< 2 Mafumu 21 >
1 Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
Manassé avait douze ans quand il monta sur le trône, et il régna cinquante-cinq ans à Jérusalem; sa mère se nommait Apsiba.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
Et il fit le mal aux yeux du Seigneur: les abominations des peuples que le Seigneur avait détruits devant les fils d'Israël.
3 Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
Il se pervertit, et il rebâtit les hauts lieux qu'avait abattus Ezéchias, son père; il releva l'autel de Baal; il planta des bois sacrés, comme Achab, roi d'Israël; il adora toute l'armée du ciel, et il la servit.
4 Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
Il bâtit un autel dans le temple du Seigneur, qui avait dit: En Jérusalem je placerai mon nom.
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
Et il bâtit un autel à toute l'armée du ciel, dans chacun des deux parvis du temple du Seigneur.
6 Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
Et il fit passer de ses fils dans la flamme; il usa de la divination et des augures, il consacra des enclos; il multiplia les devins, faisant le mal aux yeux du Seigneur pour l'irriter.
7 Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
L'idole du bois sacré, il la mit dans le temple, dont le Seigneur avait dit à David et à Salomon, son fils: En ce temple et en cette ville de Jérusalem, que j'ai choisie parmi toutes les tribus, je placerai mon nom pour toujours.
8 Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
Car je ne veux plus éloigner de la terre que j'ai donnée à leurs pères le pied des fils d'Israël, du moins de ceux qui garderont tout ce que j'ai prescrit, tous les commandements que leur a fait connaître Moïse, mon serviteur;
9 Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
Mais ils n'écoutèrent pas le Seigneur; Manassé les égara, pour qu'ils fissent le mal aux yeux du Seigneur, plus encore que les nations que le Seigneur avait détruites devant Israël.
10 Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
Et le Seigneur parla par la voix de ses serviteurs les prophètes, disant:
11 “Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
En punition de ce qu'a fait Manassé, de ses abominations, de ses crimes, qui surpassent ceux de l'Amorrhéen d'autrefois, de ce qu'il a fait tomber Israël dans le péché, par ses idoles,
12 Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
Il n'en sera pas ainsi. Voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël: Voilà que j'apporte à Jérusalem et à Juda des maux tels, que les oreilles de quiconque les ouïra en tinteront.
13 Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
Et j'étendrai sur Jérusalem la mesure de Samarie et le niveau de la maison d'Achab; je récurerai Jérusalem comme on récure un vase que l'on retourne sens dessus dessous en l'essuyant.
14 Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
Je répudierai les restes de mon héritage; je les livrerai aux mains de leurs ennemis; ils seront pour tous leurs ennemis une proie et un butin.
15 chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
En punition de ce qu'ils ont fait le mal à mes yeux, et de ce qu'ils n'ont jamais cessé de m'irriter, depuis que j'ai tiré leurs pères de l'Égypte jusqu'à ce jour.
16 Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Or, Manassé répandit à grands flots le sang innocent, jusqu'à ce que, d'une extrémité à l'autre, il en eût rempli Jérusalem, outre les péchés où il fit tomber Juda en faisant le mal aux yeux du Seigneur.
17 Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Quant au reste de l'histoire de Manassé, et aux péchés où il tomba, ne sont-ils pas écrits au livre des Faits et gestes des rois de Juda?
18 Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Manassé s'endormit avec ses pères; il fut enseveli dans le jardin de son palais, dans le jardin d'Oza, et son fils Amos régna à sa place.
19 Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
Amos avait vingt-deux ans quand il monta sur le trône, et il régna deux ans à Jérusalem; sa mère se nommait Mésollam, fille d'Arus de Jétéba.
20 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
Et il fit le mal aux yeux du Seigneur, comme l'avait fait Manassé, son père.
21 Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
Il marcha dans toutes les voies où son père avait marché, et il servit les idoles que son père avait servies, et il les adora.
22 Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
Il abandonna le Seigneur Dieu de ses pères; il ne marcha pas dans la voie du Seigneur.
23 Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
Et les serviteurs d'Amos conspirèrent contre lui, et ils le tuèrent dans son palais.
24 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
Alors, le peuple de la terre mit à mort ceux qui avaient conspiré contre le roi Amos, et il proclama roi Josias, son fils.
25 Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Quant au reste de l'histoire d'Amos, n'est-il pas écrit au livre des Faits et gestes des rois de Juda?
26 Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et on l'ensevelit en son sépulcre dans le jardin d'Oza, et Josias, son fils, régna à sa place.