< 2 Mafumu 20 >

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
Ngalezonsuku uHezekhiya wagula okokufa. UIsaya indodana kaAmozi umprofethi wasefika kuye wathi kuye: Itsho njalo iNkosi: Laya indlu yakho, ngoba uzakufa, kawuyikuphila.
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
Wasephendulela ubuso bakhe emdulini, wakhuleka eNkosini esithi:
3 “Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
Ngiyakuncenga Nkosi, ake ukhumbule ukuthi ngihambe phambi kwakho ngobuqotho langenhliziyo epheleleyo, ngenza okulungileyo emehlweni akho. UHezekhiya wasekhala inyembezi ngokukhala okukhulu.
4 Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
Kwasekusithi uIsaya engakaphumi egumeni elingaphakathi, ilizwi leNkosi lafika kuye lisithi:
5 “Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
Buyela uthi kuHezekhiya umbusi wabantu bami: Itsho njalo iNkosi, uNkulunkulu kaDavida uyihlo: Ngiwuzwile umkhuleko wakho, ngabona inyembezi zakho; khangela, ngizakusilisa; ngosuku lwesithathu uzakwenyukela endlini yeNkosi.
6 Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
Njalo ngizakwengezelela iminyaka elitshumi lanhlanu ensukwini zakho; ngikukhulule wena lalumuzi esandleni senkosi yeAsiriya; ngiwuvikele lumuzi ngenxa yami langenxa yenceku yami uDavida.
7 Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
UIsaya wasesithi: Thathani isigaqa somkhiwa. Basebesithatha, basifaka phezu kwethumba, yasisila.
8 Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
UHezekhiya wasesithi kuIsaya: Yisiphi isibonakaliso sokuthi iNkosi izangisilisa, lokuthi ngizakwenyukela endlini yeNkosi ngosuku lwesithathu?
9 Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
UIsaya wasesithi: Lesi yisibonakaliso kuwe esivela eNkosini esokuthi iNkosi izayenza into eyikhulumileyo: Isithunzi sizakuya phambili izinyathelo ezilitshumi, loba siye emuva izinyathelo ezilitshumi yini?
10 Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
UHezekhiya wasesithi: Kulula esithunzini ukuthi selule izinyathelo ezilitshumi; hatshi, kodwa isithunzi kasibuyele emuva izinyathelo ezilitshumi.
11 Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
UIsaya umprofethi wasekhala eNkosini, yasibuyisela emuva isithunzi, ngezinyathelo esasehle ngazo esikhwelweni sikaAhazi, izinyathelo ezilitshumi emuva.
12 Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
Ngalesosikhathi uMerodaki-Baladani indodana kaBaladani, inkosi yeBhabhiloni, wathumela izincwadi lesipho kuHezekhiya, ngoba wayezwile ukuthi uHezekhiya ubekade egula.
13 Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
UHezekhiya wabalalela, wabatshengisa yonke indlu yakhe yezinto eziligugu, isiliva legolide lamakha lamafutha amahle lendlu yezikhali zakhe, lakho konke okwakutholakala endlini yakhe yokuligugu; kakulalutho endlini yakhe lembusweni wonke wakhe uHezekhiya angabatshengisanga lona.
14 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
UIsaya umprofethi wasesiza enkosini uHezekhiya wathi kiyo: Batheni lababantu? Futhi bebevela ngaphi besiza kuwe? UHezekhiya wasesithi: Bebevela elizweni elikhatshana, eBhabhiloni.
15 Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
Wasesithi: Baboneni endlini yakho? UHezekhiya wasesithi: Babone konke okusendlini yami; kakulalutho phakathi kokuligugu kwami engingabatshengisanga khona.
16 Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
UIsaya wasesithi kuHezekhiya: Zwana ilizwi leNkosi.
17 Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
Khangela, insuku ziyeza lapho konke okusendlini yakho lalokho oyihlo abakubekelelayo kuze kube lamuhla kuzathwalelwa eBhabhiloni; kakuyikusala lutho, itsho iNkosi.
18 Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
Njalo bazathatha emadodaneni akho azaphuma kuwe, ozawazala, abe ngabathenwa esigodlweni senkosi yeBhabhiloni.
19 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
UHezekhiya wasesithi kuIsaya: Lihle ilizwi leNkosi olikhulumileyo. Wasesithi: Kakunjalo yini, uba kuzakuba khona ukuthula lokuvikeleka ensukwini zami?
20 Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Ezinye-ke zezindaba zikaHezekhiya, lawo wonke amandla akhe, lokuthi wenza ichibi, lomgelo, wangenisa amanzi phakathi komuzi, kakubhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoJuda?
21 Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
UHezekhiya waselala laboyise. UManase indodana yakhe wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe.

< 2 Mafumu 20 >