< 2 Mafumu 20 >

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
У то време разболе се Језекија на смрт; и дође к њему пророк Исаија, син Амосов и рече му: Овако вели Господ: Нареди за кућу своју, јер ћеш умрети и нећеш остати жив.
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
А он се окрете лицем к зиду, и помоли се Господу говорећи:
3 “Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
Ох, Господе, опомени се да сам једнако ходио пред Тобом верно и с целим срцем, и творио шта је Теби угодно. И плака Језекија веома.
4 Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
И Исаија још не беше отишао до половине двора, а дође му реч Господња говорећи:
5 “Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
Врати се и реци Језекији, вођи народа мог: Овако вели Господ Бог Давида оца твог: Чуо сам молитву твоју, и видео сам сузе твоје; ево исцелићу те, до три дана ићи ћеш у дом Господњи.
6 Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
И додаћу ти веку петнаест година, и избавићу тебе и овај град из руку цара асирског, и бранићу овај град себе ради и ради Давида, слуге свог.
7 Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
Потом рече Исаија: Донесите груду сувих смокава. И донесавши привише му на оток, и исцели се.
8 Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
А Језекија рече Исаији: Шта ће бити знак да ће ме Господ исцелити и да ћу до три дана отићи у дом Господњи?
9 Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
А Исаија рече: Ово нека ти буде знак од Господа да ће учинити Господ шта је рекао: хоћеш ли да отиде сен десет кољенаца напред или да се врати десет кољенаца натраг?
10 Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
А Језекија рече: Лако је да сен отиде напред десет кољенаца; немој, него нека се врати сен десет кољенаца натраг?
11 Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
И Исаија пророк завапи ка Господу, и врати Господ сен по кољенцима по којима беше отишао на сунчанику Ахазовом натраг за десет кољенаца.
12 Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
У то време Меродах-Валадан, син Валаданов, цар вавилонски посла књигу с даром Језекији; јер беше чуо да је болестан Језекија.
13 Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
И Језекија саслушавши посланике показа им све ризнице своје, сребро и злато и мирисе, и најбоље уље, и кућу где му беше оружје, и шта се год налажаше у ризницама његовим, не оста ништа да им не показа Језекија у кући својој и у свему господству свом.
14 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Тада дође пророк Исаија к цару Језекији и рече му: Шта су говорили ти људи и одакле су дошли к теби? А Језекија рече: Из далеке земље дошли су, из Вавилона.
15 Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
А он рече: Шта су видели у твом двору? А Језекија рече: Видели су све што има у мом двору; није остало ништа у ризницама мојим да им нисам показао.
16 Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
Тада рече Исаија Језекији: Чуј реч Господњу.
17 Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
Ево доћи ће време кад ће се однети у Вавилон све што има у кући твојој, и што су сабирали оци твоји до данас, неће остати ништа, вели Господ.
18 Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
И синове твоје, који ће изаћи од тебе, које ћеш родити, узеће да буду дворани у двору цара вавилонског.
19 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
А Језекија рече Исаији: Добра је реч Господња, коју си рекао. Још рече: Је ли? За мог века биће мир и вера?
20 Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
А остала дела Језекијина и сва јунаштва његова, и како је начинио језеро, и воду довео у град, није ли записано у дневнику царева Јудиних?
21 Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
И почину Језекија код отаца својих, а на његово се место зацари Манасија, син његов.

< 2 Mafumu 20 >