< 2 Mafumu 22 >

1 Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
Иосия бе осем години на възраст когато се възцари, и царува в Ерусалим тридесет и една година; а името на майка му бе Иедида, дъщаря на Адаия от Васкат.
2 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
Той върши това, което бе право пред Господа, като ходи напълно в пътя на баща си Давида, баз да се отклони на дясно или на ляво.
3 Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
И в осемнадесетата година на цар Иосия, царят прати в Господния дом секретаря Сафан, син на Азалия, Месуламовия син, и му каза:
4 “Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
Иди при първосвещеника Холкия та му речи да изброи внесените в Господния дом пари, които врътърите са събрали от людете,
5 Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
и нека ги предадат в ръката на работниците; които надзирават Господния дом; а а те нека ги дадат на работниците, които са в Господния дом, за да поправят разваленото на дома,
6 amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
на дърводелците, на строителите и на зидарите, - за да купят дървета и дялани камъни за да поправят дома.
7 Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
Обаче, не държаха с тях никаква сметка за предаваните в ръцете им пари, защото постъпваха честно.
8 Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
Тогава първосвещеникът Хелкия каза на секретаря Сафан: Намерих книгата на закона в Господния дом. И Хелкия даде книгата на Сафана, който я прочете.
9 Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
И секретарят Сафан отиде при царя и доложи на царя, казвайки: Слугите ти иждивиха парите, които намериха в дома, като ги предадоха в ръката на работниците, които надзирават Господния дом.
10 Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
Тоже секретарят Сафан извески на царя, казвайки: Свещеник Хелкия ми даде една книха. И Сафан я прочете пред царя.
11 Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
А царят, като чу думите на книгата на закона, раздра дрехите си.
12 Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
Тогава царят заповадя на свещеника Хелкия, на Ахикама Сафановия син, на Аховора Михеевия син, на секретаря Сафан, и на царския слуга Асаия, казвайки:
13 “Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
Идете, допитайте се до Господа за мене, за людете и за целия Юда, относно думите на тая книга, който се намери; защото голям е Господният гняв, който е пламнал против нас, понеже бащите ни не послушаха думите на тая книга та да постъпват напълно според както е писано за нас.
14 Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
И така, свещеник Хелкия, Ахикам, Аховор, Сафан и Асаия отидоха при пророчицата Олда, жена на одеждопазителя Селум, син на Текуя, Арасовия син. А тя живееше в Ерусалим, във втория участък; и те говориха с нея.
15 Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
И тя им рече: Така казва Господ Израилевият Бог: Кажете на човека, който ви е пратил до Мене:
16 ‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
Така казва Господ: Ето, Аз ще докарам злото на това място и на жителите му, според всичко което е писано в книгата, която Юдовият цар е прочел.
17 Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
Понеже Ме оставиха и кадяха на други богове, та Ме разгневиха с всичките дала на ръцате си, затова гневът Ми ще пламне против това място, и няма да угасне.
18 Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
Но на Юдовия цар, който ви прати да се допитате до Господа, така да му кажете: Така казва Гостпод Израилевият Бог: Относно думите, които ти си чул:
19 Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
Понеже сърцето ти е омекнало, и ти си се смирил пред Господа, когато си чул това, което говорих против това място и против жителите му, че ще запустеят и ще станат за проклетия, и ти раздра дрехите си и плака пред Мене, затова и Аз те послушах, казва Господ.
20 Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.
Ето, прочее, Аз ще те прибера при бащите ти, и ще се прибереш в гроба си с мир; и твоите очи няма да видят нищо от всичкото зло, което ще докарам на това място. И те доложиха на царя.

< 2 Mafumu 22 >