< 2 Mafumu 19 >

1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
It happened, when king Hezekiah heard it, that he tore his clothes, and covered himself with sackcloth, and went into the house of the LORD.
2 Iye anatuma Eliyakimu, woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
He sent Eliakim, who was over the household, and Shebna the scribe, and the elders of the priests, covered with sackcloth, to Isaiah the prophet the son of Amoz.
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.
They said to him, "Thus says Hezekiah, 'This day is a day of trouble, of rebuke, and of rejection; for the children have come to the point of birth, and there is no strength to deliver them.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a Rabusake amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.’”
It may be the LORD your God will hear all the words of Rabshakeh, whom the king of Assyria his master has sent to defy the living God, and will rebuke the words which the LORD your God has heard. Therefore lift up your prayer for the remnant that is left.'"
5 Akuluakulu a Mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
So the servants of king Hezekiah came to Isaiah.
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti, ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
Isaiah said to them, "Thus you shall tell your master, 'Thus says the LORD, "Do not be afraid of the words that you have heard, with which the servants of the king of Assyria have blasphemed me.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Look, I will put a spirit in him, and he will hear news, and will return to his own land. I will cause him to fall by the sword in his own land."'"
8 Rabusake atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
So Rabshakeh returned, and found the king of Assyria warring against Libnah; for he had heard that he had departed from Lachish.
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi, akubwera kudzachita naye nkhondo. Choncho iye anatumanso amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
When he heard it said of Tirhakah king of Ethiopia, "Look, he has come out to fight against you," he sent messengers again to Hezekiah, saying,
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
'Thus you shall speak to Hezekiah king of Judah, saying, "Do not let your God in whom you trust deceive you, saying, Jerusalem will not be given into the hand of the king of Assyria.
11 Ndithu iwe unamva chimene mafumu a Asiriya anachita ku mayiko ena onse, kuti anawawononga kotheratu. Ndipo kodi iwe nʼkupulumuka?
Look, you have heard what the kings of Assyria have done to all lands, by destroying them utterly. Will you be delivered?
12 Kodi milungu ya mitundu imene makolo anga anayigonjetsa, milungu ya anthu a ku Gozani, Harani, Rezefi ndi Aedeni amene anali ku Teli Asara, inawapulumutsa?
Have the gods of the nations delivered them, which my fathers have destroyed, Gozan, and Haran, and Rezeph, and the people of Eden that were in Telassar?
13 Kodi mafumu a Hamati, Aripadi ndi mafumu a mizinda ya Sefaravaimu, Hena ndi Iva, ali kuti?”
Where is the king of Hamath, and the king of Arpad, and the king of the city of Sepharvaim, of Hena, and Ivvah?"'"
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga aja nayiwerenga. Pomwepo anapita ku Nyumba ya Yehova nayika kalatayo pamaso pa Yehova.
Hezekiah received the letter from the hand of the messengers, and read it. Then Hezekiah went up to the house of the LORD, and spread it before the LORD.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wa Israeli, Inu amene mumakhala pa Akerubi, Inu nokha ndinu Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Hezekiah prayed before the LORD, and said, "The LORD, the God of Israel, who sit above the cherubim, you are the God, even you alone, of all the kingdoms of the earth. You have made heaven and earth.
16 Inu Yehova, tcherani khutu lanu ndipo mumve Yehova tsekulani maso anu ndipo muone, imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza kunyoza Inu Mulungu wamoyo.
Incline your ear, LORD, and hear. Open your eyes, LORD, and see. Hear the words of Sennacherib, with which he has sent to defy the living God.
17 “Inu Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu iyi ndi mayiko awo.
Truly, LORD, the kings of Assyria have laid waste the nations and their lands,
18 Iwo anaponya milungu yawo pa moto ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mitengo ndi miyala chabe, yopangidwa ndi anthu.
and have cast their gods into the fire; for they were no gods, but the work of men's hands, wood and stone. Therefore they have destroyed them.
19 Ndipo tsopano Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni ndithu mʼdzanja lake, kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndinu Mulungu.”
Now therefore, the LORD our God, save us, I beg you, out of his hand, that all the kingdoms of the earth may know that you, LORD, are God alone."
20 Ndipo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga kwa Hezekiya wakuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndamva pemphero lako lonena za Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.’”
Then Isaiah the son of Amoz sent to Hezekiah, saying, "Thus says the LORD, the God of Israel, 'Whereas you have prayed to me against Sennacherib king of Assyria, I have heard you.
21 Mawu amene Yehova wayankhula wotsutsana naye ndi awa: “Namwali wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka iwe. Mwana wamkazi wa Yerusalemu akupukusa mutu wake kumbuyo kwako.
This is the word that the LORD has spoken concerning him: "The virgin daughter of Zion has despised you and ridiculed you. The daughter of Jerusalem has shaken her head at you.
22 Kodi iweyo wanyoza ndi kuchitira chipongwe yani? Kodi ndani amene wamufuwulira mawu ako ndi kumuyangʼana monyada? Wachitiratu izi Woyera wa Israeli!
