< 2 Mafumu 2 >
1 Yehova ali pafupi kutenga Eliya kupita kumwamba mu kamvuluvulu, Eliya ndi Elisa anali pa ulendo wopita ku Giligala.
and to be in/on/with to ascend: establish LORD [obj] Elijah in/on/with tempest [the] heaven and to go: went Elijah and Elisha from [the] Gilgal
2 Eliya anawuza Elisa kuti, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Beteli.” Koma Elisa anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Beteli.
and to say Elijah to(wards) Elisha to dwell please here for LORD to send: depart me till Bethel Bethel and to say Elisha alive LORD and alive soul: myself your if: surely no to leave: forsake you and to go down Bethel Bethel
3 Ana a aneneri a ku Beteli anabwera kwa Elisa namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma musakambe zimenezi.”
and to come out: come son: child [the] prophet which Bethel Bethel to(wards) Elisha and to say to(wards) him to know for [the] day LORD to take: take [obj] lord your from upon head: leader your and to say also I to know be silent
4 Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yeriko.” Koma Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapita ku Yeriko.
and to say to/for him Elijah Elisha to dwell please here for LORD to send: depart me Jericho and to say alive LORD and alive soul: myself your if: surely no to leave: forsake you and to come (in): come Jericho
5 Ana a aneneri amene anali ku Yeriko anapita kwa Elisa, namufunsa kuti, “Kodi ukudziwa kuti lero Yehova akuchotsera mbuye wako?” Elisa anayankha kuti, “Inde ndikudziwa, koma inu musakambe zimenezi.”
and to approach: approach son: child [the] prophet which in/on/with Jericho to(wards) Elisha and to say to(wards) him to know for [the] day LORD to take: take [obj] lord your from upon head: leader your and to say also I to know be silent
6 Ndipo Eliya anati kwa Elisa, “Iwe khala pano pakuti Yehova wandituma kuti ndipite ku Yorodani.” Elisa anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Motero awiriwo anapitirira ulendo wawo.
and to say to/for him Elijah to dwell please here for LORD to send: depart me [the] Jordan [to] and to say alive LORD and alive soul: myself your if: surely no to leave: forsake you and to go: went two their
7 Anthu makumi asanu mwa ana a aneneri anawatsatira nayima chapatali moyangʼanana nawo ndipo Eliya ndi Elisa anayima mʼmphepete mwa Yorodani.
and fifty man from son: child [the] prophet to go: went and to stand: stand from before from distant and two their to stand: stand upon [the] Jordan
8 Eliya anatenga chovala chake nachipinda, napanda madzi ndi chovalacho. Madziwo anagawikana, ena kwina ena kwina, ndipo awiriwo anawoloka powuma.
and to take: take Elijah [obj] clothing his and to fold and to smite [obj] [the] water and to divide here/thus and here/thus and to pass two their in/on/with dry ground
9 Atawoloka, Eliya anati kwa Elisa, “Ndifotokozere, ndikuchitire chiyani ndisanachotsedwe pamaso pako?” Elisa anayankha kuti, “Ndikupemphani kuti mundipatse magawo awiri a mphamvu za mzimu wanu wa uneneri.”
and to be like/as to pass they and Elijah to say to(wards) Elisha to ask what? to make: do to/for you in/on/with before to take: take from from with you and to say Elisha and to be please lip: according two in/on/with spirit your to(wards) me
10 Eliya anati, “Wapempha chinthu chapatali, komabe ukandiona pamene ndikuchotsedwa pamaso pako, mphamvu wapemphayi idzakhala yako, koma ukapanda kundiona sizidzachitika.”
and to say to harden to/for to ask if to see: see [obj] me to take: take from with you to be to/for you so and if nothing not to be
11 Akuyenda ndi kumakambirana, mwadzidzidzi galeta lamoto ndi akavalo amoto anaonekera ndi kuwasiyanitsa awiriwo, ndipo Eliya anapita kumwamba mʼkamvuluvulu.
and to be they(masc.) to go: went to go: went and to speak: speak and behold chariot fire and horse fire and to separate between two their and to ascend: rise Elijah (in/on/with tempest *LAB(h)*) [the] heaven
12 Elisa anaona zimenezi ndipo anafuwula kuti, “Abambo anga! Abambo anga! Magaleta a Israeli ndi anthu ake okwera pa akavalo!” Ndipo Elisa sanamuonenso Eliyayo. Pamenepo Elisa anagwira zovala zake nazingʼamba pakati.
