< 2 Mafumu 21 >

1 Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
Manasés tenía doce años cuando se convirtió en rey, y reinó en Jerusalén durante cincuenta y cinco años. El nombre de su madre era Hefzibá.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
Sus hechos fueron malos a los ojos del Señor, al seguir las repugnantes prácticas paganas de las naciones que el Señor había expulsado ante los israelitas.
3 Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
Reconstruyó los lugares altos que su padre Ezequías había destruido, y levantó altares para Baal. Hizo un poste de ídolos de Asera, tal como lo había hecho Acab, rey de Israel, y adoró y sirvió al sol, la luna y las estrellas.
4 Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
Levantó altares paganos en el Templo del Señor, justo donde el Señor había dicho: “Pondré mi nombre en Jerusalén para siempre”.
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
Erigió altares para adorar al sol, la luna y las estrellas en los dos patios del Templo del Señor.
6 Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
Incluso sacrificó a su propio hijo como holocausto, y utilizó la adivinación y la brujería, y trató con médiums y espiritistas. Hizo mucho mal a los ojos del Señor, haciendo que éste se enojara.
7 Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
Tomó el poste del ídolo de Asera que había hecho y lo colocó en el Templo. Este era el lugar al que se refería el Señor cuando les dijo a David y a Salomón, su hijo: “En este Templo y en Jerusalén, que he elegido entre todas las tribus de Israel, pondré mi nombre para siempre.
8 Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
Nunca más haré que los israelitas se alejen de la tierra que les di a sus antepasados si tienen cuidado de seguir todo lo que les he ordenado: toda la ley que les dio mi siervo Moisés”.
9 Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
El pueblo se negó a escuchar y Manasés los llevó a pecar, de modo que el mal que hicieron fue aún peor que el de las naciones que el Señor había destruido antes de los israelitas.
10 Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
El Señor dijo por medio de sus siervos los profetas
11 “Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
“Puesto que Manasés, rey de Judá, ha cometido todos estos repugnantes pecados, haciendo cosas aún más malas que los amorreos que vivieron antes que él, y con su fomento del culto a los ídolos ha hecho pecar a Judá,
12 Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
esto es lo que dice el Señor, el Dios de Israel: ¡Cuidado! Voy a hacer caer sobre Jerusalén y Judá un desastre tal que hará zumbar los oídos de todo el que lo oiga.
13 Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
Extenderé sobre Jerusalén el cordel de medir usado contra Samaria y la plomada usada contra la casa de Acab, y limpiaré a Jerusalén como se limpia un cuenco, limpiándolo y dándole la vuelta.
14 Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
Abandonaré al resto de mi pueblo especial y lo entregaré a sus enemigos. Serán despojo y botín para todos sus enemigos,
15 chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
porque han hecho lo que es malo a mis ojos y me han hecho enojar desde el día en que sus padres salieron de Egipto hasta hoy”.
16 Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Además, Manasés asesinó a tantos inocentes que Jerusalén se llenó de un lado a otro con su sangre. Esto se sumaba al pecado que había hecho cometer a Judá, haciendo el mal a los ojos del Señor.
17 Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
El resto de lo que sucedió en el reinado de Manasés, todo lo que hizo, así como los pecados que cometió, están registrados en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Judá.
18 Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Manasés murió y fue enterrado en el jardín de su palacio, el jardín de Uzza. Su hijo Amón le sucedió como rey.
19 Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
Amón tenía veintidós años cuando llegó a ser rey, y reinó en Jerusalén durante dos años. Su madre se llamaba Mesulémet, hija de Jaruz. Ella era de Jotba.
20 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
Sus hechos fueron malos a los ojos del Señor, tal como los de su padre Manasés.
21 Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
Siguió todos los caminos de su padre, y sirvió a los ídolos que su padre había servido, inclinándose en adoración a ellos.
22 Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
Rechazó al Señor, el Dios de sus antepasados, y no siguió el camino del Señor.
23 Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
Los funcionarios de Amón conspiraron contra él y lo asesinaron en su palacio real.
24 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Pero entonces el pueblo del país mató a todos los que habían conspirado contra el rey Amón, y eligieron a su hijo Josías como rey para sucederlo.
25 Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
El resto de lo que sucedió en el reinado de Amón, y todo lo que hizo, están registrados en el Libro de las Crónicas de los Reyes de Judá.
26 Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Fue enterrado en su tumba en el jardín de Uza, y su hijo Josías lo sucedió como rey.

< 2 Mafumu 21 >