< 2 Mafumu 2 >
1 Yehova ali pafupi kutenga Eliya kupita kumwamba mu kamvuluvulu, Eliya ndi Elisa anali pa ulendo wopita ku Giligala.
Pripetilo se je, ko je Gospod hotel Elija z vrtinčastim vetrom vzeti gor v nebo, da je Elija z Elizejem odšel iz Gilgála.
2 Eliya anawuza Elisa kuti, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Beteli.” Koma Elisa anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Beteli.
Elija je rekel Elizeju: »Ostani tukaj, prosim te, kajti Gospod me je poslal v Betel.« Elizej pa mu je rekel: » Kakor Gospod živi in kakor živi tvoja duša, te ne bom zapustil.« Tako sta odšla dol do Betela.
3 Ana a aneneri a ku Beteli anabwera kwa Elisa namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma musakambe zimenezi.”
Sinovi prerokov, ki so bili pri Betelu, so prišli naprej k Elizeju in mu rekli: »Ali veš, da bo Gospod danes odvzel tvojega gospodarja iznad tvoje glave?« Ta je rekel: »Da, vem to; molčite.«
4 Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yeriko.” Koma Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Yeriko.
Elija mu je rekel: »Elizej, ostani tukaj, prosim te, kajti Gospod me je poslal v Jeriho.« Ta pa je rekel: » Kakor Gospod živi in kakor živi tvoja duša, te ne bom zapustil.« Tako sta prišla do Jerihe.
5 Ana a aneneri amene anali ku Yeriko anapita kwa Elisa, namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma inu musakambe zimenezi.”
Sinovi prerokov, ki so bili pri Jerihi, so prišli k Elizeju in mu rekli: »Ali veš, da bo Gospod danes odvzel tvojega gospodarja iznad tvoje glave?« Ta pa je odgovoril: »Da, vem to; molčite.«
6 Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yorodani.” Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapitirira ulendo wawo.
Elija mu je rekel: »Ostani, prosim te, tukaj, kajti Gospod me je poslal k Jordanu.« Ta pa je rekel: » Kakor Gospod živi in kakor živi tvoja duša, te ne bom zapustil.« In oba sta šla naprej.
7 Anthu makumi asanu mwa ana a aneneri anawatsatira nayima chapatali moyangʼanana nawo ndipo Eliya ndi Elisa anayima mʼmphepete mwa Yorodani.
Petdeset mož izmed sinov prerokov je šlo in stali so, da gledajo od daleč, onadva pa sta stala ob Jordanu.
8 Eliya anatenga chovala chake nachipinda, napanda madzi ndi chovalacho. Madziwo anagawikana, ena kwina ena kwina, ndipo awiriwo anawoloka powuma.
Elija je vzel svoje ogrinjalo, ga zvil skupaj, udaril vode in razdelile so se sèm ter tja, tako da sta oba šla preko po suhih tleh.
9 Atawoloka, Eliya anati kwa Elisa, “Ndifotokozere, ndikuchitire chiyani ndisanachotsedwe pamaso pako?” Elisa anayankha kuti, “Ndikupemphani kuti mundipatse magawo awiri a mphamvu za mzimu wanu wa uneneri.”
Pripetilo se je, ko sta šla čez, da je Elija rekel Elizeju: »Prosi, kaj naj storim zate, preden bom vzet od tebe.« Elizej je rekel: »Prosim te, naj bo nad menoj dvojen delež tvojega duha.«
10 Eliya anati, “Wapempha chinthu chapatali, komabe ukandiona pamene ndikuchotsedwa pamaso pako, mphamvu wapemphayi idzakhala yako, koma ukapanda kundiona sizidzachitika.”
Rekel je: »Prosil si težko stvar. Vendar če me boš videl, ko bom vzet od tebe, se ti bo zgodilo, toda če ne, ne bo tako.«
11 Akuyenda ndi kumakambirana, mwadzidzidzi galeta lamoto ndi akavalo amoto anaonekera ndi kuwasiyanitsa awiriwo, ndipo Eliya anapita kumwamba mʼkamvuluvulu.
Pripetilo se je, ko sta še vedno šla naprej in se pogovarjala, da se je, glej, tam prikazal ognjen bojni voz in ognjeni konji in ju ločili narazen in Elija se je z vrtinčastim vetrom dvignil v nebo.
12 Elisa anaona zimenezi ndipo anafuwula kuti, “Abambo anga! Abambo anga! Magaleta a Israeli ndi anthu ake okwera pa akavalo!” Ndipo Elisa sanamuonenso Eliyayo. Pamenepo Elisa anagwira zovala zake nazingʼamba pakati.
Elizej je to videl in klical: »Moj oče, moj oče, Izraelov bojni voz in njegovi konjeniki.« In nič več ga ni videl. Zgrabil je svoja lastna oblačila in jih pretrgal na dva kosa.
13 Iye anatola chovala cha Eliya chomwe chinagwa nabwerera ndi kukayima mʼmphepete mwa Yorodani.
Pobral je tudi Elijevo ogrinjalo, ki je padlo iz njega, odšel nazaj in obstal pri bregu Jordana.
