< 2 Mafumu 20 >

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
Ын время ачея, Езекия а фост болнав пе моарте. Пророкул Исая, фиул луй Амоц, а венит ла ел ши й-а зис: „Аша ворбеште Домнул: ‘Рындуеште че ай де рындуит касей тале, кэч вей мури, ши ну вей май трэи.’”
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
Езекия с-а ынторс ку фаца ла перете ши а фэкут Домнулуй урмэтоаря ругэчуне:
3 “Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
„Доамне, аду-Ць аминте кэ ам умблат ынаинтя Фецей Тале ку крединчошие ши курэцие де инимэ ши ам фэкут че есте бине ынаинтя Та!” Ши Езекия а вэрсат мулте лакримь.
4 Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
Исая, каре ешисе, н-ажунсесе ынкэ ын куртя дин мижлок кынд кувынтул Домнулуй й-а ворбит астфел:
5 “Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
„Ынтоарче-те ши спуне луй Езекия, кэпетения попорулуй Меу: ‘Аша ворбеште Домнул Думнезеул татэлуй тэу Давид: «Ць-ам аузит ругэчуня ши ць-ам вэзут лакримиле. Ятэ кэ те вой фаче сэнэтос; а трея зи те вей суи ла Каса Домнулуй.
6 Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
Вой май адэуга чинчспрезече ань ла зилеле тале. Те вой избэви, пе тине ши четатя ачаста, дин мына ымпэратулуй Асирией ши вой окроти четатя ачаста дин причина Мя ши дин причина робулуй Меу Давид.»’”
7 Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
Исая а зис: „Луаць о туртэ де смокине.” Ау луат-о ши ау пус-о пе умфлэтурэ. Ши Езекия с-а виндекат.
8 Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
Езекия зисесе луй Исая: „Дупэ каре семн вой куноаште кэ мэ ва виндека Домнул ши кэ мэ вой суи а трея зи ла Каса Домнулуй?”
9 Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
Ши Исая а зис: „Ятэ дин партя Домнулуй семнул дупэ каре вей куноаште кэ Домнул ва ымплини кувынтул пе каре л-а ростит. Кум врей: сэ трякэ умбра песте зече трепте ынаинте сау сэ дя ынапой ку зече трепте?”
10 Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
Езекия а рэспунс: „Ну есте маре лукру ка умбра сэ трякэ ынаинте песте зече трепте, чи май бине сэ се дя ынапой ку зече трепте.”
11 Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
Атунч, Исая, пророкул, с-а ругат Домнулуй, ши Домнул а дат ку зече трепте ынапой умбра дин локул ын каре се коборысе пе кадранул соарелуй луй Ахаз.
12 Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
Ын ачелашь тимп, Беродак-Баладан, фиул луй Баладан, ымпэратул Бабилонулуй, а тримис о скрисоаре ши ун дар луй Езекия, кэч аузисе де боала луй Езекия.
13 Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
Езекия а аскултат пе соль ши ле-а арэтат локул унде ерау лукруриле луй де прец, арӂинтул ши аурул, мироденииле ши унтделемнул чел скумп, каса луй ку арме ши тот че се афла ын вистиерииле луй: н-а фост нимик пе каре сэ ну ли-л фи арэтат Езекия ын каса луй ши ын тоате мошииле луй.
14 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Пророкул Исая а венит ын урмэ ла ымпэратул Езекия ши й-а зис: „Че ау зис оамений ачея ши де унде ау венит ла тине?” Езекия а рэспунс: „Ау венит динтр-о царэ депэртатэ, дин Бабилон.”
15 Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
Исая а май зис: „Че ау вэзут ын каса та?” Езекия а рэспунс: „Ау вэзут тот че есте ын каса мя; н-а фост нимик ын вистиерииле меле пе каре сэ ну ли-л фи арэтат.”
16 Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
Атунч, Исая а зис луй Езекия: „Аскултэ кувынтул Домнулуй:
17 Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
‘Ятэ кэ вор вени времурь кынд вор дуче ын Бабилон тот че есте ын каса та ши че ау стрынс пэринций тэй пынэ ын зиуа де азь; ну ва рэмыне нимик, зиче Домнул.
18 Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
Ши вор луа дин фиий тэй, каре вор еши дин тине, пе каре-й вей наште, ши-й вор фаче фамень служиторь ын каса ымпэратулуй Бабилонулуй.’”
19 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
Езекия а рэспунс луй Исая: „Кувынтул Домнулуй пе каре л-ай ростит есте бун.” Ши а адэугат: „Кэч ва фи паче ши линиште ын тимпул веций меле!”
20 Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Челелалте фапте але луй Езекия, тоате испрэвиле луй ши кум а фэкут язул ши каналул де апэ ши а адус апеле ын четате ну сунт скрисе оаре ын Картя Кроничилор ымпэрацилор луй Иуда?
21 Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Езекия а адормит ку пэринций сэй. Ши ын локул луй а домнит фиул сэу Манасе.

< 2 Mafumu 20 >