< 2 Mafumu 17 >

1 Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
Ngomnyaka wetshumi lambili kaAhazi inkosi yakoJuda uHosheya indodana kaEla waba yinkosi eSamariya phezu kukaIsrayeli; wabusa iminyaka eyisificamunwemunye.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
Wasesenza okubi emehlweni eNkosi, loba kunjalo kungenjengamakhosi akoIsrayeli ayengaphambi kwakhe.
3 Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
UShalimaneseri inkosi yeAsiriya wenyuka wamelana laye; uHosheya wasesiba yinceku yakhe, wathela umthelo kuye.
4 Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
Kodwa inkosi yeAsiriya yafica ugobe kuHosheya, ngoba wayethume izithunywa kuSo inkosi yeGibhithe, kazabe esenyusa umthelo enkosini yeAsiriya umnyaka ngomnyaka. Ngakho inkosi yeAsiriya yamvalela yambopha entolongweni.
5 Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
Inkosi yeAsiriya yasisenyukela kulo lonke ilizwe, yenyukela eSamariya, yayivimbezela iminyaka emithathu.
6 Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
Ngomnyaka wesificamunwemunye kaHosheya, inkosi yeAsiriya yathumba iSamariya yathumbela uIsrayeli eAsiriya, yabahlalisa eHala leHabori, umfula weGozani, lemizini yamaMede.
7 Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
Lokhu-ke kwenzeka ngoba abantwana bakoIsrayeli babonile eNkosini uNkulunkulu wabo eyayibenyuse elizweni leGibhithe ibasusa ngaphansi kwesandla sikaFaro inkosi yeGibhithe, babesabe abanye onkulunkulu,
8 ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
bahamba ezimisweni zezizwe iNkosi eyayizixotshe elifeni phambi kwabantwana bakoIsrayeli, lezamakhosi akoIsrayeli, ayezenzile.
9 Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
Abantwana bakoIsrayeli benza ensitha izinto ezingalunganga bemelene leNkosi uNkulunkulu wabo. Babezakhele indawo eziphakemeyo kuyo yonke imizi yabo, kusukela enqabeni yabalindi kuze kube semzini obiyelweyo.
10 Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Basebezimisela insika eziyizithombe lezixuku phezu kwawo wonke amaqaqa aphakemeyo langaphansi kwaso sonke isihlahla esiluhlaza.
11 Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
Basebetshisa lapho impepha endaweni zonke eziphakemeyo, njengezizwe iNkosi eyazikhokhelela ekuthunjweni phambi kwabo; benza izinto ezimbi ukuyithukuthelisa iNkosi.
12 Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
Ngoba bakhonza izithombe, iNkosi eyayithe ngazo kubo: Kaliyikuyenza linto.
13 Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
Kanti iNkosi yafakaza imelene loIsrayeli njalo imelene loJuda ngesandla sabo bonke abaprofethi lababoni bonke isithi: Phendukani endleleni zenu ezimbi, ligcine imithetho yami, izimiso zami, njengokomlayo wonke engawulaya oyihlo lengawuthumela kini ngesandla senceku zami abaprofethi.
14 Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
Loba kunjalo kabalalelanga, kodwa benza lukhuni intamo yabo, njengentamo yaboyise, abangakholwanga eNkosini uNkulunkulu wabo.
15 Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
Njalo bala izimiso zayo lesivumelwano sayo eyasenza laboyise lezifakazelo zayo eyazifakaza imelene labo, balandela ize, baba yize, balandela izizwe ezazibahanqile, iNkosi eyayibalaye ngazo ukuthi bangenzi njengazo.
16 Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
Bayitshiya yonke imilayo yeNkosi uNkulunkulu wabo, bazenzela izithombe ezibunjwe ngokuncibilikisa, amathole amabili, benza isixuku, bakhothamela lonke ibutho lamazulu, bakhonza uBhali.
17 Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
Benza amadodana abo lamadodakazi abo adabule emlilweni, benza ukuvumisa, benza imilingo, bazithengisela ukwenza okubi emehlweni eNkosi ukuyithukuthelisa.
18 Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
Ngakho iNkosi yamthukuthelela kakhulu uIsrayeli, yabasusa ebusweni bayo; kakusalanga loyedwa ngaphandle kwesizwe sakoJuda kuphela.
19 Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
Laye uJuda kayigcinanga imilayo yeNkosi uNkulunkulu wabo, kodwa bahamba ngezimiso zikaIsrayeli abazenzayo.
20 Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
INkosi yasiyala yonke inzalo yakoIsrayeli, yayihlupha, yayinikela esandleni sabaphangi, yaze yabalahla yabasusa phambi kwayo.
