< 2 Mafumu 19 >
1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
A LOHE ae la o Hezekia ke alii, haehae iho la ia i kona aahu, a hoouhi ia ia iho i ke kapa inoino, a komo aku la ia i ka hale o Iehova.
2 Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
Hoouna aku la ia ia Eliakima ka luna o ko ka hale, a me Sebena, ke kakauolelo, a me ka poe kahiko o na kahuna i hoouhiia i na kapa inoino, io Isaia la ke kaula, ke keiki a Amoza.
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
I aku la lakou ia ia, Ke olelo mai nei o Hezekia peneia, O keia la, he la pilikia, poino a me ka hoowahawana: no ka mea, ua hiki mai ka manawa e hanau ai na keiki, aohe ikaika e hanau mai ai.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
Malia paha e hoolohe mai o Iehova kou Akua i na olelo a pau a Rabesake, ka mea a ke alii o Asuria kona haku i hoouna mai ai e hoino i ke Akua ola; a e ahewa aku i na olelo a Iehova kou Akua i lohe ai; nolaila e pule aku oe no ka poe i koe i loaa.
5 Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
A hiki aku na kauwa a Hezekia ke alii io Isaia la.
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
I mai la o Isaia ia lakou, Penei oukou e olelo aku ai i ko oukou haku, Ke olelo mai nei o Iehova peneia, Mai makau oe i na olelo au i lohe ai, i ka mea a na kauwa a ke alii o Asuria i hoohiki ino mai ai ia'u.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Aia hoi, e hoouna au i makani io na la, a e lohe no ia i ka lono, a hoi aku i kona aina; a e hoohaule iho au ia ia i ka pahikaua ma kona aina iho.
8 Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
A hoi aku o Rabesake, a loaa ia ia ke alii o Asuria e kana ana i ko Lebena, no ka mea, ua lohe ia, ua haalele oia i Lakisa.
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
A lohe ia no Tirehaka ke alii o Aitiopa, i ka i ana ae, Aia hoi, ua hele mai ia e kaua mai ia oe: a hoouna hou aku la ia i na elele io Hezekia la, i aku la,
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
Penei oukou e olelo aku ai ia Hezekia ke alii o ka Iuda, e i aku, E malama o hoopunipuniia oe e kou Akua au i hilinai ai, i ka i ana'e, Aole e haawiia o Ierusalema iloko o ka lima o ke alii o ko Asuria.
11 Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
Aia hoi, ua lohe no oe i ka mea a na'lii o Asuria i hana aku ai i na aina a pau, ma ka luku loa ana ia lakou: a e hoopakeleia anei oe?
12 Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
Ua hoopakele anei na akua o na lahuikanaka ia lakou, i na mea a ko'u mau makua i luku ai: i Gozana, i Harama, i Rezepa, a me na kanaka o Edena, ka poe ma Telasara?
13 Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
Auhea ke alii o Hamata, a me ke alii o Arepada, a me ke alii no na kulanakauhale o Separevaima, o Hena, a me Iva?
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
A lawe ae la o Hezekia i na palapala mai ka lima mai o na elele, a heluhelu iho la ia mau mea: a pii ae la o Hezekia i ka hale o Iehova, a hohola aku la ia mau mea imua o Iehova.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Pule aku la o Hezekia imua o Iehova, i aku la, E Iehova ke Akua o ka Iseraela, ka mea e noho ana maluna o na keruba, o oe no ke Akua, o oe wale no, o na aupuni a pau o ka honua; o oe ka i hana i ka lani a me ka honua.
16 Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
E Iehova, e haliu mai kou pepeiao, a e lohe: e Iehova, e wehe ae i kou maka, a ike; a lohe i na olelo a Senakeriba, ana i hoouna mai ai e hoino aku i ke Akua ola.
17 “Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
He oiaio no, e Iehova, ua luku aku na'lii o Asuria i na lahuikanaka a me ko lakou aina;
18 Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
A ua haawi aku i ko lakou mau akua i ke ahi; no ka mea, aole lakou he akua, aka, he hana a na lima kanaka, he laau, a he pohaku: nolaila, ua luku aku lakou ia lakou la.
19 Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
Ano hoi, E Iehova ko makou Akua, ke nonoi aku nei au ia oe, e hoopakele mai oe ia makou mailoko mai o kona lima, i ike ai na aupuni a pau o ka honua, o oe no o Iehova ke Akua, o oe wale no.