and Elisha to see: see and he/she/it to cry father my father my chariot Israel and horseman his and not to see: see him still and to strengthen: hold in/on/with garment his and to tear them to/for two rags
13 Iye anatola chovala cha Eliya chomwe chinagwa nabwerera ndi kukayima mʼmphepete mwa Yorodani.
and to exalt [obj] clothing Elijah which to fall: fall from upon him and to return: return and to stand: stand upon lip: shore [the] Jordan
14 Ndipo Elisa anatenga chovala chomwe chinagwa kuchokera kwa Eliya napanda nacho madzi. Iye anafunsa kuti, “Ali kuti Mulungu wa Eliya?” Atapanda madzi, madziwo anagawika pakati, ena kwina ena kwina, ndipo iye anawoloka.
and to take: take [obj] clothing Elijah which to fall: fall from upon him and to smite [obj] [the] water and to say where? LORD God Elijah also he/she/it and to smite [obj] [the] water and to divide here/thus and here/thus and to pass Elisha
15 Ndipo ana a aneneri ochokera ku Yeriko atamuona anati, “Mzimu wa Eliya wakhazikika pa Elisa.” Ndipo anapita kukakumana naye nagwada ndi kuweramitsa mitu yawo pansi pamaso pake.
and to see: see him son: child [the] prophet which in/on/with Jericho from before and to say to rest spirit Elijah upon Elisha and to come (in): come to/for to encounter: meet him and to bow to/for him land: soil [to]
16 Ndipo anawuza Elisa kuti, “Ife atumiki anu tili ndi anthu amphamvu makumi asanu. Aloleni apite kuti akafunefune mbuye wanu. Mwina Mzimu wa Yehova wamutenga ndi kukamuponya ku phiri lina kapena ku chigwa china.” Elisa anayankha kuti, “Ayi, musawatume.”
and to say to(wards) him behold please there with servant/slave your fifty human son: warrior strength to go: went please and to seek [obj] lord your lest to lift: bear him spirit LORD and to throw him in/on/with one [the] mountain: mount or in/on/with one ([the] valley *Q(k)*) and to say not to send: depart
17 Koma anamukakamizabe mpaka Elisayo anachita manyazi moti sakanatha kukana. Choncho iye anati, “Atumizeni.” Ndipo anatumiza anthu makumi asanu amene anakafunafuna Eliya kwa masiku atatu koma sanamupeze.
and to press in/on/with him till be ashamed and to say to send: depart and to send: depart fifty man and to seek three day and not to find him
18 Atabwerera kwa Elisa (chifukwa anali akanali ku Yeriko), iye anawawuza kuti, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musapite?”
and to return: return to(wards) him and he/she/it to dwell in/on/with Jericho and to say to(wards) them not to say to(wards) you not to go: went
19 Anthu a mu mzindamo anati kwa Elisa, “Mbuye wathu, taonani mzinda uno uli pamalo pabwino, monga mukuoneramu, koma madzi ake ndi oyipa, nthaka yakenso ndi yosabereka.”
and to say human [the] city to(wards) Elisha behold please seat [the] city pleasant like/as as which lord my to see: see and [the] water bad: harmful and [the] land: country/planet barenness
20 Iye anati, “Patseni mbale yatsopano ndipo muyikemo mchere.” Ndipo anabweretsa mbaleyo kwa iye.
and to say to take: bring to/for me jar new and to set: put there salt and to take: bring to(wards) him
21 Kenaka Elisa anapita ku kasupe wa madziwo, nathiramo mchere mʼkasupemo nati, “Yehova akuti, ‘Ndachiritsa madzi awa. Madzi amenewa sadzabweretsanso imfa kapena kuchititsa kuti nthaka ikhale yosabereka.’”
and to come out: come to(wards) exit [the] water and to throw there salt and to say thus to say LORD to heal to/for water [the] these not to be from there still death and barenness
22 Kotero madziwo ndi abwino mpaka lero, molingana ndi mawu amene Elisa anayankhula.
and to heal [the] water till [the] day [the] this like/as word Elisha which to speak: speak
23 Kuchokera kumeneko Elisa anapita ku Beteli. Ndipo pamene ankayenda mu msewu, anyamata ena achichepere anatuluka mu mzindamo nʼkumamuseka. Iwo ankanena kuti, “Choka iwe, wachidazi! Choka iwe wachidazi”
and to ascend: rise from there Bethel Bethel and he/she/it to ascend: rise in/on/with way: journey and youth small to come out: come from [the] city and to mock in/on/with him and to say to/for him to ascend: rise bald to ascend: rise bald
24 Iye anatembenuka nawayangʼana ndipo anawatemberera mʼdzina la Yehova. Nthawi yomweyo panatulukira zimbalangondo ziwiri kuchokera kuthengo, ndi kuphapo anyamata 42.
and to turn after him and to see: see them and to lighten them in/on/with name LORD and to come out: come two bear from [the] wood and to break up/open from them forty and two youth
25 Ndipo iye anapita ku phiri la Karimeli. Pochoka kumeneko anabwerera ku Samariya.
and to go: went from there to(wards) mountain: mount [the] (Mount) Carmel and from there to return: return Samaria