21 Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
Ngoba yamdabula uIsrayeli imsusa endlini kaDavida, basebebeka uJerobhowamu indodana kaNebati ukuthi abe yinkosi. UJerobhowamu wamqhuba wamphambula uIsrayeli ekulandeleni iNkosi, wabenza bona isono esikhulu.
22 Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
Ngoba abantwana bakoIsrayeli bahamba ngazo zonke izono zikaJerobhowamu azenzayo, kabasukanga kuzo,
23 mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
iNkosi yaze yamsusa uIsrayeli phambi kwayo njengokutsho kwayo ngesandla sazo zonke inceku zayo abaprofethi. Ngakho uIsrayeli wathunjwa wasuswa elizweni lakhe wasiwa eAsiriya kuze kube lamuhla.
24 Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
Inkosi yeAsiriya yasiletha abantu abavela eBhabhiloni labavela eKutha labavela eAva labavela eHamathi labavela eSefavayimi, yabahlalisa emizini yeSamariya esikhundleni sabantwana bakoIsrayeli, badla ilifa leSamariya, bahlala emizini yayo.
25 Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
Kwasekusithi ekuqaleni kokuhlala kwabo khona kabayesabanga iNkosi; ngakho iNkosi yathumela izilwane phakathi kwabo ezabulala abanye babo.
26 Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Ngakho bakhuluma enkosini yeAsiriya besithi: Izizwe owazisusayo wazihlalisa emizini yeSamariya kaziwazi umkhuba kaNkulunkulu walelolizwe; ngakho uthumele izilwane phakathi kwazo, khangela-ke ziyazibulala, ngoba kaziwazi umkhuba kaNkulunkulu walelolizwe.
27 Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Inkosi yeAsiriya yasilaya isithi: Yisani khona omunye wabapristi elabathumbayo besuka lapho; kabayehlala khona, kabafundise umkhuba kaNkulunkulu walelolizwe.
28 Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
Ngakho omunye wabapristi ababebathumbe besuka eSamariya weza wahlala eBhetheli, wabafundisa ukuthi bangayesaba njani iNkosi.
29 Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
Loba kunjalo zonke izizwe zenza onkulunkulu bazo, zabafaka ezindlini zezindawo eziphakemeyo amaSamariya azenzayo, yileso laleso isizwe emizini yazo ezihlala kuyo.
30 Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
Labantu beBhabhiloni benza uSukothi-Benothi, labantu beKuthi benza uNerigali, labantu beHamathi benza uAshima,
31 Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
lamaAvi enza uNibazi loTaritaki, lamaSefavayimi ayetshisa abantwana bawo emlilweni esenzela uAdrameleki loAnameleki onkulunkulu beSefavayimi.
32 Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
Babeyesaba leNkosi, bazenzela abapristi bezindawo eziphakemeyo kwabaphansi kakhulu babo, ababebasebenzela ezindlini zezindawo eziphakemeyo.
33 Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
Babeyesaba iNkosi, njalo babekhonza onkulunkulu babo njengomkhuba wezizwe ezabathumbayo besuka lapho.
34 Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
Kuze kube lamuhla benza njengemikhuba yakuqala. Kabayesabi iNkosi, kabenzi njengezimiso zabo lanjengezimiselo zabo lanjengomlayo lanjengomthetho iNkosi eyakulaya abantwana bakaJakobe, owamutha ibizo elithi uIsrayeli.
35 Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
INkosi eyenza isivumelwano labo, yabalaya isithi: Kaliyikwesaba abanye onkulunkulu, lingabakhothameli, lingabasebenzeli, lingabahlabeli.
36 Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
Kodwa iNkosi eyalenyusa elizweni leGibhithe ngamandla amakhulu langengalo eyeluliweyo, yona lizayesaba njalo yona lizayikhothamela njalo yona lizayihlabela.
37 Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
Lezimiso lezimiselo lomlayo lomthetho eyalibhalela khona, lizaqaphelisa ukukwenza zonke izinsuku, lingesabi abanye onkulunkulu.
38 Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
Lesivumelwano engasenza lani lingasikhohlwa, lingesabi abanye onkulunkulu.
39 Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
Kodwa iNkosi uNkulunkulu wenu lizayesaba; yona-ke izalikhulula esandleni sezitha zenu zonke.
40 Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
Loba kunjalo kabalalelanga, kodwa benza njengomkhuba wabo wakuqala.
41 Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.
Lezizizwe zayesaba-ke iNkosi, kodwa zakhonza izithombe zazo ezibaziweyo; bobabili abantwana bazo labantwana babantwana bazo, njengokwenza kwaboyise benza labo kuze kube lamuhla.

< 2 Mafumu 17 >