< 2 Mafumu 20 >

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
W tych dniach Ezechiasz śmiertelnie zachorował. Przyszedł do niego prorok Izajasz, syn Amosa, i powiedział mu: Tak mówi PAN: Rozporządź swym domem, bo umrzesz i nie będziesz żył.
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
Wtedy [Ezechiasz] odwrócił swoją twarz do ściany i modlił się do PANA:
3 “Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
O PANIE, proszę cię, wspomnij teraz, że postępowałem wobec ciebie w prawdzie i z doskonałym sercem, czyniąc to, co dobre w twoich oczach. I płakał Ezechiasz rzewnie.
4 Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
Ale zanim Izajasz wyszedł do środkowego dziedzińca, doszło do niego słowo PANA:
5 “Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
Wróć i powiedz Ezechiaszowi, wodzowi mego ludu: Tak mówi PAN, Bóg Dawida, twego ojca: Wysłuchałem twojej modlitwy [i] widziałem twoje łzy. Oto uzdrawiam cię: trzeciego dnia wejdziesz do domu PANA.
6 Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
Dodam też do twoich dni piętnaście lat i wybawię ciebie i to miasto z ręki króla Asyrii. I będę bronić tego miasta ze względu na siebie i ze względu na Dawida, swego sługę.
7 Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
Następnie Izajasz powiedział: Przynieście garstkę suchych fig. Gdy wzięli [je] i położyli na wrzód, wyzdrowiał.
8 Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
Ezechiasz zapytał Izajasza: Jaki [będzie] znak [tego], że PAN mnie uzdrowi i że na trzeci dzień pójdę do domu PANA?
9 Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
Izajasz odpowiedział: To [będzie] znakiem od PANA, że uczyni PAN tę rzecz, którą obiecał: Czy cień ma się posunąć o dziesięć stopni, czy ma się cofnąć o dziesięć stopni?
10 Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
Ezechiasz odpowiedział: Łatwo cieniowi posunąć się o dziesięć stopni. Nie – niech cień cofnie się o dziesięć stopni.
11 Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
Wtedy prorok Izajasz zawołał do PANA. I on cofnął cień o dziesięć stopni, po których przesunął się na zegarze słonecznym Achaza.
12 Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
W tym czasie Berodach-Baladan, syn Baladana, król Babilonu, posłał listy i dar do Ezechiasza. Usłyszał bowiem, że Ezechiasz chorował.
13 Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
I Ezechiasz wysłuchał [posłańców], i pokazał im cały skarbiec swoich kosztowności, srebro, złoto, wonności, drogocenne olejki oraz swoją zbrojownię, a także wszystko, co się znajdowało w jego składach. Nie było nic, czego Ezechiasz by im nie pokazał w swoim domu i w całym swoim państwie.
14 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Wtedy prorok Izajasz przyszedł do króla Ezechiasza i zapytał go: Co powiedzieli ci mężczyźni i skąd przybyli do ciebie? Ezechiasz odpowiedział: Przybyli z dalekiej ziemi, z Babilonu.
15 Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
Znowu zapytał: Co widzieli w twoim domu? Ezechiasz odpowiedział: Widzieli wszystko, co jest w moim domu. Nie było nic, czego bym im nie pokazał w swoich skarbcach.
16 Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
Wtedy Izajasz powiedział do Ezechiasza: Słuchaj słowa PANA.
17 Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
Oto przyjdą dni, kiedy wszystko, co jest w twoim domu i co zgromadzili twoi ojcowie aż do tego dnia, zostanie zabrane do Babilonu. Nic nie pozostanie, mówi PAN.
18 Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
Z twoich synów, którzy będą pochodzić od ciebie i których spłodzisz, zabiorą [niektórych] i będą eunuchami w pałacu króla Babilonu.
19 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
Wtedy Ezechiasz powiedział do Izajasza: Dobre jest słowo PANA, które wypowiedziałeś. I dodał: Czyż [ono] nie jest [dobre], jeśli za moich dni będzie pokój i prawda?
20 Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
A pozostałe dzieje Ezechiasza, cała jego potęga i [to], jak zbudował sadzawkę i kanał, którymi sprowadził wodę do miasta, czy nie są zapisane w księdze kronik królów Judy?
21 Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
I Ezechiasz zasnął ze swoimi ojcami, a jego syn Manasses królował w jego miejsce.

< 2 Mafumu 20 >