< 2 Mafumu 17 >

1 Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
Idet tolvte Akas's, Judas Konges, Aar blev Hosea, Elas Søn, Konge i Samaria over Israel i ni Aar.
2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
Og han gjorde det, som var ondt for Herrens Øjne, dog ikke som Israels Konger, som vare før ham.
3 Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
Salmanasser, Kongen af Assyrien, drog op imod ham; og Hosea blev hans Tjener og gav ham Skænk.
4 Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
Men Kongen af Assyrien saa et Forbund deri, at Hosea havde sendt Bud til So, Kongen af Ægypten, og ikke bragt Skat til Kongen af Assyrien Aar for Aar; da satte Kongen af Assyrien ham fast og lagde ham bunden i et Fængsel.
5 Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
Thi Kongen af Assyrien drog op i det ganske Land og drog op til Samaria og belejrede den i tre Aar.
6 Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
I Hoseas niende Aar indtog Kongen af Assyrien Samaria og førte Israel bort til Assyrien; og han lod dem bo i Hala og i Habor ved Floden Gosan og i Medernes Stæder.
7 Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
Og det skete, fordi Israels Børn havde syndet imod Herren deres Gud, som havde ført dem op af Ægyptens Land, fra at være under Faraos, Kongen af Ægyptens, Magt, og fordi de frygtede andre Guder;
8 ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
og de vandrede i de Hedningers Skikke, hvilke Herren havde fordrevet for Israels Børns Ansigt, og i dem, som Israels Konger havde indført;
9 Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
og Israels Børn skjulte Ting, som ikke var ret for Herren deres Gud og byggede sig Høje i alle Stæder, fra Vogternes Taarn indtil hver fast Stad;
10 Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
og de oprejste sig Støtter og Astartebilleder paa hver ophøjet Høj og under hvert grønt Træ;
11 Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
og de gjorde Røgelse der paa alle Højene ligesom Hedningerne, hvilke Herren havde bortført fra deres Ansigt, og de gjorde onde Ting til at opirre Herren;
12 Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
og de tjente de stygge Afguder, om hvilke Herren havde sagt til dem: I skulle ikke gøre denne Ting;
13 Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
og Herren lod vidne i Israel og i Juda ved alle sine Profeter, alle Seere, sigende: Vender om fra eders onde Veje og holder mine Bud, mine Skikke, efter den hele Lov, som jeg bød eders Fædre, og efter det, som jeg sendte til eder om ved mine Tjenere, Profeterne;
14 Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
men de havde ikke været lydige, men de forhærdede deres Nakke, ligesom deres Fædres Nakke, de, som ikke troede paa Herren deres Gud;
15 Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
tilmed forkastede de hans Skikke og hans Pagt, som han havde gjort med deres Fædre, og hans Vidnesbyrd, som han havde vidnet for dem, og de vandrede efter Forfængelighed og bleve forfængelige, og efter Hedningerne, der vare trindt omkring dem, om hvilke Herren havde budet dem, at de ikke skulde gøre som de;
16 Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
ja de forlode alle Herren deres Guds Bud og gjorde sig støbte Billeder, to Kalve, og de gjorde Astartebilleder og tilbade al Himmelens Hær og tjente Baal;
17 Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
og de lode deres Sønner og deres Døtre gaa igennem Ilden og omgikkes med Spaadom og agtede paa Fugleskrig og solgte sig til at gøre det, som var ondt for Herrens Øjne, for at opirre ham: —
18 Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
derfor blev Herren saare vred paa Israel og bortdrev dem fra sit Ansigt; der blev ingen tilovers uden Judas Stamme alene.
19 Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
Heller ikke Juda holdt Herrens, deres Guds, Bud; men de vandrede efter Israels Skikke, som de havde indført.
20 Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
Saa forkastede Herren al Israels Sæd og plagede dem og gav dem i Røveres Hænder, indtil han havde bortstødt dem fra sit Ansigt.
