< 2 Mafumu 17 >

1 Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
En la douzième année du règne d'Achaz, en Juda, Osée, fils d'Ela, commença en Samarie, sur Israël, un règne de neuf ans.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
Et il fit le mal aux yeux du Seigneur, mais non comme les rois d'Israël qui avaient existé avant lui.
3 Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
Salmanasar, roi des Assyriens, marcha contre lui; Osée lui fut asservi, et il lui paya un tribut.
4 Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
Ensuite, Salmanasar trouva en Osée une iniquité, en ce qu'il avait envoyé des messagers à Ségor, roi d'Égypte, et n'avait point payé cette année-là le tribut au roi des Assyriens; et celui-ci l'assiégea et le jeta, enchaîné, dans une prison.
5 Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
Puis, il parcourut toute la terre d'Israël, et monta à Samarie, qu'il assiégea trois ans.
6 Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
Ce fut en la neuvième année du règne d'Osée, que Salmanasar prit Samarie, et transporta Israël en Assyrie, où il l'établit en Hala, en Habor, sur le fleuve Gozan, et sur les montagnes des Mèdes.
7 Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
Et cela arriva, parce que les fils d'Israël avaient péché contre le Seigneur leur Dieu, qui les avait tirés de l'Égypte, et délivrés des mains du roi Pharaon; parce qu'ils avaient craint d'autres dieux.
8 ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
Car ils avaient marché dans les voies des nations que le Seigneur avait exterminées devant les fils d'Israël, et dans celles des rois d'Israël qui avaient fait de tels péchés,
9 Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
Et dans celles des enfants d'Israël, adonnés à des coutumes qui n'étaient point selon le Seigneur leur Dieu; ils s'étaient bâti des hauts lieux en toutes les villes, depuis les tours des guetteurs jusqu'aux cités entourées de remparts.
10 Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Et ils s'étaient dressé des colonnes dans des bois sacrés sur toutes les hautes collines, et sous tous les arbres touffus.
11 Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
Et ils avaient fait des sacrifices sur tous les hauts lieux, comme les nations que le Seigneur avait expulsées de devant leur face; ils avaient formé de honteuses associations, ils avaient gravé des images pour irriter le Seigneur.
12 Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
Et ils avaient servi des idoles au sujet desquelles le Seigneur leur avait dit: Ne faites point cette offense au Seigneur.
13 Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
Cependant, le Seigneur protestait en Israël et en Juda par la bouche de tous ses voyants et de tous ses prophètes, disant: Détournez-vous de vos mauvaises voies, observez mes commandements et mes préceptes; suivez en toutes choses la loi que j'ai donnée à vos pères, et tout ce que je leur ai mandé par mes serviteurs les prophètes.
14 Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
Mais ils ne l'écoutaient point; ils s'endurcissaient le cœur plus que ne l'avaient fait leurs pères.
15 Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
Ils ne gardaient aucun des témoignages que portait le Seigneur; ils marchaient à la suite des vanités, étant vains eux-mêmes; à la suite des nations qui les entouraient, au sujet desquelles le Seigneur leur avait dit: Ne faites pas comme elles.
16 Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
Ils abandonnaient les commandements du Seigneur leur Dieu; ils s'étaient fait deux génisses jetées en fonte; ils plantaient des bois sacrés; ils adoraient toute l'armée du ciel, et ils servaient Baal.
17 Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
Et ils faisaient passer dans la flamme de Moloch leurs fils et leurs filles; ils usaient de la divination et des présages, et ils s'attachaient à faire le mal aux yeux du Seigneur et à l'irriter.
18 Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
Et le Seigneur conçut un grand courroux contre Israël; il le rejeta de devant sa face, et il ne resta que la seule tribu de Juda.
19 Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
Et Juda lui-même n'observa point les commandements du Seigneur son Dieu; il marcha dans les voies d'Israël, et il répudia le Seigneur.
20 Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
Et le Seigneur se courrouça contre toute la race d'Israël; il les ébranla, il les livra à tous ceux qui vinrent les piller, jusqu'à ce. qu'il les rejetât de devant sa face.
21 Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
Il le fit surtout parce qu'Israël ayant rejeté la maison de David, et s'étant donné pour roi Jéroboam, fils de Nabat, Jéroboam entraîna Israël hors des voies du Seigneur, et lui fit commettre un grand péché.
