< 2 Mafumu 2 >

1 Yehova ali pafupi kutenga Eliya kupita kumwamba mu kamvuluvulu, Eliya ndi Elisa anali pa ulendo wopita ku Giligala.
Or il arriva lorsque l'Eternel voulut enlever Elie aux cieux par un tourbillon, qu'Elie et Elisée partirent de Guilgal.
2 Eliya anawuza Elisa kuti, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Beteli.” Koma Elisa anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Beteli.
Et Elie dit à Elisée: Je te prie demeure ici, car l'Eternel m'envoie jusqu'à Bethel. Mais Elisée répondit: L'Eternel est vivant, et ton âme est vivante, que je ne te laisserai point; ainsi ils descendirent à Bethel.
3 Ana a aneneri a ku Beteli anabwera kwa Elisa namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma musakambe zimenezi.”
Et les fils des Prophètes qui étaient à Bethel, sortirent vers Elisée, et lui dirent: Ne sais-tu pas bien qu'aujourd'hui l'Eternel va enlever ton maître d'avec toi? Et il répondit: Je le sais bien aussi; taisez-vous.
4 Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yeriko.” Koma Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Yeriko.
Et Elie lui dit: Elisée, je te prie, demeure ici, car l'Eternel m'envoie à Jérico. Mais il lui répondit: L'Eternel est vivant, et ton âme est vivante, que je ne te laisserai point! Ainsi ils s'en allèrent à Jérico.
5 Ana a aneneri amene anali ku Yeriko anapita kwa Elisa, namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma inu musakambe zimenezi.”
Et les fils des Prophètes qui étaient à Jérico vinrent vers Elisée, et lui dirent: Ne sais-tu pas bien que l'Eternel va enlever aujourd'hui ton maître d'avec toi? Et il répondit: Je le sais bien aussi; taisez-vous.
6 Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yorodani.” Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapitirira ulendo wawo.
Et Elie lui dit: Elisée, je te prie demeure ici, car l'Eternel m'envoie jusqu'au Jourdain. Mais il répondit: L'Eternel est vivant, et ton âme est vivante, que je ne te laisserai point; ainsi ils s'en allèrent eux deux ensemble.
7 Anthu makumi asanu mwa ana a aneneri anawatsatira nayima chapatali moyangʼanana nawo ndipo Eliya ndi Elisa anayima mʼmphepete mwa Yorodani.
Et cinquante hommes d'entre les fils des Prophètes vinrent, et se tinrent loin vis-à-vis; et eux deux s'arrêtèrent près du Jourdain.
8 Eliya anatenga chovala chake nachipinda, napanda madzi ndi chovalacho. Madziwo anagawikana, ena kwina ena kwina, ndipo awiriwo anawoloka powuma.
Alors Elie prit son manteau, et le replia, et il en frappa les eaux, qui se divisèrent en deux, et ils passèrent tous deux à sec.
9 Atawoloka, Eliya anati kwa Elisa, “Ndifotokozere, ndikuchitire chiyani ndisanachotsedwe pamaso pako?” Elisa anayankha kuti, “Ndikupemphani kuti mundipatse magawo awiri a mphamvu za mzimu wanu wa uneneri.”
Quand ils furent passés, Elie dit à Elisée: Demande ce que tu veux que je fasse pour toi, avant que je sois enlevé d'avec toi. Et Elisée répondit: Je te prie que j'aie de ton esprit autant que deux.
10 Eliya anati, “Wapempha chinthu chapatali, komabe ukandiona pamene ndikuchotsedwa pamaso pako, mphamvu wapemphayi idzakhala yako, koma ukapanda kundiona sizidzachitika.”
Et il lui dit: Tu as demandé une chose difficile; si tu me vois enlever d'avec toi, cela te sera accordé; mais si tu ne me vois point, cela ne te sera point accordé.
11 Akuyenda ndi kumakambirana, mwadzidzidzi galeta lamoto ndi akavalo amoto anaonekera ndi kuwasiyanitsa awiriwo, ndipo Eliya anapita kumwamba mʼkamvuluvulu.
Et il arriva que comme ils marchaient, en parlant, voilà, un chariot de feu et des chevaux de feu les séparèrent l'un de l'autre; et Elie monta aux cieux par un tourbillon.
12 Elisa anaona zimenezi ndipo anafuwula kuti, “Abambo anga! Abambo anga! Magaleta a Israeli ndi anthu ake okwera pa akavalo!” Ndipo Elisa sanamuonenso Eliyayo. Pamenepo Elisa anagwira zovala zake nazingʼamba pakati.
Et Elisée le regardant criait: Mon père! mon père! chariot d'Israël, et sa cavalerie! et il ne le vit plus; puis prenant ses vêtements, il les déchira en deux pièces.
13 Iye anatola chovala cha Eliya chomwe chinagwa nabwerera ndi kukayima mʼmphepete mwa Yorodani.
Et il leva le manteau d'Elie qui était tombé de dessus lui, et s'en retourna, et s'arrêta sur le bord du Jourdain.
