< 2 Mafumu 20 >

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
En ce temps-là, Ezéchias fut atteint d’une maladie mortelle. Le prophète Isaïe, fils d’Amoç, lui rendit visite et lui dit: "Ainsi parle l’Eternel: Donne tes ordres à ta maison, car tu vas mourir; tu ne te rétabliras pas."
2 Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
Ezéchias tourna la face vers le mur et implora l’Eternel en ces termes:
3 “Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
"De grâce, Seigneur, daigne te souvenir que j’ai marché devant toi fidèlement et d’un cœur sincère, et que j’ai fait ce qui te plaît!" Puis il éclata en longs sanglots.
4 Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
Isaïe n’avait pas encore quitté la cour du milieu quand l’Eternel s’adressa de nouveau à lui:
5 “Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
"Retourne pour dire à Ezéchias, le souverain de mon peuple: Ainsi parle l’Eternel, le Dieu de David, ton père: J’Ai entendu ta prière et vu tes larmes, je te guérirai, et dès le troisième jour tu monteras dans la maison de Dieu.
6 Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
Je prolongerai ta vie de quinze ans, je te délivrerai ainsi que cette ville de la main du roi d’Assyrie, et j’étendrai ma protection sur cette ville, à cause de moi et à cause de mon serviteur David."
7 Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
Isaïe dit: "Qu’on prenne un gâteau de figues." On le prit, on l’appliqua sur l’ulcère, et Ezéchias se rétablit.
8 Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
Ezéchias dit à Isaïe: "A quel signe reconnaîtrai-je que l’Eternel me guérira et que je pourrai monter le troisième jour dans la maison de Dieu?"
9 Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
Isaïe répondit: "Voici le signe que l’Eternel te propose pour te prouver qu’il réalisera la promesse qu’il a faite: Faut-il que l’ombre avance de dix degrés ou recule de dix degrés?
10 Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
C’Est chose facile, répliqua Ezéchias, que l’ombre descende de dix degrés; qu’elle revienne plutôt en arrière de dix degrés!"
11 Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
Le prophète Isaïe invoqua alors l’Eternel, qui ramena l’ombre de dix degrés en arrière sur le cadran où elle était descendue, sur le cadran d’Achaz.
12 Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
Berodac-Baladan, fils de Baladan, roi de la Babylonie, ayant appris en ce temps-là qu’Ezéchias avait été malade, lui envoya des lettres et un présent.
13 Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
Ezéchias écouta avec complaisance les messagers et leur fit voir en entier la maison où il conservait ses objets de prix, argent, or, aromates et huiles précieuses, ainsi que son arsenal et toute ce que contenaient ses trésors; il n’y eut rien dans son palais et dans toutes ses possessions qu’il ne leur montrât.
14 Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
Le prophète Isaïe, rendant visite au roi Ezéchias, lui demanda: "Qu’ont dit ces hommes et d’où viennent-ils pour te voir? Ils viennent d’une région lointaine, de la Babylonie," répliqua Ezéchias.
15 Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
"Qu’ont-ils vu dans ta demeure?" demanda encore Isaïe. "Ils ont vu tout ce qui se trouve dans mon palais, repartit Ezéchias; mes trésors ne contiennent pas un objet que je ne leur aie montré."
16 Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
Isaïe dit alors à Ezéchias: "Ecoute ce que dit le Seigneur:
17 Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
Il viendra un temps où l’on emportera en Babylonie tout ce que renferme ton palais avec tes trésors amassés par tes aïeux; il n’en restera rien, dit l’Eternel.
18 Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
On emmènera aussi une partie de tes fils qui te devront le jour, de ceux que tu engendreras, pour les employer comme fonctionnaires au palais du roi d’Assyrie."
19 Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
Ezéchias dit alors à Isaïe: "Bienveillante est la sentence de l’Eternel que tu m’as transmise." Et il ajouta: "Au moins, la paix et l’ordre régneront tant que je vivrai!"
20 Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Pour les autres faits concernant Ezéchias, tous ses exploits, la piscine et l’aqueduc qu’il a fait établir pour amener l’eau dans la ville, tout cela, est consigné dans le livre des annales des rois de Juda.
21 Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Ezéchias, s’étant endormi avec ses pères, eut pour successeur son fils Manassé.

< 2 Mafumu 20 >