< 2 Mafumu 16 >
1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
The seuenteenth yeere of Pekah the sonne of Remaliah, Ahaz the sonne of Iotham King of Iudah began to reigne.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Twentie yeere olde was Ahaz, when hee began to reigne, and he reigned sixteene yeere in Ierusalem, and did not vprightly in the sight of the Lord his God, like Dauid his father:
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
But walked in the way of ye kings of Israel, yea, and made his sonne to go through the fire, after the abominations of the heathen, whom the Lord had cast out before the children of Israel.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Also he offred and burnt incense in the hie places and on the hilles, and vnder euery greene tree.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
Then Rezin king of Aram and Pekah sonne of Remaliah King of Israel came vp to Ierusalem to fight: and they besieged Ahaz, but could not ouercome him.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
At the same time Rezin king of Aram restored Elath to Aram, and droue the Iewes from Elath: so the Aramites came to Elath, and dwelt there vnto this day.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
Then Ahaz sent messengers to Tiglath Pileser king of Asshur, saying, I am thy seruant and thy sonne: come vp, and deliuer me out of the hand of the king of Aram, and out of the hand of the King of Israel which rise vp against me.
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
And Ahaz tooke the siluer and the golde that was found in the house of the Lord, and in the treasures of the Kings house, and sent a present vnto the King of Asshur.
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
And the King of Asshur consented vnto him: and the King of Asshur went vp against Damascus. and when he had taken it, he caryed the people away to Kir, and slew Rezin.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
And King Ahaz went vnto Damascus to meete Tiglath Pileser King of Asshur: and when King Ahaz sawe the altar that was at Damascus, he sent to Vriiah the Priest the paterne of the altar, and the facion of it, and all the workemanship thereof.
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
And Vriiah the Priest made an altar in al poyntes like to that which King Ahaz had sent from Damascus, so did Vriiah the Priest against King Ahaz came from Damascus.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
So when the King was come from Damascus, the King sawe the altar: and the King drewe neere to the altar and offered thereon.
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
And hee burnt his burnt offering, and his meate offring, and powred his drinke offring, and sprinkled the blood of his peace offrings besides the altar,
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
And set it by the brasen altar which was before the Lord, and brought it in farther before the house betweene the altar and the house of the Lord, and set it on the North side of the altar.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
And King Ahaz commanded Vriiah the Priest, and sayde, Vpon the great altar set on fire in the morning the burnt offring, and in the euen the meate offring, and the Kings burnt offring and his meate offering, with the burnt offring of all the people of the lande, and their meate offring, and their drinke offrings: and powre thereby all the blood of the burnt offring, and all the blood of the sacrifice, and the brasen altar shalbe for me to inquire of God.
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
And Vriiah the Priest did according to all that King Ahaz had commanded.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
And King Ahaz brake the borders of the bases, and tooke the caldrons from off them, and tooke downe the sea from the brasen oxen that were vnder it, and put it vpon a pauement of stones.
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
And the vaile for the Sabbath (that they had made in the house) and the Kings entrie without turned he to the house of the Lord, because of the King of Asshur.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Concerning the rest of the actes of Ahaz, which he did, are they not written in the booke of the Chronicles of the Kings of Iudah?
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Ahaz slept with his fathers, and was buryed with his fathers in the citie of Dauid, and Hezekiah his sonne reigned in his steade.