< 2 Mafumu 16 >

1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
in/on/with year seven ten year to/for Pekah son: child Remaliah to reign Ahaz son: child Jotham king Judah
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
son: aged twenty year Ahaz in/on/with to reign he and six ten year to reign in/on/with Jerusalem and not to make: do [the] upright in/on/with eye: appearance LORD God his like/as David father his
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
and to go: walk in/on/with way: conduct king Israel and also [obj] son: child his to pass in/on/with fire like/as abomination [the] nation which to possess: take LORD [obj] them from face: before son: descendant/people Israel
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
and to sacrifice and to offer: offer in/on/with high place and upon [the] hill and underneath: under all tree luxuriant
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
then to ascend: rise Rezin king Syria and Pekah son: child Remaliah king Israel Jerusalem to/for battle and to confine upon Ahaz and not be able to/for to fight
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
in/on/with time [the] he/she/it to return: rescue Rezin king Syria [obj] Elath to/for Syria and to slip [obj] [the] Jew from Eloth (and Edomite *Q(K)*) to come (in): come Elath and to dwell there till [the] day: today [the] this
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
and to send: depart Ahaz messenger to(wards) Tiglath-pileser Tiglath-pileser king Assyria to/for to say servant/slave your and son: child your I to ascend: rise and to save me from palm king Syria and from palm king Israel [the] to arise: attack upon me
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
and to take: take Ahaz [obj] [the] silver: money and [obj] [the] gold [the] to find house: temple LORD and in/on/with treasure house: home [the] king and to send: depart to/for king Assyria bribe
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
and to hear: hear to(wards) him king Assyria and to ascend: rise king Assyria to(wards) Damascus and to capture her and to reveal: remove her Kir [to] and [obj] Rezin to die
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
and to go: went [the] king Ahaz to/for to encounter: meet Tiglath-pileser Tiglath-pileser king Assyria Damascus and to see: see [obj] [the] altar which in/on/with Damascus and to send: depart [the] king Ahaz to(wards) Uriah [the] priest [obj] likeness [the] altar and [obj] pattern his to/for all deed: work his
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
and to build Uriah [the] priest [obj] [the] altar like/as all which to send: depart [the] king Ahaz from Damascus so to make Uriah [the] priest till to come (in): come [the] king Ahaz from Damascus
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
and to come (in): come [the] king from Damascus and to see: see [the] king [obj] [the] altar and to present: come [the] king upon [the] altar and to ascend: offer up upon him
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
and to offer: burn [obj] burnt offering his and [obj] offering his and to pour [obj] drink offering his and to scatter [obj] blood [the] peace offering which to/for him upon [the] altar
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
and [obj] [the] altar [the] bronze which to/for face: before LORD and to present: come from with face: before [the] house: home from between [the] altar and from between house: temple LORD and to give: put [obj] him upon thigh [the] altar north [to]
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
(and to command *Q(K)*) [the] king Ahaz [obj] Uriah [the] priest to/for to say upon [the] altar [the] great: large to offer: burn [obj] burnt offering [the] morning and [obj] offering [the] evening and [obj] burnt offering [the] king and [obj] offering his and [obj] burnt offering all people [the] land: country/planet and offering their and drink offering their and all blood burnt offering and all blood sacrifice upon him to scatter and altar [the] bronze to be to/for me to/for to enquire
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
and to make: do Uriah [the] priest like/as all which to command [the] king Ahaz
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
and to cut [the] king Ahaz [obj] [the] perimeter [the] base and to turn aside: remove from upon them ([obj] *Q(K)*) [the] basin and [obj] [the] sea to go down from upon [the] cattle [the] bronze which underneath: under her and to give: put [obj] him upon pavement stone
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
and [obj] (portico *Q(K)*) [the] Sabbath which to build in/on/with house: home and [obj] entrance [the] king [the] outer to turn: surround house: temple LORD from face: because king Assyria
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
and remainder word: deed Ahaz which to make: do not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Judah
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
and to lie down: be dead Ahaz with father his and to bury with father his in/on/with city David and to reign Hezekiah son: child his underneath: instead him

< 2 Mafumu 16 >