22 Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
Car, les fils d'Israël tombèrent tous dans le péché de Jéroboam, et ils ne s'en retirèrent point,
23 mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
Jusqu'à ce que le Seigneur eût expulsé Israël de devant sa face, comme il l'en avait menacé par la voix de tous ses serviteurs les prophètes. Et Israël fut emmené en la terre des Assyriens, où il est encore de nos jours.
24 Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
Ensuite, le roi des Assyriens amena des hommes de Babylone, de Chuth, d'Aïa, d'Emath, de Sepharvaïm, et il les établit en Samarie à la place des fils d'Israël; ils se partagèrent son territoire, et ils demeurèrent dans ses villes.
25 Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
Dans les premiers temps de leur séjour, ils ne craignaient point le Seigneur, et le Seigneur envoya contre eux des lions qui en tuèrent quelques- uns.
26 Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Ils le firent savoir au roi des Assyriens, disant: Les nations que tu as transportées et assises dans les villes de Samarie, ne connaissaient point les jugements du Dieu de cette terre; et il a envoyé contre eux des lions; et voilà que ces lions les tuent, parce qu'ils ne savent pas les jugements du Dieu de cette terre.
27 Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Et le roi des Assyriens donna ses ordres, disant: Emmenez d'ici des gens, qu'ils partent, qu'ils demeurent avec vous; ils vous éclaireront sur les jugements du Dieu de cette terre.
28 Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
Et ils emmenèrent un des prêtres qu'on avait transportés de Samarie; il s'établit à Béthel; il les éclaira, et il leur apprit comme ils devaient craindre le Seigneur.
29 Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
Mais, chaque nation fabriqua ses dieux; on les plaça dans les temples des hauts lieux que les Samaritains avaient construits; chaque nation eut les siens dans les villes qu'elle habitait.
30 Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
Ceux de Babylone avaient fabriqué Soccoth-Benith; ceux de Chuth, Ergel; ceux d'Emath, Asimath;
31 Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
Les Evéens fabriquèrent Eblazer et Tharthac; ceux de Sepharvaïm firent le mal quand ils brûlèrent leurs fils dans les flammes d'Adra-Moloch et d'Ana- Moloch, leurs dieux.
32 Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
Ils craignaient le Seigneur; mais ils avaient établi leurs abominations dans les temples des hauts lieux qu'avaient construits les Samaritains, chacun dans la ville que sa nation habitait; ils craignaient le Seigneur; mais ils avaient institué pour eux des prêtres des hauts lieux, et ils sacrifiaient dans les temples des hauts lieux.
33 Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
Ils craignaient le Seigneur, mais ils servirent leurs dieux selon l'usage des nations dont ils avaient été tirés.
34 Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
Jusqu'à ce jour, ils ont agi selon leurs usages; les mêmes gens craignent le Seigneur et agissent selon leurs mœurs, selon leurs usages, et en même temps selon la loi et les préceptes que le Seigneur a donnés aux fils de Jacob, qu'il a appelé aussi Israël;
35 Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
Avec qui le Seigneur fit jadis alliance, disant: Vous ne craindrez point d'autres dieux, vous ne les adorerez pas, vous ne les servirez point, vous ne leur ferez point de sacrifices.
36 Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
Vous ne craindrez, vous n'adorerez, vous n'honorerez par des sacrifices que le Seigneur qui vous a ramenés d'Égypte par sa toute-puissance, et par son bras très-haut.
37 Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
Vous observerez toujours les ordonnances, les jugements, la loi et les commandements qu'il a écrits, pour que vous les pratiquiez; vous ne craindrez point d'autres dieux.
38 Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
Et vous n'abandonnerez point l'alliance qu'il a faite avec vous, et vous ne craindrez point d'autres dieux;
39 Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
Vous ne craindrez que le Seigneur votre Dieu, et il vous délivrera de tous vos ennemis;
40 Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
Vous ne suivrez point les pratiques que suivent les Gentils.
41 Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.
Ces nations nouvelles craignaient donc le Seigneur, et elles servaient leurs idoles; et leurs fils, et les fils de leurs fils, ont fait comme leurs pères jusqu'à nos jours.

< 2 Mafumu 17 >