< 2 Mafumu 16 >

1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
In the seventeenth year of Phacee the son of Romelia reigned Achaz the son of Joatham king of Juda.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Achaz was twenty years old when he began to reign, and he reigned sixteen years in Jerusalem: he did not that which was pleasing in the sight of the Lord his God, as David his father.
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
But he walked in the way of the kings of Israel: moreover he consecrated also his son, making him pass through the fire according to the idols of the nations: which the Lord destroyed before the children of Israel.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
He sacrificed also and burnt incense in the high places and on the hills, and under every green tree.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
Then Basin king of Syria, and Phacee son of Romelia king of Israel came up to Jerusalem to fight: and they besieged Achaz, but were not able to overcome him.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
At that time Rasin king of Syria restored Aila to Syria, and drove the men of Juda out of Aila: and the Edomites came into Aila, and dwelt there unto this day.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
And Achaz sent messengers to Theglathphalasar king of the Assyrians, saying: I am thy servant, and thy son: come up, and save me out of the hand of the king of Syria, and out of the hand of the king of Israel, who are risen up together against me.
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
And when he had gathered together the silver and gold that could be found in the house of the Lord, and in the king’s treasures, he sent it for a present to the king of the Assyrians.
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
And he agreed to his desire: for the king of the Assyrians went up against Damascus, and laid it waste: and he carried away the inhabitants thereof to Cyrene, but Basin he slew.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
And king Achaz went to Damascus to meet Theglathphalasar king of the Assyrians, and when he had seen the altar of Damascus, king Achaz sent to Urias the priest a pattern of it, and its likeness according to all the work thereof.
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
And Urias the priest built an altar according to all that king Achaz had commanded from Damascus, so did Urias the priest, until king Achaz came from Damascus.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
And when the king was come from Damascus, he saw the altar and worshipped it: and went up and offered holocausts, and his own sacrifice.
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
And offered libations and poured the blood of the peace offerings, which he had offered upon the altar.
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
But the altar of brass that was before the Lord, he removed from the face of the temple, and from the place of the altar, and from the place of the temple of the Lord: and he set it at the side of the altar toward the north.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
And king Achaz commanded Urias the priest saying: Upon the great altar offer the morning holocaust, and the evening sacrifice, and the king’s holocaust, and his sacrifice, and the holocaust of the whole people of the land, and their sacrifices, and their libations: and all the blood of the holocaust, and all the blood of the victim thou shalt pour out upon it: but the altar of brass shall be ready at my pleasure.
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
So Urias the priest did according to all that king Achaz had commanded him.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
And king Achaz took away the graven bases, and the laver that was upon them: and he took down the sea from the brazen oxen that held it up, and put it upon a pavement of stone.
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
The Musach also for the sabbath, which he had built in the temple: and the king’s entry from without he turned into the temple of the Lord, because of the king of the Assyrians.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Now the rest of the acts of Achaz, which he did, are they not written in the book of the words of the days of the kings of Juda?
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Achaz slept with his fathers, and was buried with them in the city of David, and Ezechias his son reigned in his stead.

< 2 Mafumu 16 >