20 Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
A hoouna aku la o Isaia ke keiki a Amoza io Hezekia la, i aku la, Ke olelo mai nei o Iehova ke Akua o ka Iseraela peneia, Ua lohe au i ka mea au i pule mai ai ia'u no Senakeriba ke alii o Asuria.
21 Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
Eia ka olelo a Iehova i olelo mai ai nona; O ka wahine puupaa, ke kaikamahine a Ziona, ua hoowahawaha mai ia ia oe, a ua akaaka mai ia oe: o ke kaikamahine a Ierusalema, ua hooluli mai ia i kona poo mahope ou.
22 Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
Owai la kau i hoino ai, a i hoohiki ino ai? Maluna owai kau i hookiekie ai i ka leo, a hapai ai i kou maka iluna? maluna o ka Mea Hemolele o ka Iseraela.
23 Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
Ma kou poe elele ua hoino oe ia Iehova, a ua i mai, Me na halekaa o'u a nui, ua pii mai au i kahi kiekie o na mauna, i na aoao hoi o Lebanona, a e kua aku au i kona mau laau kedera loloa, a me kona mau laau paina maikai: a e komo aku au i ka halekipa o kona mokuna, i ka ululaau o kona kihapai ulu.
24 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
Ua eli iho an, a ua inu i ka wai malihini, a me ka poho o kuu wawae, ua hoomaloo au i na muliwai o Aigupita.
25 “‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
Aole anei oe i lohe i ka manawa mamua, na'u no ia i hana, a i na wa kahiko, na'u no ia i hookumu? ano, ua hooko no au, i lilo ai oe i mea e luku ai i na kulanakauhale i hoopaaia, a lilo i mau puu opala.
26 Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
Nolaila ua nawaliwali ko lakou poe kanaka, a ua weliweli a pihoihoi, ua like lakou me ka launahele o ke kula, a me ka laau uliuli, me ka weuweu maluna o ka hale, a me ka palaoa eleele mamua o ka opuu ana.
27 “‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
Aka, ua ike au i kou noho ana, a me kou hele ana iwaho, a me kou komo ana iloko, a me kou inaina ana ia'u.
28 Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
No kou inaina ana mai ia'u, a no ka pii ana mai o kou haaheo iloko o ko'u pepeiao, nolaila, e hookomo au i ko'u lou i kou ihu, a me ko'u kaulawaha i kou lehelehe, a e hoihoi aku au ia oe ma ke ala au i hele mai nei.
29 “Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
O keia ka hoailona ia oe, e ai oukou i keia makahiki i ka ai uluwale, a ia makahiki aku i ka mea uluwale; a i ke kolu o ka makahiki e lulu oukou, a e hoiliili, a e kanu i na malawaina, a e ai i kona hua.
30 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
A o ke koena i pakele o ka ohana o Iuda e kolo lea ke aa malalo, a e hua mai i ka hua maluna.
31 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
No ka mea, e puka aku auanei ke koena mai Ierusalema aku, a me ka poe i pakele mai ka mauna o Ziona aku: o ka ikaika o Iehova e hana mai i keia.
32 “Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
No ia mea, ke olelo mai nei o Iehova penei no ke alii o Asuria, Aole ia e komo maloko o keia kulanakauhale, aole hoi e pana aku i ka pua malaila, aole hoi o hele mai imua ona me ka palekaua, aole e hoahu i puu e ku pono ana ia ia.
33 Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
Ma ke ala ana i hele mai ai, malaila oia e hoi aku ai, aole ia e komo iloko o keia kulanakauhale, wahi a Iehova.
34 Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
No ka mea, e malama no wau i keia kulanakauhale, e hoola no ia ia no'u, a no Davida kau kauwa.
35 Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
A ia po iho, hele aku la ka anela o Iehova, a luku aku la, ma kahi hoomoana o ko Asuria, i hookahi haneri a me kanawalukumamalima tausani: a ala ae la lakou i kakahiaka nui, aia hoi, he poe kupapau make lakou a pau.
36 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
A haalele aku la o Senakeriba ke alii o Asuria, hele aku a hoi aku la, a noho iho la ma Nineve.
37 Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.
A i kona hoomana ana ma ka hale o Niseroka kona akua, o Aderameleka, a me Sarezera, kana mau keiki, pepehi aku la laua ia ia me ka pahikaua, a holo laua i ka aina o Ararata. A noho alii iho la o Esarehadona, kana keiki, ma kona hakahaka.