14 Ndipo Elisa anatenga chovala chomwe chinagwa kuchokera kwa Eliya napanda nacho madzi. Iye anafunsa kuti, “Ali kuti Mulungu wa Eliya?” Atapanda madzi, madziwo anagawika pakati, ena kwina ena kwina, ndipo iye anawoloka.
Ensuite il prit le manteau d'Elie, qui était tombé de dessus lui, et frappa les eaux, et dit: Où est l'Eternel le Dieu d'Elie, l'Eternel lui-même? Il frappa donc les eaux, et elles se divisèrent en deux; et Elisée passa.
15 Ndipo ana a aneneri ochokera ku Yeriko atamuona anati, “Mzimu wa Eliya wakhazikika pa Elisa.” Ndipo anapita kukakumana naye nagwada ndi kuweramitsa mitu yawo pansi pamaso pake.
Et quand les fils des Prophètes qui étaient à Jérico vis-à-vis, l'eurent vu, ils dirent: L'Esprit d'Elie s'est posé sur Elisée, et ils vinrent au-devant de lui, et se prosternèrent devant lui en terre;
16 Ndipo anawuza Elisa kuti, “Ife atumiki anu tili ndi anthu amphamvu makumi asanu. Aloleni apite kuti akafunefune mbuye wanu. Mwina Mzimu wa Yehova wamutenga ndi kukamuponya ku phiri lina kapena ku chigwa china.” Elisa anayankha kuti, “Ayi, musawatume.”
Et lui dirent: Voici maintenant avec tes serviteurs cinquante hommes puissants, nous te prions qu'ils s'en aillent chercher ton maître, de peur que l'Esprit de l'Eternel ne l'ait enlevé, et ne l'ait jeté sur quelque montagne, ou dans quelque vallée; et il répondit: N'y envoyez point.
17 Koma anamukakamizabe mpaka Elisayo anachita manyazi moti sakanatha kukana. Choncho iye anati, “Atumizeni.” Ndipo anatumiza anthu makumi asanu amene anakafunafuna Eliya kwa masiku atatu koma sanamupeze.
Mais ils le pressèrent tant par leurs paroles, qu'il en était honteux. Il [leur] dit donc: Envoyez-y. Et ils envoyèrent [ces] cinquante hommes, qui pendant trois jours cherchèrent [Elie], mais ils ne le trouvèrent point.
18 Atabwerera kwa Elisa (chifukwa anali akanali ku Yeriko), iye anawawuza kuti, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musapite?”
Puis ils retournèrent vers lui à Jérico, où il s'était arrêté, et il leur dit: Ne vous avais-je pas dit de n'y aller point?
19 Anthu a mu mzindamo anati kwa Elisa, “Mbuye wathu, taonani mzinda uno uli pamalo pabwino, monga mukuoneramu, koma madzi ake ndi oyipa, nthaka yakenso ndi yosabereka.”
Et les gens de la ville dirent à Elisée: Voici maintenant, la demeure de cette ville est bonne, comme mon Seigneur voit, mais les eaux en sont mauvaises, et la terre en est stérile.
20 Iye anati, “Patseni mbale yatsopano ndipo muyikemo mchere.” Ndipo anabweretsa mbaleyo kwa iye.
Et il dit: Apportez-moi un vase neuf, et mettez-y du sel; et ils le lui apportèrent.
21 Kenaka Elisa anapita ku kasupe wa madziwo, nathiramo mchere mʼkasupemo nati, “Yehova akuti, ‘Ndachiritsa madzi awa. Madzi amenewa sadzabweretsanso imfa kapena kuchititsa kuti nthaka ikhale yosabereka.’”
Puis il alla vers le lieu d'où sortaient les eaux, et il y jeta le sel, en disant: Ainsi a dit l'Eternel: J'ai rendu ces eaux saines, elles ne causeront plus la mort, et [la terre ne sera plus] stérile.
22 Kotero madziwo ndi abwino mpaka lero, molingana ndi mawu amene Elisa anayankhula.
Elles furent donc rendues saines, [et elles l'ont été] jusqu'à ce jour, selon la parole qu'Elisée avait proférée.
23 Kuchokera kumeneko Elisa anapita ku Beteli. Ndipo pamene ankayenda mu msewu, anyamata ena achichepere anatuluka mu mzindamo nʼkumamuseka. Iwo ankanena kuti, “Choka iwe, wachidazi! Choka iwe wachidazi”
Il monta de là à Bethel; et comme il montait par le chemin, des petits garçons sortirent de la ville, et en se moquant de lui, ils lui disaient: Monte chauve, monte chauve.
24 Iye anatembenuka nawayangʼana ndipo anawatemberera mʼdzina la Yehova. Nthawi yomweyo panatulukira zimbalangondo ziwiri kuchokera kuthengo, ndi kuphapo anyamata 42.
Et [Elisée]regarda derrière lui, et les ayant regardés, il les maudit au Nom de l'Eternel; sur quoi deux ourses sortirent de la forêt, et déchirèrent quarante-deux de ces enfants-là.
25 Ndipo iye anapita ku phiri la Karimeli. Pochoka kumeneko anabwerera ku Samariya.
Et il s'en alla de là en la montagne de Carmel, d'où il s'en retourna à Samarie.

< 2 Mafumu 2 >