< 2 Mafumu 21 >

1 Manase anakhala mfumu ali ndi zaka khumi ndi ziwiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 55. Amayi ake anali Hefiziba.
Manasse var tolv År gammel, da han blev Konge, og han herskede fem og halvtredsindstyve År i Jerusalem. Hans Moder hed Hefziba.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, potsatira mchitidwe wonyansa wa mitundu imene Yehova anayipirikitsa pofika Aisraeli.
Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, og efterlignede de Folkeslags Vederstyggeligheder, som HERREN havde drevet bort foran Israeliterne.
3 Iyetu anamanganso malo opembedzera mafano amene Hezekiya abambo ake anawawononga. Anamangira Baala maguwa a nsembe ndi mtengo wa fano la Asera monga anachitira Ahabu mfumu ya Israeli ndipo ankapembedza zolengedwa zonse zamlengalenga.
Han byggede atter de Offerhøje, som hans Fader Ezekias havde ødelagt, rejste Altre for Ba'al, lavede en Asjerastøtte, ligesom Kong Akab af Israel havde gjort, og tilbad og dyrkede hele Himmelens Hær.
4 Anamanga maguwa ansembewa mʼNyumba ya Yehova, mʼmene Yehova ananena kuti, “Mu Yerusalemu ndidzayikamo Dzina langa.”
Og han byggede Altre i HERRENs Hus, om hvilket HERREN havde sagt: "I Jerusalem vil jeg stedfæste mit Navn."
5 Mʼmabwalo onse awiri a Nyumba ya Yehova, Manase anamangamo maguwa opembedzerapo zinthu zamlengalenga.
Og han byggede Altre for hele Himmelens Hær i begge HERRENs Hus's Forgårde.
6 Iye anapsereza mwana wake pa moto ngati nsembe, ankachita za matsenga, ankawombeza mawula, ankapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndiponso ankapembedza mizimu. Iyeyo anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova ndipo anakwiyitsa Yehovayo.
Han lod sin Søn gå igennem Ilden, drev Trolddom og tog Varsler og ansatte Dødemanere og Sandsigere; han gjorde meget, som var ondt i HERRENs Øjne, og krænkede ham.
7 Iye anatenga fano losema la Asera limene analipanga ndi kuliyika mʼNyumba ya Yehova, Nyumba imene Yehova ananena kwa Davide ndi mwana wake Solomoni kuti, “Mʼnyumba iyi ndi mu Yerusalemu ndiwo malo amene ndasankha pakati pa mafuko onse a Aisraeli kuyikamo Dzina langa kwamuyaya.
Den Asjerastøtte, han lod lave, opstillede han i det Hus, om bvilket HERREN havde sagt til David og hans Søn Salomo: "I dette Hus og i Jerusalem, som jeg har udvalgt af alle Israels Stammer, vil jeg stedfæste mit Navn til evig Tid;
8 Sindidzalola kuti Aisraeli achotsedwe mʼdziko lawo limene ndinapatsa makolo awo ngati iwowo adzasamala kuchita zinthu zonse zimene ndinawalamula ndi kusunga malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anawapatsa.”
og jeg vil ikke mere lade Israel vandre bort fra det Land, jeg gav deres Fædre, dog kun på det Vilkår, at de omhyggeligt overholder alt, hvad jeg har pålagt dem, hele den Lov, min Tjener Moses gav dem."
9 Koma anthu sanamvere. Manase anawasocheretsa, kotero kuti anachita zoyipa zambiri kupambana anthu a mitundu ina amene Yehova anawawononga pamene Aisraeli ankafika.
Men de vilde ikke høre, og Manasse forførte dem til at handle værre end de Folkeslag, HERREN havde udryddet foran Israeliterne.
10 Yehova anayankhula kudzera mwa atumiki ake, aneneri kuti,
Da talede HERREN ved sine Tjenere Profeterne således:
11 “Manase mfumu ya Yuda wachita machimo onyansawa ndipo wachita zoyipa kupambana Aamori amene analipo kale iye asanabadwe ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda ndi mafano ake.
"Efterdi Kong Manasse af Juda har øvet disse Vederstyggeligheder, ja øvet Ting, som er værre end alt, hvad Amoriterne, der var før ham. øvede, og tillige ved sine Afgudsbilleder har forledt Juda til Synd,
12 Choncho Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taonani, ndikubweretsa pa Yerusalemu ndi Yuda mavuto akuti aliyense amene adzawamve adzathedwa nzeru.
derfor, så siger HERREN, Israels Gud: Se, jeg bringer Ulykke over Jerusalem og Juda, så det skal ringe for Ørene på enhver, der hører derom!
