< 2 Mafumu 21 >

1 Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
son: aged two ten year Manasseh in/on/with to reign he and fifty and five year to reign in/on/with Jerusalem and name mother his Hephzibah Hephzibah
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD like/as abomination [the] nation which to possess: take LORD from face: before son: descendant/people Israel
3 Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
and to return: rescue and to build [obj] [the] high place which to perish Hezekiah father his and to arise: raise altar to/for Baal and to make Asherah like/as as which to make: do Ahab king Israel and to bow to/for all army [the] heaven and to serve: minister [obj] them
4 Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
and to build altar in/on/with house: temple LORD which to say LORD in/on/with Jerusalem to set: put [obj] name my
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
and to build altar to/for all army [the] heaven in/on/with two court house: temple LORD
6 Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
and to pass [obj] son: child his in/on/with fire and to divine and to divine and to make: do medium and spiritist to multiply to/for to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD to/for to provoke
7 Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
and to set: make [obj] idol [the] Asherah which to make in/on/with house: home which to say LORD to(wards) David and to(wards) Solomon son: child his in/on/with house: home [the] this and in/on/with Jerusalem which to choose from all tribe Israel to set: put [obj] name my to/for forever: enduring
8 Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
and not to add: again to/for to wander foot Israel from [the] land: soil which to give: give to/for father their except if to keep: careful to/for to make: do like/as all which to command them and to/for all [the] instruction which to command [obj] them servant/slave my Moses
9 Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
and not to hear: hear and to go astray them Manasseh to/for to make: do [obj] [the] bad: evil from [the] nation which to destroy LORD from face: before son: descendant/people Israel
10 Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
and to speak: speak LORD in/on/with hand: by servant/slave his [the] prophet to/for to say
11 “Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
because which to make Manasseh king Judah [the] abomination [the] these be evil from all which to make: do [the] Amorite which to/for face: before his and to sin also [obj] Judah in/on/with idol his
12 Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
to/for so thus to say LORD God Israel look! I to come (in): bring distress: harm upon Jerusalem and Judah which all (to hear: hear her *Q(K)*) to tingle two ear his
13 Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
and to stretch upon Jerusalem [obj] line Samaria and [obj] level house: household Ahab and to wipe [obj] Jerusalem like/as as which to wipe [obj] [the] dish to wipe and to overturn upon face her
14 Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
and to leave [obj] remnant inheritance my and to give: give them in/on/with hand: power enemy their and to be to/for plunder and to/for plunder to/for all enemy their
15 chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
because which to make: do [obj] [the] bad: evil in/on/with eye: seeing my and to be to provoke [obj] me from [the] day: today which to come out: come father their from Egypt and till [the] day: today [the] this
16 Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
and also blood innocent to pour: kill Manasseh to multiply much till which to fill [obj] Jerusalem lip: edge to/for lip: edge to/for alone from sin his which to sin [obj] Judah to/for to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD
17 Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
and remainder word: deed Manasseh and all which to make: do and sin his which to sin not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Judah
18 Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
and to lie down: be dead Manasseh with father his and to bury in/on/with garden house: home his in/on/with Garden (of Uzza) (Garden of) Uzza and to reign Amon son: child his underneath: instead him
19 Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
son: aged twenty and two year Amon in/on/with to reign he and two year to reign in/on/with Jerusalem and name mother his Meshullemeth daughter Haruz from Jotbah
20 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD like/as as which to make: do Manasseh father his
21 Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
and to go: walk in/on/with all [the] way: conduct which to go: walk father his and to serve: minister [obj] [the] idol which to serve: minister father his and to bow to/for them
22 Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
and to leave: forsake [obj] LORD God father his and not to go: walk in/on/with way: conduct LORD
23 Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
and to conspire servant/slave Amon upon him and to die [obj] [the] king in/on/with house: home his
24 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
and to smite people [the] land: country/planet [obj] all [the] to conspire upon [the] king Amon and to reign people [the] land: country/planet [obj] Josiah son: child his underneath: instead him
25 Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
and remainder word: deed Amon which to make: do not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Judah
26 Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
(and to bury *LB(ah)*) [obj] him in/on/with tomb his in/on/with Garden (of Uzza) (Garden of) Uzza and to reign Josiah son: child his underneath: instead him

< 2 Mafumu 21 >