< 2 Mafumu 18 >

1 Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
І сталося третього року Осі́ї, сина Елиного, Ізраїлевого царя, зацарював Єзекія, син Ахазів, цар Юдин.
2 Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
Він був віку двадцяти й п'яти літ, коли зацарював, і царював в Єрусалимі двадцять і дев'ять літ. А ім'я́ його матері — Аві, дочка́ Захарія.
3 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
І робив він угодне в Господніх оча́х, усе так, як робив був його батько Давид.
4 Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
Він понищив па́гірки, і поламав стовпи для богів, і стяв Астарту, і розбив мідяно́го змія, якого зробив був Мойсей, бо аж до цих днів Ізраїлеві сини все кадили йому й кликали його: Нехушта́н.
5 Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
Він наді́явся на Господа, Бога Ізраїля, і такого, як він, не було між усіма́ царями Юдиними, ані між тими, що були перед ним.
6 Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
І міцно тримався він Господа, не відступався від Нього, і додержував заповіді Його, що наказав був Господь Мойсеєві.
7 Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
І був Господь із ним, — у всьому, куди він ходив, він мав пово́дження. І збунтувався він на асирійського царя, і не служив йому.
8 Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
Він побив филисти́млян аж до Аззи́ та границі її від вартово́ї башти аж до тверди́нного міста.
9 Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
І сталося четвертого року царя Єзекії, — це сьомий рік Осі́ї, Елиного сина, Ізраїлевого царя, — пішов Салманаса́р, цар асирійський, на Самарію, та й обліг її.
10 Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
І здобув він її по трьох рока́х: шостого року Єзекії, — це дев'ятий рік Осі́ї, Ізраїлевого царя, — була здобута Самарія.
11 Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
І вигнав асирійський цар Ізраїля до Асирії, і попровадив їх у Халах, і в Хавор, над річку Ґазан, та до мідійських міст.
12 Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
Це за те, що не слухалися вони голосу Господа, Бога свого, і переступали заповіта Його; усього, що наказав був Мойсей, раб Господній, вони ані не слухали, ані не робили.
13 Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
А чотирнадцятого року царя Єзекії прийшов Санхері́в, цар асирійський, на всі укріплені Юдині міста́, та й захопи́в їх.
14 Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
І послав Єзекія, цар Юдин, до царя асирійського, до Лахішу, говорячи: „Згрішив я! Відійди від мене, а що накладе́ш на мене, понесу́.“І наклав асирійський цар на Єзекію, Юдиного царя, три сотні талантів срібла та тридцять талантів золота.
15 Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
І віддав Єзекія все срібло, зна́йдене в Господньому домі та в царе́вих скарбни́цях.
16 Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
Того ча́су Єзекія відрубав золото з дверей Господнього дому та зо стовпів, що покрив був Єзекія, Юдин цар, золотом, і дав його́ асирійському цареві.
17 Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
А асирійський цар послав із Лахішу до царя Єзекії головного кома́ндувача, і великого є́внуха та великого ча́шника з великим ві́йськом до Єрусалиму. І пішли вони, і прийшли та й стали над водотя́гом горі́шнього ставу, що на битій дорозі до поля Валю́шників.
18 Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
І кли́кнули вони до царя, і до них вийшов Еліяким, син Хілкійї, начальник палати, і писар Шевна, та Йоах, син Асафів, ка́нцлер.
19 Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
І сказав до них великий ча́шник: „Скажіть Єзекії: Отак сказав великий цар, цар асирійський: Що́ це за надія, на яку ти наді́єшся?
20 Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
Чи думаєш ти, що слово уст, то вже рада та сила до війни? На ко́го тепер наді́єшся, що збунтувався проти мене?
21 Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
Тепер оце ти надієшся собі опе́ртися на оту пола́ману очерети́ну, на Єгипет, що коли хто опирається на неї, то вона вхо́дить у долоню йому й продіря́влює її. Отакий фараон, цар єгипетський, для всіх, хто надіється на нього.
22 Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
А коли ви скажете мені: Ми наді́ємось на Господа, Бога нашого, то чи ж Він не Той, що Єзекія понищив па́гірки Його та же́ртівники Його, і сказав Юді та Єрусалимові: перед оцим тільки же́ртівником будете вклонятися в Єрусалимі?
23 “‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
А тепер піди в за́клад із моїм паном, ассирійським царем, і я дам тобі дві тисячі ко́ней, якщо ти зможеш собі дати на них верхівці́в.
24 Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
І як же ти проженеш хоч одно́го намісника з найменших слуг мого пана? А ти собі наді́єшся на Єгипет ради колесни́ць та верхівців!
25 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
Тепер же, чи без Господа прийшов я на це місце, щоб знищити його? Господь сказав був мені: Піди на той край та знищ його!“
26 Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
І сказав Еліяким, син Хілкійї, і Шевна та Йоах до великого ча́шника: „Говори до своїх рабів по-араме́йському, бо ми розуміємо, і не говори з нами по-юде́йському в слух тих людей, що на мурі“.
27 Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
І сказав до них великий ча́шник: „Чи пан мій послав мене говорити ці слова́ до твого пана та до тебе? Хіба не до цих людей, що сидять на мурі, щоб із вами їсти вій кал та пити свою се́чу?“
28 Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
І став великий чашник, і кликнув гучним голосом по-юдейському, і говорив і сказав: „Послухайте слово великого царя, царя асирійського:
29 Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
Так сказав цар: Нехай не ду́рить вас Єзекія, бо він не зможе врятува́ти вас від руки його!
30 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
І нехай не запевня́є вас Єзекія Господом, говорячи: Рятуючи, врятує вас Господь, і не буде да́но цього міста в руку царя асирійського.
31 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
Не слухайте Єзекії, бо так сказав цар асирійський: Примиріться зо много, та й ви́йдіть до мене, та й їжте кожен свій виноград та кожен фіґу свою, і пийте кожен воду зо своєї ко́панки,
32 mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
аж поки я не прийду́ й не візьму́ вас до краю такого ж, як ваш Край, до кра́ю збіжжя та виноградного соку, до краю хліба та виноградників, до краю оливки, оливного соку та меду, — щоб ви жили й не вмирали! І не слухайте Єзекії, коли він намовляє вас, говорячи: Господь порятує нас!
33 Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
Чи справді врятували боги тих народів, кожен свій край від руки асирійського царя?
34 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
Де боги Гамату та Арпаду? Де боги Сефарваїму, Гени та Івви? Чи врятува́ли вони Самарію від моєї руки?
35 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
Котрий з-поміж усіх богів цих краї́в урятував свій край від моєї руки, — то невже ж Господь уряту́є Єрусалим від моєї руки?“
36 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
І мовчав той наро́д, і не відповів йому ані сло́ва, бо це був нака́з царя, що сказав: „Не відповідайте йому́!“
37 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.
І прийшов Еліяким, син Хілкійї, начальник палати, і писар Шевна, і Йоах, Асафів син, ка́нцлер, із роздертими шатами, до Єзекії, і доне́сли йому слова́ великого чашника.

< 2 Mafumu 18 >