13 Ndidzalanga Yerusalemu ndi Yuda pogwiritsa ntchito muyeso umene ndinalangira Samariya ndi Ahabu pamodzi ndi nyumba yake. Ndidzayeretsa Yerusalemu monga mmene munthu amachitira popukuta mbale ndipo atayipukuta amayivundikira pansi.
Jeg vil trække samme Målesnor over Jerusalem som over Samaria og bruge samme Lod som ved Akabs Hus; jeg vil afviske Jerusalem, som man afvisker et Fad og vender det om;
14 Ndidzawataya anthu otsala amene ndi cholowa changa ndipo ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo. Adzachotsedwa ndipo adaniwo adzawalanda zinthu zonse
jeg forstøder, hvad der er tilbage af min Ejendom, oggiver dem i deres Fjenders Hånd, og de skal blive til Rov og Bytte for alle deres Fjender,
15 chifukwa anachita zoyipa pamaso panga ndipo akhala akundikwiyitsa kuchokera tsiku limene makolo awo anatuluka mu Igupto mpaka lero lino.’”
fordi de gjorde, hvad der var ondt i mine Øjne, og krænkede mig, lige fra den Dag deres Fædre drog ud af Ægypten og indtil i Dag!"
16 Kuwonjezera apo, Manase anakhetsa kwambiri magazi a anthu osalakwa mpaka magaziwo kuyenderera mu Yerusalemu kuyambira mbali ina mpaka mbali ina, kuphatikiza pa kuchimwitsa Yuda, kotero kuti anthu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Desuden udgød Manasse uskyldigt Blod i store Måder, så han fyldte Jerusalem dermed til Randen, for ikke at tale om den Synd; han begik ved at forlede Juda til Synd, så de gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne.
17 Ntchito zina za Manase ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Hvad der ellers er at fortælle om Manasse, alt, hvad han udførte, og den Synd, han begik, står jo optegnet i Judas Kongers Krønike.
18 Manase anagona ndi makolo ake ndipo anayikidwa mʼmanda mʼmunda wa Uza, ku nyumba yaufumu. Ndipo Amoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Så lagde Manasse sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet i Haven ved sit Hus, i Uzzas Have; og hans Søn Amon blev Konge i hans Sted.
19 Amoni anakhala mfumu ali ndi zaka 22 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka ziwiri. Amayi ake anali Mesulemeti mwana wa Haruzi, wochokera ku Yotiba.
Amon var to og tyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede to År i Jerusalem. Hans Moder hed Mesjullemet og var en Datter af Haruz fra Jotba.
20 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira Manase abambo ake.
Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, ligesom hans Fader Manasse;
21 Anatsatira makhalidwe onse a abambo ake. Ankapembedza mafano amene abambo akewo ankawapembedza ndipo ankawagwadira.
han vandrede nøje i sin Faders Spor og dyrkede Afgudsbillederne, som hans Fader havde dyrket, og tilbad dem;
22 Iyeyo anasiya Yehova Mulungu wa makolo ake ndipo sanayende mʼnjira ya Yehova.
han forlod HERREN, sine Fædres Gud, og vandrede ikke på HERRENs Vej.
23 Nduna za Amoni zinamuchita chiwembu ndipo zinamupha mʼnyumba yake.
Amons Folk sammensvor sig imod ham og dræbte Kongen i hans
24 Koma anthu a mʼdzikomo anapha onse amene anachitira chiwembu Mfumu Amoni, nayika Yosiya mwana wake kukhala mfumu mʼmalo mwake.
men Folket fra Landet dræbte alle dem, der havde sammensvoret sig imod Kong Amon, og gjorde hans Søn Josias til Konge i hans Sted.
25 Ntchito zina za Amoni ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Hvad der ellers er at fortælle om Amon, og hvad han udførte, står jo optegnet i Judas Kongers Krønike.
26 Iye anayikidwa mʼmanda ake mʼmunda wa Uza. Ndipo Yosiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Man jordede ham i hans Faders Grav i Uzzas Have; og hans Søn Josias blev Konge i hans Sted.

< 2 Mafumu 21 >