< 2 Mafumu 19 >
1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
Ce qu’ayant entendu le roi Ezéchias, il déchira ses vêtements, se couvrit d’un sac, et entra dans la maison du Seigneur.
2 Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
Et il envoya Eliacim, intendant de sa maison, Sobna, le scribe, et les anciens d’entre les prêtres, couverts de sacs, à Isaïe, le prophète, fils d’Amos,
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
Lesquels dirent: Voici ce que dit Ezéchias: C’est un jour de tribulation, de reproche et de blasphème, que ce jour: des enfants sont venus jusqu’à l’enfantement, et celle qui est en travail n’a pas de forces.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
Peut-être que le Seigneur ton Dieu entendra toutes les paroles de Rabsacès, qu’a envoyé le roi des Assyriens, son maître, pour insulter le Dieu vivant, et l’attaquer par les paroles que le Seigneur ton Dieu a entendues: fais donc une prière au Seigneur pour les restes qui ont été retrouvés.
5 Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
Les serviteurs du roi Ezéchias vinrent donc vers Isaïe.
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
Et Isaïe leur répondit: Vous direz à votre maître: Voici ce que dit le Seigneur: Ne crains point à cause des paroles que tu as entendues, par lesquelles m’ont blasphémé les serviteurs du roi des Assyriens.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Voilà que moi je lui enverrai un esprit, et il apprendra une nouvelle, et il retournera dans sa terre, et je l’abattrai par le glaive dans sa terre.
8 Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
Rabsacès s’en retourna donc, et il trouva le roi des Assyriens assiégeant Lobna; car il avait su qu’il s’était retiré de devant Lachis.
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
Et lorsque Sennachérib eut entendu, au sujet de Tharaca, roi d’Ethiopie, des gens disant: Voilà qu’il est sorti pour combattre contre vous, et qu’il allait marcher contre ce roi, il envoya des messagers à Ezéchias, en disant:
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
Vous direz ceci à Ezéchias, roi de Juda: Que votre Dieu, en qui vous avez confiance, ne vous séduise pas, et ne dites point: Jérusalem ne sera point livrée aux mains du roi des Assyriens.
11 Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
Car vous-même, vous avez appris ce que les rois des Assyriens ont fait à tous les pays, comment ils les ont ravagés: est-ce donc que seul vous pourrez échapper?
12 Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
Est-ce que les dieux des nations ont délivré tous ceux qu’ont ravagés mes pères, c’est-à-dire Gozan, Haran, Réseph, et les enfants d’Eden, qui étaient en Thélassar?
13 Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
Où est le roi d’Emath, le roi d’Arphad, le roi de la ville de Sépharvaïm, d’Ana et d’Ava?
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
C’est pourquoi, lorsqu’Ezéchias eut reçu la lettre de Sennachérib de la main des messagers, et qu’il l’eut lue, il monta dans le temple, et étendit la lettre devant le Seigneur,
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Et il pria en sa présence, disant: Seigneur Dieu d’Israël, qui êtes assis sur les chérubins, c’est vous qui êtes le seul Dieu de tous les rois de la terre; c’est vous qui avez fait le ciel et la terre.
16 Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
Inclinez votre oreille et écoutez; ouvrez vos yeux. Seigneur, et voyez: écoutez toutes les paroles de Sennachérib, qui a envoyé pour incriminer devant nous le Dieu vivant.
17 “Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
Il est vrai, Seigneur, les rois des Assyriens ont détruit les nations et toutes leurs terres,
18 Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
Et ils ont jeté leurs dieux dans le feu; car ce n’étaient point des dieux, mais des ouvrages de mains d’hommes, de bois et de pierre, et ils les ont détruits.
19 Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
Maintenant donc, Seigneur notre Dieu, sauvez-nous de la main de ce roi, afin qu’ils sachent, tous les royaumes de la terre, que c’est vous qui êtes le seul Seigneur Dieu.
20 Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
Or Isaïe, fils d’Amos, envoya vers Ezéchias, disant: Voici ce que dit le Seigneur Dieu d’Israël: La prière que tu m’as faite touchant Sennachérib, roi des Assyriens, je l’ai entendue.
21 Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
Voici la parole que le Seigneur a dite de lui: Elle t’a méprisé et elle t’a raillé, la vierge, fille de Sion, derrière toi elle a secoué la tête, la fille de Jérusalem.
22 Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
Qui as-tu insulté et qui as-tu blasphémé? contre qui as-tu élevé la voix, et porté en haut les yeux? contre le saint d’Israël.
23 Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
Par l’entremise de tes serviteurs tu as insulté le Seigneur, et tu as dit: Avec la multitude de mes quadriges je suis monté sur le haut des montagnes, au sommet du Liban: j’ai coupé par le pied ses hauts cèdres et ses sapins les plus beaux. Je suis même entré jusqu’à l’extrémité de ses limites, et la forêt de son Carmel,
24 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
C’est moi qui l’ai coupée par le pied. Et j’ai bu des eaux étrangères, et j’ai séché par les traces de mes pieds toutes les eaux fermées.
25 “‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
N’as-tu donc point ouï dire ce que dès le commencement j’ai fait? Dès les jours anciens je l’ai préparé, et c’est maintenant que je l’ai exécuté; et des villes de combattants fortifiées seront comme des collines ruinées.
26 Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
Et ceux qui y sont dedans, faibles de main, ont tremblé et ont été confondus: ils sont devenus comme le foin d’un champ, comme l’herbe verte des toits et qui sèche avant de venir à maturité.
27 “‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
Ta demeure, ton entrée, ta sortie, et ton chemin par où tu es venu, je les ai sus d’avance, et même ta fureur contre moi.
28 Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
Tu as été furieux contre moi, et ton orgueil est monté à mes oreilles: c’est pourquoi je mettrai un cercle à tes narines et un mors à tes lèvres, et je te ramènerai par la voie par laquelle tu es venu.
29 “Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
Mais pour toi, Ezéchias, voici un signe: Mange cette année ce que tu trouveras; en la seconde année, ce qui naîtra de soi-même; mais, en la troisième année, semez et recueillez, plantez des vignes et mangez-en le fruit.
30 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
Et tout ce qui sera de reste de la maison de Juda, jettera des racines en bas et fera des fruits en haut.
31 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
Car de Jérusalem sortiront des restes, et ce qui sera sauvé de la montagne de Sion: le zèle du Seigneur des armées fera cela.
32 “Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
C’est pourquoi voici ce que dit le Seigneur du roi des Assyriens: Il n’entrera point dans cette ville, il ne lancera point contre elle de flèche; pas un bouclier ne l’occupera, et pas un retranchement ne l’entourera.
33 Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
Il retournera par la voie par laquelle il est venu; et il n’entrera point dans cette ville, dit le Seigneur.
34 Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
Je protégerai cette ville, et je la sauverai à cause de moi et à cause de mon serviteur David.
35 Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
Il arriva donc en cette nuit-là qu’il vint un ange du Seigneur, et qu’il tua dans le camp des Assyriens cent quatre-vingt mille hommes. Et lorsqu’au point du jour il se fut levé, il vit tous les corps des morts et, se retirant, il s’en alla.
36 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
Ainsi s’en retourna Sennachérib, roi des Assyriens, et il demeura à Ninive.
37 Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et lorsqu’il adorait dans le temple Nesroch, son dieu, Adramélech et Sarasar, ses fils, le frappèrent du glaive, et s’enfuirent dans la terre des Arméniens, et Asarhaddon, son fils, régna eu sa place.