< 2 Mafumu 18 >

1 Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
In the third year of Hoshea, the son of Elah, the king of Israel: Hezekiah, the son of Ahaz, reigned as king of Judah.
2 Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
He was twenty-five years old when he had begun to reign, and he reigned for twenty-nine years in Jerusalem. The name of his mother was Abi, the daughter of Zechariah.
3 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
And he did what was good before the Lord, in accord with all that his father David had done.
4 Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
He destroyed the high places, and he crushed the statues, and he cut down the sacred groves. And he broke apart the bronze serpent, which Moses had made. For even until that time, the sons of Israel were burning incense to it. And he called its name Nehushtan.
5 Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
He hoped in the Lord, the God of Israel. And after him, there was no one similar to him, among all the kings of Judah, nor even among any of those who were before him.
6 Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
And he clung to the Lord, and he did not withdraw from his footsteps, and he carried out his commandments, which the Lord had instructed to Moses.
7 Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
Therefore, the Lord was also with him. And he conducted himself wisely in all the things to which he went forth. Also, he rebelled against the king of the Assyrians, and he did not serve him.
8 Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
He struck the Philistines as far as Gaza, and in all their borders, from the tower of the watchmen to the fortified city.
9 Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
In the fourth year of king Hezekiah, which was the seventh year of Hoshea, the son of Elah, the king of Israel: Shalmaneser, the king of the Assyrians, ascended to Samaria, and he fought against it,
10 Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
and he seized it. For after three years, in the sixth year of Hezekiah, that is, in the ninth year of Hoshea, the king of Israel, Samaria was captured.
11 Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
And the king of the Assyrians took away Israel into Assyria. And he located them in Halah and in Habor, at the rivers of Gozan, in the cities of the Medes.
12 Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
For they did not listen to the voice of the Lord, their God. Instead, they transgressed his covenant. All that Moses, the servant of the Lord, had instructed, they would neither hear, nor do.
13 Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
In the fourteenth year of king Hezekiah, Sennacherib, the king of the Assyrians, went up to all the fortified cities of Judah, and he captured them.
14 Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
Then Hezekiah, the king of Judah, sent messengers to the king of the Assyrians at Lachish, saying: “I have offended. Withdraw from me, and all that you will impose upon me, I will bear.” And so the king of the Assyrians levied a tax upon Hezekiah, the king of Judah, of three hundred talents of silver and thirty talents of gold.
15 Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
And Hezekiah gave all the silver that had been found in the house of the Lord, and in the treasuries of the king.
16 Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
At that time, Hezekiah broke apart the doors of the temple of the Lord, with the plates of gold which he had affixed to them. And he gave these to the king of the Assyrians.
17 Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
Then the king of the Assyrians sent Tartan, and Rabsaris, and Rabshakeh, from Lachish, to king Hezekiah, with a powerful hand, to Jerusalem. And when they had ascended, they arrived in Jerusalem, and they stood beside the aqueduct of the upper pool, which is along the way of the fuller’s field.
18 Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
And they called for the king. But there went out to them Eliakim, the son of Hilkiah, the first ruler of the house, and Shebnah, the scribe, and Joah, the son of Asaph, the keeper of records.
19 Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
And Rabshakeh said to them: “Speak to Hezekiah: Thus says the great king, the king of the Assyrians: What is this faith, in which you strive?
20 Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
Perhaps, you have taken counsel, so that you would prepare yourself for battle. In whom do you trust, so that you would dare to rebel?
21 Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
Do you hope in Egypt, that staff of a broken reed, which, if a man would lean upon it, breaking, it would pierce his hand? Such is Pharaoh, the king of Egypt, to all who would trust in him.
22 Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
But if you say to me: ‘We have faith in the Lord, our God.’ Is it not he, whose high places and altars Hezekiah has taken away? And did he not instruct Judah and Jerusalem: ‘You shall adore before this altar in Jerusalem?’
23 “‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
Now therefore, cross over to my lord, the king of the Assyrians, and I will give to you two thousand horses, and we will see if you even have enough riders for them.
24 Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
So how can you resist one prince from the least of my lord’s servants? Do you have faith in Egypt because of the chariots and horsemen?
25 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
Is it not by the will of the Lord that I have chosen to ascend to this place, so that I may destroy it? The Lord said to me: ‘Ascend to this land, and destroy it.’”
26 Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
Then Eliakim, the son of Hilkiah, and Shebnah, and Joah, said to Rabshakeh: “We beseech you, that you may speak to us, your servants, in Syriac. For we understand that language to some extent. And do not speak to us in the Jews’ language, in the hearing of the people, who are upon the wall.”
27 Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
And Rabshakeh responded to them, saying: “Has my lord sent me to your lord and to you, so that I may speak these words, and not instead to the men who are sitting upon the wall, so that they may eat their own dung, and drink their own urine with you?”
28 Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
And so, Rabshakeh stood up, and he exclaimed in a great voice, in the Jews’ language, and he said: “Listen to the words of the great king, the king of the Assyrians.
29 Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
Thus says the king: Let not Hezekiah lead you astray. For he will not be able to rescue you from my hand.
30 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
And do not let him give you faith in the Lord, saying: ‘The Lord will rescue and free us, and this city will not be delivered into the hand of the king of the Assyrians.’
31 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
Do not choose to listen to Hezekiah. For thus says the king of the Assyrians: Do with me what is for your own good, and come out to me. And each one of you will eat from his own vine, and from his own fig tree. And you shall drink water from your own wells,
32 mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
until I arrive and transfer you into a land, similar to your own land, a fruitful and fertile land of wine, a land of bread and vineyards, a land of olives and oil and honey. And you will live, and not die. Do not choose to listen to Hezekiah, who deceives you, saying: ‘The Lord will free us.’
33 Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
Have any of the gods of the nations freed their land from the hand of the king of Assyria?
34 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
Where is the god of Hamath, and of Arpad? Where is the god of Sepharvaim, of Hena, and of Avva? Have they freed Samaria from my hand?
35 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
Which ones among all the gods of the lands have rescued their region from my hand, so that the Lord would be able to rescue Jerusalem from my hand?”
36 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
But the people were silent, and they did not respond at all to him. For indeed, they had received an instruction from the king that they should not respond to him.
37 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.
And Eliakim, the son of Hilkiah, the first ruler of the house, and Shebnah, the scribe, and Joah, the son of Asaph, the keeper of records, went to Hezekiah with their garments torn. And they reported to him the words of Rabshakeh.

< 2 Mafumu 18 >