< 2 Mafumu 16 >

1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
La dix-septième année de Phacée, fils de Romélias, régna Achaz, fils de Joatham, roi de Juda.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Achaz avait vingt ans lorsqu’il devint roi, et il régna seize ans à Jérusalem. Il ne fit pas ce qui est droit aux yeux de Yahweh, son Dieu, comme avait fait David, son père.
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
Mais il marcha dans la voie des rois d’Israël, et même il fit passer son fils par le feu, selon les abominations des nations que Yahweh avait chassées devant les enfants d’Israël.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Il offrait des sacrifices et des parfums aux hauts lieux, sur les collines et sous tout arbre vert.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
Alors Rasin, roi de Syrie, et Phacée, fils de Romélias, roi d’Israël, montèrent contre Jérusalem pour l’attaquer. Ils assiégèrent Achaz, mais ils ne purent pas le vaincre.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
Dans ce même temps, Rasin, roi de Syrie, ramena Elath au pouvoir des Syriens; il expulsa les Juifs d’Elath, et les Syriens vinrent à Elath, où ils ont habité jusqu’à ce jour.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
Achaz envoya des messagers à Téglathphalasar, roi d’Assyrie, pour lui dire: « Je suis ton serviteur et ton fils; monte et délivre-moi de la main du roi de Syrie et de la main du roi d’Israël, qui se sont levés contre moi. »
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
Et Achaz prit l’argent et l’or qui se trouvaient dans la maison de Yahweh et dans les trésors de la maison du roi, et il l’envoya en présent au roi d’Assyrie.
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
Le roi d’Assyrie l’écouta, et le roi d’Assyrie monta contre Damas et, l’ayant prise, il en emmena les habitants en captivité à Qir, et il fit mourir Rasin.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
Le roi Achaz se rendit à Damas au-devant de Téglathphalasar, roi d’Assyrie. Ayant vu l’autel qui était à Damas, le roi Achaz envoya au prêtre Urias le modèle de l’autel et sa forme selon tout son travail.
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
Le prêtre Urias construisit l’autel; le prêtre Urias le fit entièrement d’après le modèle que le roi Achaz avait envoyé de Damas, avant que le roi ne revienne de Damas.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
A son arrivée de Damas, le roi vit l’autel. Le roi s’approcha de l’autel et il y monta;
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
il fit brûler son holocauste et son oblation, versa sa libation, et répandit sur l’autel le sang de ses sacrifices pacifiques.
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
Il éloigna de devant la maison, d’entre le nouvel autel et la maison de Yahweh, l’autel d’airain qui était devant Yahweh, et il le plaça à côté du nouvel autel, vers le nord.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
le roi Achaz donna encore cet ordre au prêtre Urias: « Fais brûler sur le grand autel l’holocauste du matin et l’oblation du soir, l’holocauste du roi et son oblation, l’holocauste de tout le peuple du pays et leur oblation, verses-y leur libation et répands-y tout le sang des holocaustes et tout le sang des sacrifices. Pour ce qui concerne l’autel d’airain, il m’appartiendra d’y pourvoir. »
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
Le prêtre Urias fit tout ce qu’avait ordonné le roi Achaz.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
En outre, le roi Achaz brisa les cadres et les bases, et ôta les bassins qui étaient dessus; il descendit la mer d’airain de dessus les bœufs d’airain qui la supportaient, et il la posa sur un pavé de pierres;
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
il changea, dans la maison de Yahweh, par considération pour le roi d’Assyrie, le portique du sabbat, qu’on avait construit dans la maison, et l’entrée extérieure du roi.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Le reste des actes d’Achaz, et tout ce qu’il a fait, cela n’est-il pas écrit dans le livre des Chroniques des rois de Juda?
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Achaz se coucha avec ses pères, et il fut enterré avec ses pères dans la cité de David. Ezéchias, son fils, régna à sa place.

< 2 Mafumu 16 >