Whom have you defied and blasphemed? Against whom have you exalted your voice and lifted up your eyes on high? Against the Holy One of Israel.
23 Kudzera mwa amithenga ako wonyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta ochuluka ndinakwera mapiri ataliatali, pa msonga za mapiri a Lebanoni. Ndigwetsa mitengo yake ya mkungudza yayitali kwambiri, mitengo yake ya payini yabwino kwambiri. Ndalowanso mʼkati mwake mwenimweni, mwa nkhalango yake yowirira kwambiri.
By your messengers you have defied the LORD, and have said, 'With the multitude of my chariots, I have come up to the height of the mountains, to the innermost parts of Lebanon; and I will cut down its tall cedars, and its choice fir trees; and I will enter into his farthest lodging place, the forest of his fruitful field.
24 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndipo ndinamwa madzi a kumeneko. Ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’”
I have dug and drunk strange waters, and with the sole of my feet will I dry up all the rivers of Egypt.'
25 “‘Kodi sunamvepo? Zimenezi ndinazikhazikitsa kalekale. Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndachita kuti zichitikedi, iwe kwako kunali kungosandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
Haven't you heard how I have done it long ago, and formed it of ancient times? Now have I brought it to pass, that it should be yours to lay waste fortified cities into ruinous heaps.
26 Anthu a kumeneko ndi opanda mphamvu, athedwa nzeru ndipo ali ndi manyazi. Ali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu womera pa denga, umene umawuma usanakule nʼkomwe.’”
Therefore their inhabitants were of small power. They were dismayed and confounded. They were like the grass of the field, and like the green herb, like the grass on the rooftops when it is scorched by the east wind.
27 “‘Koma Ine ndimadziwa kukhala kwako, kutuluka kwako ndi kulowa kwako, ndi mkwiyo wako pa Ine.
But I know your sitting down, and your going out, and your coming in, and your raging against me.
28 Chifukwa chakuti wandikwiyira ndipo ndamva za mwano wako, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndi kuyika chitsulo changa mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokudzeretsa njira yomwe unadzera pobwera.’
Because of your raging against me, and because your arrogance has come up into my ears, therefore I will put my hook in your nose, and my bridle in your lips, and I will turn you back by the way by which you came."
29 “Koma iwe Hezekiya, chizindikiro chako chidzakhala ichi: “Chaka chino mudzadya tirigu wamphulumukwa, ndipo chaka chamawa mudzadya tirigu wongodzimerera. Koma chaka chachitatu mudzadzala ndi kukolola, mudzawoka mphesa ndipo mudzadya zipatso zake.
"'This shall be the sign to you: You shall eat this year that which grows of itself, and in the second year that which springs of the same; and in the third year sow, and reap, and plant vineyards, and eat its fruit.
30 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsale adzazika mizu ndi kubereka zipatso.
The remnant that has escaped of the house of Judah shall again take root downward, and bear fruit upward.
31 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni kudzachokera gulu la anthu opulumuka.” “Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
For out of Jerusalem a remnant will go out, and out of Mount Zion those who shall escape. The zeal of the LORD of hosts will do this.'
32 “Choncho chimene Yehova akunena za mfumu ya ku Asiriya ndi ichi: “‘Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi. Sadzayandikira mzindawu ndi zishango zake kapena kumanga nthumbira ya nkhondo.
"Therefore thus says the LORD concerning the king of Assyria, 'He shall not come to this city, nor shoot an arrow there, neither shall he come before it with shield, nor cast up a mound against it.
33 Adzabwerera potsata njira imene anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu, akutero Yehova.
By the way that he came, by the same shall he return, and he shall not come to this city,' says the LORD.
34 Ndidzateteza mzinda umenewu kuwupulumutsa, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
'For I will defend this city to save it, for my own sake, and for my servant David's sake.'"
35 Usiku umenewo mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya ku Asiriya ndi kupha ankhondo 185,000. Ndipo pamene anthu anadzuka mmawa, taonani, mitembo inali ngundangunda!
It happened that night, that the angel of the LORD went out, and struck one hundred eighty-five thousand in the camp of the Assyrians. When men arose early in the morning, look, these were all dead bodies.
36 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anapasula misasa ndi kuchoka. Anabwerera ku Ninive nakakhala kumeneko.
So Sennacherib king of Assyria departed, and went and returned, and lived at Nineveh.
37 Tsiku lina, pamene Senakeribu ankapembedza mʼnyumba ya Nisiroki mulungu wake, ana ake Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga ndipo anathawira ku dziko la Ararati. Tsono Esrahadoni, mwana wake, analowa ufumu mʼmalo mwake.
It happened, as he was worshipping in the house of Nisroch his god, that Adrammelech and Sharezer struck him with the sword; and they escaped into the land of Ararat. Esarhaddon his son reigned in his place.

< 2 Mafumu 19 >