14 Ndipo Elisa anatenga chovala chomwe chinagwa kuchokera kwa Eliya napanda nacho madzi. Iye anafunsa kuti, “Ali kuti Mulungu wa Eliya?” Atapanda madzi, madziwo anagawika pakati, ena kwina ena kwina, ndipo iye anawoloka.
Vzel je Elijevo ogrinjalo, ki je padlo iz njega, udaril vode in rekel: »Kje je Gospod, Elijev Bog?« Ko je tudi on udaril vode, so se razdelile sèm ter tja in Elizej je šel preko.
15 Ndipo ana a aneneri ochokera ku Yeriko atamuona anati, “Mzimu wa Eliya wakhazikika pa Elisa.” Ndipo anapita kukakumana naye nagwada ndi kuweramitsa mitu yawo pansi pamaso pake.
Ko so ga sinovi prerokov, ki so opazovali pri Jerihi, zagledali, so rekli: »Elijev duh počiva na Elizeju.« Prišli so, da ga srečajo in se do tal priklonili pred njim.
16 Ndipo anawuza Elisa kuti, “Ife atumiki anu tili ndi anthu amphamvu makumi asanu. Aloleni apite kuti akafunefune mbuye wanu. Mwina Mzimu wa Yehova wamutenga ndi kukamuponya ku phiri lina kapena ku chigwa china.” Elisa anayankha kuti, “Ayi, musawatume.”
Rekli so mu: »Glej torej, s tvojimi služabniki bo petdeset močnih mož. Naj odidejo, prosimo te in poiščejo tvojega gospodarja, da ga ni morda gor vzel Gospodov Duh in ga vrgel na kako goro ali v kako dolino.« Rekel je: »Ne pošiljajte.«
17 Koma anamukakamizabe mpaka Elisayo anachita manyazi moti sakanatha kukana. Choncho iye anati, “Atumizeni.” Ndipo anatumiza anthu makumi asanu amene anakafunafuna Eliya kwa masiku atatu koma sanamupeze.
Ko so mu prigovarjali, dokler ni bil osramočen, je rekel: »Pošljite.« Zato so poslali petdeset mož in iskali tri dni, toda niso ga našli.
18 Atabwerera kwa Elisa (chifukwa anali akanali ku Yeriko), iye anawawuza kuti, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musapite?”
Ko so ponovno prišli k njemu (kajti mudil se je pri Jerihi), jim je rekel: »Ali vam nisem rekel: ›Ne pojdite?‹«
19 Anthu a mu mzindamo anati kwa Elisa, “Mbuye wathu, taonani mzinda uno uli pamalo pabwino, monga mukuoneramu, koma madzi ake ndi oyipa, nthaka yakenso ndi yosabereka.”
Ljudje iz mesta so Elizeju rekli: »Glej, prosim te, lega tega mesta je prijetna, kakor vidi moj gospod, toda voda je slaba in tla jalova.«
20 Iye anati, “Patseni mbale yatsopano ndipo muyikemo mchere.” Ndipo anabweretsa mbaleyo kwa iye.
Rekel je: »Prinesite mi nov vrč in vanj dajte sol.« In prinesli so ga k njemu.
21 Kenaka Elisa anapita ku kasupe wa madziwo, nathiramo mchere mʼkasupemo nati, “Yehova akuti, ‘Ndachiritsa madzi awa. Madzi amenewa sadzabweretsanso imfa kapena kuchititsa kuti nthaka ikhale yosabereka.’”
Šel je naprej, k izviru vodá in vanj vrgel sol ter rekel: »Tako govori Gospod: ›Ozdravil sem te vode, od tod ne bo nič več smrti ali jalove dežele.‹«
22 Kotero madziwo ndi abwino mpaka lero, molingana ndi mawu amene Elisa anayankhula.
Tako so bile vode ozdravljene do tega dne, glede na Elizejevo besedo, ki jo je govoril.
23 Kuchokera kumeneko Elisa anapita ku Beteli. Ndipo pamene ankayenda mu msewu, anyamata ena achichepere anatuluka mu mzindamo nʼkumamuseka. Iwo ankanena kuti, “Choka iwe, wachidazi! Choka iwe wachidazi”
Od tam je odšel gor k Betelu in ko je šel gor po poti, so prišli iz mesta majhni otroci, ga zasmehovali in mu rekli: »Pojdi gor, plešec; pojdi gor, plešec.«
24 Iye anatembenuka nawayangʼana ndipo anawatemberera mʼdzina la Yehova. Nthawi yomweyo panatulukira zimbalangondo ziwiri kuchokera kuthengo, ndi kuphapo anyamata 42.
Ta se je obrnil nazaj, pogledal nanje in jih preklel v Gospodovem imenu. In iz gozda sta prišli dve medvedki ter izmed njih raztrgali dvainštirideset otrok.
25 Ndipo iye anapita ku phiri la Karimeli. Pochoka kumeneko anabwerera ku Samariya.
Od tam je odšel na goro Karmel in od tam se je vrnil v Samarijo.