the temple.
6 amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
They must give that money to the carpenters, the builders, and the masons, and they should also buy the timber and the stones that they will use to repair the temple.
7 Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
But the men who supervise the work will not be required to make a report on the money that is given to them, saying what they spent it for, because those men are completely honest.”
8 Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
[After Shaphan said that to Hilkiah] the king’s secretary, Hilkiah said to Shaphan, “I have found in the temple a scroll on which is written the laws [that God gave to Moses]!” Hilkiah gave the scroll to Shaphan, and he started to read it.
9 Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
Then Shaphan [took the scroll] to the king and said to him, “Your temple guards have taken the money that was in the temple, and they have given it to the men who will supervise the work of repairing the temple.”
10 Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
Then Shaphan said to the king, [“I have brought to you] a scroll that Hilkiah gave to me.” And Shaphan started to read it to the king.
11 Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
When the king heard the laws that were written in the scroll that Shaphan was reading to him, he tore his clothes [because he was very dismayed].
12 Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
Then he gave these instructions to Hilkiah, to Shaphan’s son Ahikam, to Micaiah’s son Achbor, and to Asaiah, the king’s special advisor:
13 “Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
“Go and ask Yahweh for me and for all the people of Judah, about what is written in this scroll that has been found. Because [it is clear that] Yahweh is very angry with us because our ancestors disobeyed what was written on this scroll, things that we [should have done].”
14 Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
So Hilkiah, Ahikam, Achbor, Shaphan, and Asaiah went to (consult/talk with) a woman whose name was Huldah, who was a prophetess who lived in the newer/northern part of Jerusalem. Her husband Shallum, son of Tikvah and grandson of Harhas, took care of the robes that were worn [in the temple] (OR, [by the king]). [Those five men told her about the scroll].
15 Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
She said to them, “This is what Yahweh the God whom we Israelis [worship] says: ‘Go back and tell the king who sent you
16 ‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
that this is what Yahweh says: “Listen to this carefully. I am going to cause all the people who live here in Jerusalem to experience a disaster, which is what was written in the scroll that the king has read.
17 Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
I will do that because they have abandoned me, and they burn incense to [honor] other gods. They have caused me to become very angry by [worshiping] the idols that they have made (OR, by all the wicked things that they have done), and my anger is like [MET] a fire that will not be put out.”
18 Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
The king of Judah sent you to inquire what I, Yahweh, wanted you to do, so this is what you should say to him: “Because you have heeded what was written in the scroll,
19 Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
and you repented and humbled yourself when you heard what I said to warn you [about what would happen to] this city and the people who live here and because you tore your robes and wept in my presence, I have heard you. I said that I would cause this city to be abandoned. It will be a city whose name people will use when they curse someone. But I have heard what you prayed,
20 Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.
so I will allow you to die [EUP] and be buried peacefully. I will cause the people who live here to experience a terrible disaster, but you will not [be alive to] see it.”’” After the men heard that, they returned to King Josiah and gave him that message.