< 2 Mafumu 22 >

1 Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
Josias var otte År gammel, da han blev Konge, og han herskede een og tredive År i Jerusalem. Hans Moder hed Jedida og var en Datter af Adaja fra Bozkat.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
Han gjorde, hvad der var ret i HERRENs Øjne, og vandrede nøje i sin Fader Davids Spor uden at vige til højre eller venstre.
3 Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
I Kong Josias's attende Regeringsår sendte Kongen Statsskriveren Sjafan, en Søn af Mesjullams Søn Azalja, til HERRENs Hus og sagde:
4 “Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
"Gå op til Ypperstepræsten Hilkija og lad ham tage de Penge frem, der er indkommet i HERRENs Hus, og som Dørvogterne har samlet ind hos Folket,
5 Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
for af man kan give Pengene til dem, der står for Arbejdet, dem, der har Tilsyn med HERRENs Hus; de skal så give dem til Arbejderne i HERRENs Hus til Istandsættelse af de brøstfældige Steder på Templet,
6 amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
til Tømrerne, Bygningsmændene og Murerne, og til Indkøb af Træ og tilhugne Sten til Templets Istandsættelse.
7 Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
Bog skal der ikke holdes Regnskab med dem over de Penge, der overlades dem, men de skal handle på Tro og Love."
8 Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
Da sagde Ypperstepræsten Hilkija til Statsskriveren Sjafan: "Jeg har fundet Lovbogen i HERRENS Hus!" Og Hilkija gav Sjafan Bogen, og han læste den.
9 Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
Derpå begav Statsskriveren Sjafan sig til Kongen og aflagde Beretning for ham og sagde: "Dine Trælle har taget de Penge frem, der fandtes i Templet, og givet dem til dem, der står for Arbejdet, dem, der har Tilsyn med HERRENs Hus."
10 Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
Derpå gav Statsskriveren Sjafan Kongen den Meddelelse: "Præsten Hilkija gav mig en Bog!" Og Sjafan læste den for Kongen.
11 Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
Men da Kongen hørte, hvad der stod i Lovbogen, sønderrev han sine Klæder;
12 Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
og Kongen bød Præsten Hilkija, Ahikam, Sjafans Søn, Akbor, Mikas Søn, Statsskriveren Sjafan og Kongens Tjener Asaja:
13 “Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
"Gå hen og rådspørg på mine og Folkets og hele Judas Vegne HERREN om Indholdet af denne Bog, der er fundet; thi stor er Vreden, der er blusset op hos HERREN imod os, fordi vore Fædre ikke har adlydt Ordene i denne Bog og ikke har handlet nøje efter, hvad der står skrevet deri."
14 Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
Præsten Hilkija, Ahikam, Akbor, Sjafan og Asaja gik da hen og talte med Profetinden Hulda, som var gift med Sjallum, Opsynsmanden over Tøjet, en Søn af Harhas's Søn Tikva, og som boede i Jerusalem i den nye Bydel.
15 Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
Hun sagde til dem: "Så siger HERREN, Israels Gud: Sig til den Mand, der sendte eder til mig:
16 ‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
Så siger HERREN: Se, jeg vil bringe Ulykke over dette Sted og dets Indbyggere, alt, hvad der står i den Bog, Judas Konge har læst,
17 Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
til Straf for at de har forladt mig og tændt Offerild for andre Guder, så at de krænkede mig med alt deres Hænders Værk, og min Vrede vil blusse op mod dette Sted uden at slukkes!
18 Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
Men til Judas Konge, der sendte eder for at rådspørge HERREN, skal I sige således: Så siger HERREN, Israels Gud: De Ord, du har hørt, står fast;
19 Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
men efterdi dit Hjerte bøjede sig og du ydmygede dig for HERREN, da du hørte, hvad jeg har talet mod dette Sted og dets Indbyggere, at de skal blive til Rædsel og Forbandelse, og efterdi du sønderrev dine Klæder og græd for mit Åsyn, så har også jeg hørt dig, lyder det fra HERREN!
20 Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.
Og jeg vil lade dig samles til dine Fædre, og du skal samles til dem i Fred i din Grav, uden at dine Øjne får al den Ulykke at se, som jeg vil bringe over defte Sted." Det Svar bragte de Kongen.

< 2 Mafumu 22 >