< 2 Mafumu 16 >

1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
In the seventeenth year of Pekah son of Remaliah, Ahaz son of Jotham, king of Judah, has reigned.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Ahaz [is] a son of twenty years in his reigning, and he has reigned sixteen years in Jerusalem, and he has not done that which [is] right in the eyes of his God YHWH, like his father David,
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
and he walks in the way of the kings of Israel, and he has also caused his son to pass over into fire, according to the abominations of the nations that YHWH dispossessed from the presence of the sons of Israel,
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
and he sacrifices and makes incense in high places, and on the heights, and under every green tree.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
Then Rezin king of Aram, and Pekah son of Remaliah, king of Israel, go up to Jerusalem, to battle, and they lay siege to Ahaz, and they have not been able to fight.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
At that time Rezin king of Aram has brought back Elath to Aram, and casts out the Jews from Elath, and the Arameans have come to Elath, and dwell there to this day.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
And Ahaz sends messengers to Tiglath-Pileser king of Asshur, saying, “I [am] your servant and your son; come up and save me out of the hand of the king of Aram, and out of the hand of the king of Israel, who are rising up against me.”
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
And Ahaz takes the silver and the gold that is found in the house of YHWH, and in the treasures of the house of the king, and sends to the king of Asshur [as] a bribe.
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
And the king of Asshur listens to him, and the king of Asshur goes up to Damascus, and seizes it, and removes [the people of] it to Kir, and he has put Rezin to death.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
And King Ahaz goes to meet Tiglath-Pileser king of Asshur [at] Damascus, and sees the altar that [is] in Damascus, and King Ahaz sends to Urijah the priest the likeness of the altar, and its pattern, according to all its work,
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
and Urijah the priest builds the altar according to all that King Ahaz has sent from Damascus; so Urijah the priest did until the coming in of King Ahaz from Damascus.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
And the king comes in from Damascus, and the king sees the altar, and the king draws near on the altar, and offers on it,
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
and burns his burnt-offering and his present as incense, and pours out his drink-offering, and sprinkles the blood of the peace-offerings that he has, on the altar.
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
As for the altar of bronze that [is] before YHWH—he brings [it] near from the front of the house, from between the altar and the house of YHWH, and puts it on the side of the altar, northward.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
And King Ahaz commands him—Urijah the priest—saying, “On the great altar burn as incense the burnt-offering of the morning, and the present of the evening, and the burnt-offering of the king, and his present, and the burnt-offering of all the people of the land, and their present, and their drink-offerings; and all the blood of the burnt-offering, and all the blood of the sacrifice, you sprinkle on it, and the altar of bronze is for me to inquire [by].”
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
And Urijah the priest does according to all that King Ahaz commanded.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
And King Ahaz cuts off the borders of the bases, and turns aside the laver from off them, and he has taken down the sea from off the bronze oxen that [are] under it, and puts it on a pavement of stones.
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
And the covered place for the Sabbath that they built in the house, and the entrance of the king outside, he turned [from] the house of YHWH, because of the king of Asshur.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
And the rest of the matters of Ahaz that he did, are they not written on the scroll of the Chronicles of the Kings of Judah?
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Ahaz lies with his fathers, and is buried with his fathers in the City of David, and his son Hezekiah reigns in his stead.

< 2 Mafumu 16 >