21 Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
Thi Israel havde revet sig løs fra Davids Hus, og de gjorde Jeroboam, Nebats Søn, til Konge; og Jeroboam drog Israel bort fra Herren og kom dem til at synde en stor Synd.
22 Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
Og Israels Børn vandrede i alle Jeroboams Synder, som han gjorde; de vege ikke derfra,
23 mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
indtil Herren bortdrev Israel fra sit Ansigt, saaledes som han havde sagt ved alle sine Tjenere, Profeterne; saa blev Israel bortført fra sit Land til Assyrien indtil denne Dag.
24 Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
Og Kongen af Assyrien lod komme Folk af Babel og af Kut og af Ava og af Hamath og Sefarvajm og lod dem bo i Samarias Stæder, i Israels Børns Sted, og de indtoge Samaria til Ejendom og boede i dens Stæder.
25 Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
Og det skete, der de begyndte at bo der, at de ikke frygtede Herren; da sendte Herren Løver iblandt dem, og disse sønderreve nogle af dem.
26 Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Derfor sagde de til Kongen af Assyrien: De Hedninger, som du lod forflytte og bo i Samarias Stæder, kende ikke, hvad der er ret imod Landets Gud; derfor sendte han Løver iblandt dem, og se, disse sønderreve dem, fordi de ikke kende, hvad der er ret imod Landets Gud.
27 Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
Da bød Kongen af Assyrien og sagde: Fører en af de Præster derhen, som I bortførte derfra, og lader ham drage hen og bo der, at han kan lære dem, hvad der er ret imod Landets Gud.
28 Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
Saa kom en af Præsterne, som de havde bortført fra Samaria, og boede i Bethel og lærte dem, hvorledes de skulde frygte Herren.
29 Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
Men hvert Folk gjorde sig sin Gud, og de satte dem i Husene paa de Høje, som Samaritanerne gjorde, hvert Folk i sine Stæder, hvori de boede.
30 Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
Thi de Mænd af Babel havde gjort Sukoth-Benoth, og de Mænd af Kut havde gjort Nergal, og de Mænd af Hamath havde gjort Asima,
31 Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
og de al Ava havde gjort Nibhas og Tharthak, og de af Sefarvajm opbrændte deres Sønner i Ilden for Adramelek og Anamelek, Sefarvajms Guder.
32 Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
De frygtede ogsaa Herren og gjorde sig i Flæng Præster paa Højene og gjorde Offer for dem i Husene paa Højene.
33 Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
De frygtede Herren, og de tjente deres Guder efter de Hedningers Vis, som de vare bortførte fra.
34 Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
De gøre efter den første Vis, indtil denne Dag; de frygte ikke Herren, ej heller gøre de efter deres Skikke og efter deres Befalinger og efter Loven og efter Budet, som Herren bød Jakobs Børn, hvis Navn han kaldte Israel;
35 Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
og Herren gjorde en Pagt med dem og bød dem, sigende: I skulle ikke frygte andre Guder og ikke tilbede dem og ikke tjene dem og ikke ofre til dem.
36 Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
Men Herren, som førte eder op af Ægyptens Land med stor Kraft og med en udrakt Arm, ham skulle I frygte, og ham skulle I tilbede og ofre til.
37 Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
Og I skulle holde de Skikke og Befalinger og Loven og Budet, som han lod skrive for eder, at gøre derefter alle Dage; men I skulle ikke frygte andre Guder.
38 Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
Og I skulle ikke forglemme den Pagt, som jeg gjorde med eder, og ikke frygte andre Guder.
39 Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
Men I skulle frygte Herren eders Gud, og han skal fri eder fra alle eders Fjenders Haand.
40 Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
Dog, de hørte ikke; men de gjorde efter deres første Vis.
41 Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.
Saa frygtede disse Hedninger Herren og tjente deres Billeder; ogsaa deres Børn og deres Børnebørn, efter som deres Fædre gjorde, saa gøre de indtil denne Dag.

< 2 Mafumu 17 >